100% found this document useful (3 votes)
2K views

Maliro Ndi Miyambo Ya Chewa

This document summarizes several Achewa traditions and mourning practices related to childbirth and childhood deaths in under 3 sentences. It discusses: 1) Traditions surrounding a woman giving birth, including prohibitions on the husband and restrictions during mourning. 2) Common causes of infant mortality like lack of nutrition and traditional practices like giving babies herbs. 3) Mourning rituals like waking the village leader, building shelters, and prohibitions on the family during mourning.

Uploaded by

Ephrate
Copyright
© © All Rights Reserved
We take content rights seriously. If you suspect this is your content, claim it here.
Available Formats
Download as PDF, TXT or read online on Scribd
100% found this document useful (3 votes)
2K views

Maliro Ndi Miyambo Ya Chewa

This document summarizes several Achewa traditions and mourning practices related to childbirth and childhood deaths in under 3 sentences. It discusses: 1) Traditions surrounding a woman giving birth, including prohibitions on the husband and restrictions during mourning. 2) Common causes of infant mortality like lack of nutrition and traditional practices like giving babies herbs. 3) Mourning rituals like waking the village leader, building shelters, and prohibitions on the family during mourning.

Uploaded by

Ephrate
Copyright
© © All Rights Reserved
We take content rights seriously. If you suspect this is your content, claim it here.
Available Formats
Download as PDF, TXT or read online on Scribd
You are on page 1/ 86

Maliro ndi Miyambo ya Achewa, Bukhu

la Chiwiri

Archibald J. Makumbi

Malawi National Commission for UNESCO


All rights reserved. No part of this publication may be reproduced, stored in a
retrieval system, or transmitted in any form or by any means, electronic,
mechanical, photocopying, recording, or otherwise, without the prior written
permission of the copyright owner.

Chiyamiko
Ndiyamika Boma la Malawi pondilola kulemba bukuli, makamaka Bungwe lija la
‘African Book Selection Committee, pondichitira chifundo.

Zikomo kwa Rev. Amoni Dembo Mvula amene adalola kundiuza zina zakale,
ndikutinso adandilimbikitsa pamene ndidayamba kufooka.

Mayamiko anga apitenso kwa akulu a DRCM Nkhoma, amene adandilola kukaona
ku chipinda chosungira zakale.

Ndiyamikanso bwenzi langa Norman L Nkomba pondithandiza kulemba bukuli.


Zikomonso kwa onse amene adandithandiza pa zina.

AJ Makumbi

Zithunzi zina zidajambulidwa ndi JE Chande kuonjezera pa zimene adajambula


mlembi wa bukuli; koma zina a M Yeta adangotsanzira zimene adajambula
mlembi.

1
Zam’kati
Mawu oyamba Tsamba
1 Maliro a mwana wofera m’chikuta
2 Mwana wamasiku kapena miyezi
3 Mwana wamtengwa
4 Kubadwa kwa mwana*
5 Mwana woyamba kumera mano kumwamba
6 Maleredwe a ana a Achewa
7 Mwana wamasiye
8 Mnyamata
9 Mayi wolowa kudambwe*
10 Mayina a gule wamkulu*
11 Mtsikana akapeza bwenzi*
12 Chinamwali
13 Namwali akatha msinkhu
14 Mkazi wachitengwa
15 Mkazi akakhala ndipakati
16 Maliro a mkazi wosiya mwana pobereka
17 Munthu wakhate
18 Munthu wodwala nthomba
19 Uzimba
20 Kapolo
21 Za ufiti, mankhwala ndi matsenga
22 Masasa
23 Munthu wofa ndi mankhwala
24 Maliro a munthu womwa mwavi
25 Maliro a munthu wachuma
26 Munthu wophedwa mwangozi
27 Maliro a munthu wofa mwadzidzidzi
28 Maliro a munthu wakhunyu
29 Munthu wopsa ndi moto
30 Munthu wodzipha yekha

2
31 Maliro a chitsiru
32 Mdulo (tsempho)
33 Maliro a mkamwini
34 Maliro a namkungwi
35 Maliro a nduna ya mfumu
36 Maliro a mfumu ya mzinda
37 Ufumu wa Achewa*
38 Mawu otsiriza
38

3
Mawu oyamba
Cholembera bukuli n’choti tilondole za miyambo ya Achewa kuti mbiriyi
isungidwe kuti ana am’tsogolo adzaidziwe.

Anthu a mu Africa ambiri ndiwo ‘Abantu’ amene amakhala kumwera, kuvuma ndi
kuzambwe kwa Africa.

Mbiri ya dziko la Africa idadziwika kalekale, Ambuye asanabadwe, monga nthawi


ija ya Aisaraeli ndi Mfumu Farao. Ndiponso mbiri ya chitukuko cha makhalidwe
olongosoka (Civilization) idayambira kumpoto kwa Africa (Egipito). Koma
chifukwa cha chipululu chamchenga akumwera, kuvuma ndi kuzambwe
sadalandire chitukukochi, chidaoloka nyanja yaikulu n’kukafika ku Mesopotamia
(Babuloni) ndi maiko ena a ku Europe.

Abantu posadziwa za makhalidwe olongosoka ndi Mulungu woona adakhulupirira


zaufiti, matsenga, mdulo, ndiponso adakhulupirira kuti mzimu wa amene adafa
kale ungathe kupha munthu wamoyo ngati sakhulupirira kapena kusamala
miyambo.

Ndipo popeza kuti Achewa ndi limodzi mwamagulu a mtundu wa Abantu, ndifuna
kulondola maliro ndi miyambo ya Achewa, ndi mmene iwo amasamalira
miyamboyo.

Pokhala kuti mtundu uliwonse umayamba pa mwana, tidzayamba za mwana


mpaka za wamkulu.

4
Cholinga cha bukuli
Ganizo loti ndilembe bukuli litandifikira ndidaganiza kuti ndidayenera kuyamba
ndalowa kudambwe kuti ndidziwe zambiri za gule wamkulu. Ndipo ndisadalowe
ndidayambabe kulemba bukuli ngakhale mfundo zake zidali zogendagenda.
Nthawiyi idali chaka cha 1946 ndipo bukuli lidatuluka 1948, ndipo wolisindikiza
adali a Longman – Green Company Limited ku United Kingdom. Bukuli litatuluka
mafumu a mzinda adakhumudwa nalo ndipo zotsatira zake zidali zogula mabuku
onse ndi kuwatentha, motero padali adani awiri, mpingo ndi amizinda. Pofuna kuti
ndidziwe kwambiri za gule wamkulu ndidapempha chilolezo kumpingo wanga kuti
ndilowe kudambwe koma adandikaniza koma popeza ndidali ndi cholinga,
m’chaka cha 1970 ndidakalowabe kudambwe. Mosataya nthawi ndidaphunzira
zambiri panthawi yochepa ndipo ndidatulukako m’chaka cha 1980.

Ndidakadzipereka kumpingo kuti andiimitse pa zampingo. N’talongosola


ndidapitirira ndi zolinga zanga poti tsopano ndidalibe mlandu. Patangopita
kanthawi ndili kuonerera gule wamasana, mpingo udandipeza wolakwa
n’kundidula mumpingo. A boma atafufuza adapeza kuti bukuli si loyenera
kumagwiritsa ntchito ku sukulu zapulayimale koma zasekondale zokha. Pamathero
pozindikira zonsezi, bukuli lidavomerezedwa ndi Unduna wa za Maphunziro kuti
ndi lofunika. Gule wamkulu si chipembedzo ayi koma miyambo ya mtundu wa
Achewa panthawi yapamaliro ndiponso pometa anamwali. Nyengo yake ndi
nthawi yachilimwe yokhayokha.

Mpingo utanthauza gulu la anthu lochitira zinthu limodzi mogwirizana motero


mpingo si Chikhirisitu chokha ayi, angakhale nyawu ndi mpingonso ‘church
culture’. Kodi Chikhirisitu chimakhala chopanda mwambo wolowera
Chikhirisitucho? Anthu a ku England ali ndi Chikhirisitu kuphatikizapo miyambo.
Anthu a ku Israel adali ndi mwambo woti munthu azisamba asanadye, kotero tsiku
lina adafunsa Ambuye Yesu kuti bwanji ophunzira akudya osasamba?

Maliro ndi Miyambo ya Achewa

Maliro a mwana wofera m’chikuta (Kubadwa kwa mwana)

5
Pamene mkazi ali wodwala pakati pamakhala miyambo ndi chisamaliro chambiri.
Panthawiyi mkaziyo saloledwa kuyang’ana mtembo wa munthu wakufa kuti
angadzabereke mwana wamzukwa. Koma ndi zomvetsa chisoni kuti amagwira
ntchito zolemetsa, mwinanso kumenyedwa ndi mwamuna wake ngati alakwa.

Mwamunayo saloledwa kuyenda ndi akazi ena, kapenanso kuyendera mitala yake,
kuti angadule mkaziyo. Ndiponso saloledwa kukumba manda mpaka mkaziyo
atadzakhala bwino.

Chifukwa chakusowa ndi kusadziwa chakudya chopatsa mphamvu monga zipatso,


mkaka ndi zina zotere, panthawi yobala, ambiri amabala mwana wopanda
mphamvu mwina woferatu. Atakhala woferatu amatchedwa ‘nthayo’, kapena
‘nsenye’. Amasonkhana amayi m’nyumbamo, koma osalira popeza amati
mwanayo si munthu weniweni. Atakhalakhala amasonkhanitsa makasu ndi
mitsuko, kenaka kamwana kakufako nabereka napita nako pamalo otchedwa
‘nsenye’, nakumba nakakwirira.

Mwana akamwalira, mzamba (namwino) amatenga mankhwala nawaza pa


mphuthu zonse ziwiri zakhomo. Mankhwalawa amasonyeza kuti mwanayo si
munthu wakuti amuna angamugwire, popeza kuti ngati atatero akhoza kuzitengera
matenda oopsya.

Ataika malirowo amayi onse amatenga mitsuko yawo napita kumadzi, nakasamba
kukachotsa ziwanda. Akafika kumudzi, amatenga makasu nawaula ndi moto;
amatero kuti ziwanda zingatsalire kumakasuwo.

Amagona panyumba yamaliro masiku ena kudikira ndi kutsangalatsa mayi


wofedwayo. Atatero amaitanizana amayi napita pamalo amene adaika kamwanako
kukatemera mankhwala ali maliseche. Amayiwo amatemana mphini ndipo magazi
ake amagwera pa muundapo, kenaka nachoka. Makolo a mwana womwalirayo
amapita pamalopo pakatha masiku atatu kukatemedwa mankhwala, iwonso ali
maliseche. Akamaliza kutemedwako amachoka pa muundapo.

Ndipo kukakhala kuti mkaziyo wapita pachabe kawiri kapena katatu, pamakhala
mlandu wakuti mwamuna sali kuyenda bwino, bwanji mkazi angopita pachabe
nthawi zonse. Mwa ici, ankhoswe akuchimuna ndi akuchikazi amakumana
nakamba mlanduwo, ndipo amalipira mbuzi, ndiko kuti mzimu umene ulikupha
anawo ukhululuke. Patsiku lometa amatenga nkhuku naponya m’nyumbamo.

6
Dzina la nkhukuyo amati, ‘nkhuku yakumitu’ ndipo amadya ndi ana okha a
m’nyumbamo.

Maliro a mwana wamasiku kapena miyezi

Pamaliro awa pali imfa zosiyanasiyana. Zifukwa zake za imfayi tanena kale kuti
Abantu sadadziwe makhalidwe olongosoka, ngati ukhondo ndi chakudya
choyenera, choncho amachita zambiri mosalongosoka.

Nthawi yakuti mwana wabadwa mzamba amatenga ufa m’manja nathira


m’chipande, natenga madzi pang’ono nathira m’chipandemo nasakaniza ndi ufawo
kuchita phala koma losapsa. Atatero amatenga namwetsa mwanayo kuti adziwe
kuti ali wamoyo kapena wakufa.

Mwanayo amalira kwambiri kukana phalalo koma mzambayo amam’kakamizabe


namaseka kuti mwanayo ndi wamoyo. Ichi ndi chinthu choopsa popeza matumbo a
mwana sangathe konse kusungunula chakudyachi ndipo chimangoima malo
amodzi ndi kuyamba kuola, choncho mwanayo amadwala kwambiri, mwina
mimba imatupa. Mwanayo amapatsidwa phala kuyambira panthawi yobadwayi
mpaka miyezi isanu, ndipo pamwezi wachisanu ndi chimodzi mwanayo
amapatsidwa zakudya zolimba monga nsima, nthochi ndi zina zotero.

Mwinanso mayiyo amatafunira mwanayo chimanga namulavulira m’kamwa ngati


mbalame. Pa chifukwa ichi mwanayo amadwaladwala ndipo mwina amamwalira
pasanapite masiku ambiri. Mwanayo akamwalira makolo a mwana amati mfiti
idamulodza ndithu.

Pali mbiri yakuti ku England kukabadwa ana zana limodzi (100), ndiponso kuno
ku Africa kwabadwanso ana 100, ana 40 a ku Africa amamwalira isanathe miyezi
isanu ndi umodzi, koma a ku England amamwalira mwina anayi okha patapita zaka
zambiri.

Panthawi yomwalira mwanayo, amayi amafulumira kukauza mfumu kuti mwana


uja wamwalira. Kenaka amatsuka mtembowo. Akatha kutsuka mtembowo amuna
amafika nabuma.

Amuna amapita kukakumba manda, ndipo akazi amakatenga miyala nayiwunjika


pafupi ndi mandawo. Amakonza bokosi lamphasa kuti ponyamula asavutike.

7
Atatha zonsezi amapita kumudzi nakatenga mtembo, ndipo amaliranso kwambiri
podziwa kuti tsopano mwanayo ali kukaikidwa kumanda ndipo sitidzamuonanso.

Pokaika malirowa amatenga miphika yonse imene mwanayo ankadyeramo, nsupa


yamafuta ndi zonse zake kuti zipitire limodzi ndi mwanayo. Akamaliza
amakasamba nadzagona pamtanda (pakhonde) masiku ena. Panthawiyi banja
lililonse sililoledwa kugona m’nyumba mwawo kuti angadule mfedwayo. Atatero
amameta natuluka pamtanda.

Mwana wamtengwa

Mabanja a Achewa adali ndi machitidwe osiyanasiyana. Pamene mnyamata


afunsira mbeta ndipo aloledwa, asanachite chinamwali mkaziyo saloledwa kugona
malo amodzi ndi mwamuna wakeyo. Atametedwa chinamwali iwo amalowana
m’nyumbamo, ndipo itapita nthawi mwina m’nyumbamo mumaoneka mwana
woyamba. Masiku onse mwana woyamba amatchedwa dzina ndi makolo a
kuchimuna.

Kalelo mwamuna sankaloledwa kutenga mkazi kupita naye kwawo ngati ntchito
zake sizidali zokwanira kusunga munthu. Ndiponso ngati m’banjamo mulibe
mwana, popeza amayi a mkazi amati, ‘Sitidziwa, mwina mwamunayo
ngosabereka.’ Choncho ngati iye sankaonetsa izi sankaloledwa konse kutenga
‘chitengwa’. Zitengwa zilipo zamitundu iwiri: chitengwa chodziwana bwino ndi
ankhoswe akuchimuna ndi akuchikazi, ndi chongomvana mwamuna ndi mkazi
wake.

Koma m’mutu uno tifuna kutsata za chitengwa chodziwika kwa ankhoswe.


Mnyamatayo amapita kwa ankhoswe ake akuchimuna nati, ‘Mukandipemphere
chitengwa kwa ankhoswe anzanu, akuchikazi.’

Ankhoswe aja amapitadi kwa anzawo aja nati, ‘Pepani anzathu, ife timafuna kuti
mkaziyu akatiphikire kwathu.’ Ndipo ankhoswe akuchikazi amauza nkhaniyi
makolo a mkaziyo. Atavomerezana, amati, ‘Chabwino, wathuyu tengani, koma
pakaoneka matenda ndi zovuta zina muzidzatiuza mofulumira.’

Amapereka nkhuku yodziwitsa ankhoswe akuchikazi kuti, ‘Wanu tatenga ndife a


mudzi wakuti.’

Atakhalakhala uko, mwina pamapezeka matenda, ndipo anthu onse amadankhawa,


natumiza mthenga wokanena kumudzi kwa mkazi kuti mwana kapena iye mwini

8
akudwala. Nthawi zina mwana amadwala mwadzidzidzi ndipo pasanapite masiku
mwanayo amamwalira. Mwankhawa, amatumiza mthenga wokanena kwawo kwa
mkazi kuti mwana wa mwana wanu uja amwalira.

Zikamveka izi akhoswe akuchikazi, amadodoma nati, ‘Bwanji mwadzatiuza


maliro, nanga matenda mudalekeranji kudzatiuza?’ Akafika pafupi ndi mudziwo
amayamba kulira nazungulira mudziwo, ndipo eni mudzi amatenga mbuzi yakuti
anthuwo alowe m’mudzimo.

Atalandira mbuziyo amalowa m’mudzi nayamba mlandu wakuti, sadauzidwe


zamatenda a mwanayu. Ndipo eni mudzi amavomera kuchimwa kwawo popereka
mkanda kuti malirowo awatulutse.

Malirowo mwina amawanyamula kupita kwa mkazi. Ataika malirowo, ankhoswe


akuchikazi amafikanso nati, ‘Lero tabwera kudzalandira malipiro a mlandu uja.’
Ndipo akuchimuna amapereka mbuzi imodzi kapena ziwiri, koma ngati ankhoswe
akuchikazi aja sakhutira amati, ‘Dipoli silikukwana, chifukwa choti mudabisa
matenda a mwana wathu.’ Ataonjeza, amapatsana chimwerana mowa, kusonyeza
chiyanjano, kuti pakati pawo pasakhalepo kanthu kena, koma chikondi chokha.

Koma chikakhala chitengwa chosadziwika bwino ndi ankhoswe, pamakhala


mlandu waukulu, popeza ankhoswe akuchikazi amati, ‘Ife sitinkadziwa kuti wathu
ali kuno. Kodi chitengwachi nkhuku yake mudapatsa yani?’ Ndipo ankhoswe
akuchimuna amapereka mbuzi imodzi ya ‘ndapusa’ kuti adangotenga munthu wa
eni mwakuseri. Ndiponso amapereka malipiro a mlandu wakuti, ‘Wanu wafera
kuno.’ Mlanduwu umakhala woposa woyambawo.

Zitatha izi amatuluka pamtanda nameta kuchotsa ziwanda zimene zidakhalira


kutsitsi.

Mwamunayo amaponya kanthu m’nyumbamo, mbuzi kapena nkhuku kuti mzimu


ukhale pansi. Dzina la nkhukuyo amati, ‘chakumitu’.

Kuyamba kwa banja

Choyambirira kuyamba ndi banja. Kuti banja liyambike ndiye kuti mwamuna ndi
mkazi akambirana zachibwenzi chodzadzetsa banja. Atagwirizana mnyamata
amadziwitsa atsibweni ake (malume) za nkhaniyo. Mosazengereza atsibweni aja
mwina amatuma wina kuti akafunsire mbeta. Atafika kumudzi kuja amamulonjera
motere: ‘Monitu.’ Iye amayankha kuti, “Ee moni.” ‘Nanga n’kwabwino?’ Iye

9
amati, “Ee n’kwabwino.” Kenaka amamfunsa kuti, ‘Nanga mwatiyendera?’
“Zoonadi tadzakuyenderani. Koma chodzera kunotu n’chakuti, kwathuku tili ndi
tambala ndiye timati tidzasinthane ndi msoti wanu,” iyeyu amayankha motero.

‘Iyayi, mwabwera ndi nkhani ya bwino. Nanga dzina la msotiwo ndani?’


“Tobalire, mwana wobanda uja.” Nkhoswe yakuchikazi imati, ‘Chabwino
zamveka, pitani mumvera kuno.’

Kumadzulo amalume, omwenso ndi nkhonswe yakuchikazi, amapita kwa makolo


amsungwana uja nati, ‘Kunyumbaku kunadza mwana wa mbwetu, amasimba kuti
tambala wakwawo adapezapo msoti womwe ndi Tobalireyu, ndiye ndimati
timufunse ngati adagwirizana kale ndi mnyamata yemwe nkhonswe yake
inandipezayo.’

Atafunsidwa Tobalire amavomera kuti, ‘Zoonadi, mnyamatayo ndamukonda ndi


mtima wanga wonse.’ Zikatero makolo amafunsana motere, ‘Kodi mnyamata
amene uja ndi wantchito ndiponso waulemu?’ Ndiye ena akachitira umboni kuti
zoona ndi mnyamata wa makhalidwe abwino, amabweza mawu kuchimuna kuti
mnyamatayo wavomerezedwa.

Mosazengereza akuchimuna amakonza tsiku lokatula mnyamatayo. Komatu tsono


amabwera atakonzeratu zofunikira zonse, monga chamlomo, khasu, chikwanje,
ndiponso nkhwangwa. Kachidzulo amafika naye kumudzi kuja. Nkhonswe
yakuchimuna imalonjerana ndi eni mudzi. Ndiye amapereka chamlomo. Pokonza
zakudya, nkhuku imaphikidwa yamphumphu ndi kuipereka yonse kwa
mwamunayo.

Mwana

Nthawi yobadwa mwana pamakhala ntchembere zikuluzikulu zokhazokha,


kuphatikizapo namkungwi.

Mwana akabadwa, chodziwitsa kuti mwanayo ndi wamoyo amalira kuti, ‘Ng’a!
Ng’a! Ng’a!’ Mosazengereza amanjata mchombo wa kamwanako kuti mphepo
ingamulowe m’mimba. Amayi amatenga chipande n’kuthiramo ufa ndi madzi
n’kumatakasa ndi chala chamkombaphala mosaliika pamoto konse. Akasakaniza,
amagadamitsa mwanayo ndi kumumwetsera pachikhato. Kenaka amamusambitsa.
Zikatero amaimba nthungululu kuti mfumu idziwe, komanso mudzi onse. Kenaka
namkungwi amakadziwitsa mfumu motere: “Odi, amfumu!” Mfumu imayankha
kuti, “Odini.” Ikatero imatsegula chitseko ndikunena kuti, “Lowani.” Namkungwi

10
atalowa mfumu imati, “Tikuoneni.” Namkungwi amati, “Zikomo amfumu.”
Mfumu imati, “Kodi n’kwabwino?” “N’kwabwino. Kutereku n’kudzakudziwitsani
kuti, mwana uja anali wodwalayu tsono wakhala tsonga.” Mfumu imati, “Kodi,
zikatero zakhala bwino. Kuteroko kuli munthu wamtundu wanji?” “Ndithu,
kwabadwa munthu wamwamuna,” nankungwiyo amatero. Mfumu imati, “Zikomo
kwambiri. Umo ndimo zinthu zimayenera kukhalira. Nanga makeyo ali bwanji?”
“Ali bwinobwino ndithu wopandanso kamtsaliro.’ Mfumu imati, “Kodi! Zakhala
bwino.”

Pambuyo pake mwanayo amamutcha dzina. Nthawi zambiri mayina amakhala a


matanthauzo, osonyeza chisangalalo, madandaulo, chidzudzulo, kapena
chikumbutso cha zosangalatsa kapena mikwingwirima. Ena mwa mayinawo ndi
awa:

Dzina Tanthauzo
Tobalire kwangovutika kubereka
Tankhulenji chonena tilibe
Tafatatha tangotitsirizani
Chipezayani ine ndiye ndatsogolako
Balalata chidzakupeza
Phereni ndekha sindingathe
Nkafanikhale zivute zitani sindidzaopa
Kapazam’mbali wamaganizo opotoka
Kamwendom’njira wosakhazikika pamalo amodzi
Titani tigwira mtengo wanji
Chimkondenji mutopa kukamba za ine
Chapansi kubisalira
Mumderanji ndimalakwanji
Mwathaanansi mwatsala nokha
Zayakunkhongo wosaweruzika
Kulinji wosalabadira zam’tsogolo
Kumvenji kumbuyo kulibe maso
Mawuawawa mawu owawa aposa saiwalika
Mtisunge tikhale nawo musatitaye
Mtengaponji palibe chomwe mupindulepo
Mferamo mwangoferamo opanda mwana
Zagwazatha zachitika kale
Kangachepe ndikwanitsa musandiderere
Katsonga kupezapo bwino
Mwalipeza mudzatikumbukira

11
Mzati mlimbiko pogomezera
Dalitso mphatso yaulere
Munguuza wosowa nansi
Kathewera chovala m’chiuno mokha
Msasata ndalira ena
Mphindapansi zolowere n’kudyere mwana
Zimpita wosaweruzika
Mwaonanji mudandileka kale
Kamzunguze mpitireni pansi musamuuza
Bololo sakondamadzi simungandithe
Mwadzaangati mwachepa
Mkalinacho chidani chamgonamgona
Chikalipo kusungira zinthu mumtima
Sulitha zikukanika
Msekamwamvu womana kapena wosamverana chisoni
Masautso kusowetsa mtendere
Msekadala chikondi chachinyengo
Mlimbanaye suyotu mumuona nokha
Sindisamala chichitikechichitike
Sosola pitikitsani kapena chotsani
Mtalimanja munthu wosasowa kanthu
Chosadziwa zosakonzekera kuti zichitika
Tchete kavuwevuwe
Kanthun’kako kusadalira za ena
Mthyoka wolumala ziwalo
Mzembera wosanena zoona
Mphungusatayanthenga wakaligwiritsa
Kayendekeza woyembekezera ufumu

Mwana akabadwa, amadwala matenda osiyanasiyana. Ena mwa matendawa ndi:

Liwombo Pakatikati pa mutu pamawoneka polowa. Pamatukula ndipo


makolo amakhala tcheru namaonetsetsapo usana ndi usiku.
Pakangoleka kutukula kapenanso kutupa amakhala ndi nkhawa.
Liliwo Panthawi yoti mwana asome, zopatuka zake zimakhala za
chisasu. Ili ndilo liliwo.
Mauka Thupi lamwana limatentha, ngakhalenso kudzidzimuka.
Malungo kunjenjemera kapena kuti (manjenje), kutenthanso thupi.
Chisanzosanzo Akadya kapena kuyamwa n’kumasanza.
Kufumbata zala zimafumbatirana n’kuchita ngati kuti zauma.

12
Maso m’masomu mumakhala kapena mumatuluka manthongo,
kenaka maso amafiira, ndi kuwawa kwambiri.
Ukweche m’phechepeche mwa mwana mumatuluka matuza oyera
ndiponso onyenyesa zedi.
Utumbidwa (tsempho) mwana wooneka wosasangalala, komanso wopanda
chilakolako chakuti adye. Thupi lake looneka ngati lidawawuka
ndi moto. Mimba imauma komanso miyendo imatupa.

Mphala

Pamudzi ulionse pamakhala kanyumba kena kodziwika ndi dzina lakuti mphala.
Nyumba imeneyi ndi ya anyamata ang’onoang’ono amene sadakwatire. Pamene
mwana wakula ndithu amamutumiza kwa agogo ake. Atasunzunukapo, ngati ndi
mnyamata amakagona kumphala kwa anzake. Anyamata amagonera ndi kudyera
limodzi ndipo usiku amaphunzitsana nthano, miyambi ndi zina. Nyumbayo
imakhala ngati sukulu yophunziriramo maluso osiyanasiyana, monga kuweta
ng’ombe, mbuzi, nkhosa; kumweta tsekera ndi kuphunzitsana kumanga mfundo
yachimuna. Pakakhala makangano, amaweruzana bwinobwino potsutsa wolakwa.
Pamakhala ena okulirapo omwe amakhala ngati atsogoleri. Komanso kumeneko
kumakhala kuphunzitsana maudindo monga kutolera nkhuni, kuweta ziweto ndi
masewero ena olimbitsa matupi. Pali chikhulupiriro choti ana ogona m’mphala
amakula bwino ndipo amakhala olimba m’thupi, aulemu, omvera, antchito ndi
ochangamuka.

Alipo ana ena amene amathawa kumphala nabwerera kwa makolo awo. Oterewa
amawaseka. Zikatero mwana wotero amamusala nakhala ndipo amakhala
chiyendayekha. Pakudya nsima, mwana sayenera kuyamba kusamba. Kumphala
kumakhala chidyerano, womwe ndi mchitidwe wosonkhanitsa nsima zonse
m’mphalamo n’kumadyera limodzi. Ana amaonetsa osakhuta msanga malinga
n’kubadwa kwawo.

Kubusa kumakoma panthawi yodya mondokwa chifukwa chakudya sichisowa.


Kubusa akamabwera anyamata amaimba kuti, “Wopanira m’phika ali chete
tangosauka.” Komanso ntchito yokolola ikatha, anthu amachita khunkha m’minda
ya anthu ena. Abusa aziweto akafika kumudzi amapeza chingowe, nseche, thathika
ndi misere zonsezi amadyera limodzi kumphala kuja.

13
Kuka

Nyumba imene mumagona makolo amaitcha kuka. Makolo amakono akugoneka


ana m’kuka poonetsa chikondi. Ndiye ana ogona m’kuka sadziimira paokha kotero
nkhuni, madzi, zovala ndi zofunda zonse angozipeza zokonzakonza. Ana otere
amakhala ngati mtengo wokulira m’malunje umene suwombendwa ndi mphepo,
kapena mtengo wotere umakhala wofooka ndi wosalimba. Ana ogona m’kuka
ambiri amakhala opanda mkhalidwe wa umunthu. Choyambirira amatengera
makolo awo kwambiri. Makolo akamamenyana iwo amatenga mbali. Ndipo ana
otere amakhala onyada, ozikonda ndiponso osadziwa kuchedza ndi anzawo.
Akatalikirana ndi makolo awo amaona ngati akuzudzika kwambiri.

Mwana woyamba kumera mano kumwamba

Achewa ataona kuti m’banja lina mwabadwa mwana, koma pomera mano ayamba
kumwamba, makolo ake amwanayo amapita msanga kwa mfumu nam’dziwitsa
zonse za mwanayo. Pakati pa Achewa amaganiza kuti mwana wotere adzakhala
mfiti, wodya anthu ndiponso wosatsutsidwa. Podziwa ichi, samalola mwana
kukhala pakati pawo.

Makolo amwana amakondwera kwambiri pamene mfumu yawalamulira choti


achite pa mwanayo. Mfumu itamva mawuwo, imalamula kuti mwanayo am’taye
pamadzi, kapena aphedwe.

Ndipo makolo a mwana akam’funitsitsa mwanayo amayesa kupepesa kwa mfumu


kuti mwanayo asamuphe. Ndipo mfumu imalamula kuti koma ayenera kuombola
moyo wa mwanayo. Mwamsanga makolo a mwanayo amasonkhanitsa chuma
chonenedwa ndi mfumu napereka, ndipo mwana amaomboledwa. Koma anthu
samakhulupirira, amangoti ‘ndiye mfiti ndi waliuma’, angakhale suli choncho.

Koma ngati mwanayo amulephera kumuombola amamutenga namutaya padziwe


kaya pambirira (mathithi), ndipo pamalopo amatchapo dzina. Monga ku Mvera,
kufupi ndi Mfumu Chiwere, kuli malo otere omwe amawatcha ‘Kumtaya Ana’.
Ndikhulupirira alipo malo ena ambiri kumene anawo adatayidwa ndi kuphedwa
m’dziko lathu lino.

14
Maliro otere samawalira kapena kugonera pamtanda, koma amangochita ngati
ataya galu wachiwewe.
Komanso sizikudziwika ngati makolo a mwanayo amakondwera ndi mchitidwewu.

Maleredwe a ana a Achewa

Achewa adali ndi miyambo yolerera ana awo. Ndipo m’mutuwu munenedwa
mwachidule miyambo ina ya Achewa yokhudza maleredwe ya ana monga iyi:

• Mwana akabadwa m’banja, anansi a banjalo akuchikazi ndi akuchimuna


amalinda osakhala ndi ufulu m’nyumba mwawo.
• Mwanayo limafika tsiku lake lakumtenga, bambo ndi mayi. Ndipo
amadziwitsa anansi kuti mwanayo nditenga lero, ndipo onse anali
kumasulidwa ndi kukhalanso aufulu. Koma ngati mwamunayo adapita
kwina, mwanayo amatengedwa ndi banja lina. Napangana ndi banjalo
kuwapatsa chuma (mbuzi ndi zina), popeza ankakhulupirira kuti, ngati
satero mwanayo akhala wopanda magazi ndiponso wopanda mphamvu.
• Ngati pamudzipo pali gule wa nyawu, amatenga mwanayo namuimbira
ng’oma m’makutu, ndiponso amamukweza pamsana pa nyawu. Uwu
umakhala ngati ubatizo wawo wosonyeza kuti mwanayo tsopano
wabatizidwa.
• Mwana wachisamba makolo ake saloledwa kum’tchula dzina lake lenileni.
Pakumuitana, amangoti, ‘Muna, Bambo kapena Tata.’ Akakhala wamkazi
amati, ‘Buthu, Chimwana, Mbombe, Kamayi kapena Khanda.’ Komatu ena
atha kumuitana dzina lake lenileni. Dzina la mwana limachokera kwawo
kwa mwamuna nthawi zonse.
• Nsalu, Malaya, miphika, mkuzi, nsengwa ndi zina za mwana zikagona panja
samalola mwana kugwira nazonso ntchito, kuti mwanayo angafe.
• Mwanayo amauzidwa kuti ngati apisa mum’phika (kuba ndiwo) ndiye kuti
adzitengera matenda amasaya (mdulo).
• Mwana akachokapo makolo ake amakhala omangika m’banja ati, ngati
sasunga mwambo apha mwanayo mwakum’dula.
Pamene ndinali kulemba mawuwa, ndidamva mkulu wina akuti,
kumpingo wina kunali banja lina limene lidadikira mwana wawo yemwe
adatchona ku Harare kalekale, komwe adakhalako zaka zoposa khumi ndi
zisanu. Zachisoni, anthuwa kuti adalibe ufulu pazaka zonsezi.
• Mwana wina akatema mnzake m’mutu ndi mwala, mpeni ndi zina,
mwanayo amametedwa pabalapo navekedwa mkanda woyera.

15
• Mnyamata akagwaza mnzake ndi chisongole chosokera mphasa ndiye kuti
wolasidwayo amayenera kutenga nkhuku yoyera napatsa amene
anamugwazayo.
• Mwana ayenera kudya dothi kuti atsendere liombo (msoma).
• Mwana akamalira pamene mayi ali patchito yolima kapena yophika, wina
amulande mayiyo khasulo kukhala lake, kaya ngati akuphika, amulande
nsimayo. Amatero popeza kuti kuteroko ndi kuzunza mwana.
• Mwana avekedwe mkanda pakhosi, pamiyendo, pamanja ndi m’chiuno.
Womutcha dzina am’patsenso mkanda.

Miyambo ina ya Achewa

• Bango ndiloletsedwa kumenyera munthu chifukwa limaondetsa.


• Mwamuna sayenera kulowa ku nkhokwe popeza amadya chipalasiro
mphalo.
• Mayi woyembekezera (wapakati) sayenera kuona mtembo kapena gule
wamkulu kuopa kuti angatengere, podzabereka angazabereke mzukwa.
• Mayi asamathire mchere mu m’phika panthawi yoti ali payekha.
• Si bwino kugonera malo amodzi ndi mkazi panthawi yoti ali pathala
laling’ono.
• Sikoyenera kuyamba kusamba m’manja akulu asanasambe.
• Ulemu wa amayi umasonyezedwa mwakuomba m’manja.
• Poyetsemula kumafunika kuyetsemulira m’manja.
• Patsiku lokatula mbeta si mwambo kumaliza nsima yonse m’mbale koma
kuisiya angakhale sudakhute, koma nkhuku imene yaphedwa iyenera
kuperekedwa m’phika wonse osagawa.
• Si mwambo kutsutsana kapena kupolokezana pamene mfumu ikuyankhula.
• Mtsikana akathyola bano azibindikira mpaka matenda atatha, komanso
osathira mchere mum’phika.
• Paulendo, wotsogolera izikhala mfumu.
• Pakumwa madzi aziyamba ndi akuluakulu.
• Wotsogolera kumaliro ndi mfumu.
• Mtengo wa namwali suyenera kugwetsedwa, popeza mfumu siimenyedwa.

Mwana wamasiye

16
M’dziko lonse lapansi pamaoneka ana amasiye. Pakati pa Achewa ana amasiye
adalipo, koma kasamalidwe kapena machitidwe ake amasiyana ndi mmene
imachitira mitundu ina ya anthu.

Pamene mayi wamwalira amasiya ana pabanja. Anawa amasauka kwambiri popeza
mabanja ena amawakana kuwalera nati, ‘Nditha kulera ana amasiye, koma pamene
mzimu wa mayi wawo ubwera kufuna ana akewo utha kudzatenga mwana wina,
mwina m’malo motenga mwana wamasiyeyo ungadzatenge mmodzi mwa ana
anga.’ China ndichakuti amaopa kulongosola ana amasiyewo.

Pomwalira mayi, mwina amasiya mwana wakhanda wobadwa nthawi yomwe


wamwalira mayiyo. Zikatero amayi amatenga kamwanako nakapha kuti kapitire
pamodzi ndi mayi womwalirirayo. Izi amuna samadziwa, popeza amayiwo
amachita mochenjera kwambiri ndiponso mwachinsinsi. Malirowa sadziwika kwa
anthu ambiri koma amayi akuluakulu okha. Ndipo malirowa amaikidwa kumalo
aja otchedwa ‘nsenye’ kumene ana aang’ono kwambiri amaikidwa akamwalira.

Za maikidwe ndi machitidwe a mayiyo tifotokoza ponena za mkazi wapakati.

Mnyamata

Mnyamata akakula, makolo ndi amalume ake amapangana kuti mnyamata ayenera
kupita ku nyawu. Uyu ndi gule wa Achewa amene amachita panthawi yamaliro
yokha. Monga mudziwa nyawu zilikuchuluka kwambiri m’maboma awa:
Lilongwe, Dowa, Kasungu, Nkhotakota, Ntchisi, Mchinji, ndi Dedza, popeza
kumeneku ndiko kuchimake kwa Achewa.

Makolo amasonkhanitsa chuma: nkhuku, mbuzi ndi zina zoti akazipereke ku


nyawuko monga mwamalamulo ake. Ali pafupi kufika, mnyamatayo amam’manga
nsalu m’maso, namvula zovala. Akafika amamulowetsa m’chinyawu nati, ‘Mira,
mira, mira.’ Ndi mchitidwewu, amafuna kuti alowemo ndithu.

Nyawu imapangidwa ndi zinthu monga izi: makoko, udzu, luzi, ndi chibzero.
Akalowa mnyamatayo amadabwa kwambiri, popeza asanabwere kudambwe
(kumalo kumene amapangira nyawu) amauzidwa kuti nyawu ndi nyama yamafuta
imene amaitulutsa padziwe ndi mbeza ndipo nyambo yake ndi dzira. Koma pa
nthawiyi iye amaona kuti zonse zimene adamva zidali zonama.

17
Zikatero ku dambweko akuluakulu amamenya anyamatawo zolimba, ndipo ena
amavulala kwambiri. Amatenga mnyamata, namutulutsa m’nyuwu, nayamba
kum’menya kwambiri. Makolo a mnyamatayo amaneneratu zimene mnyamatayo
amachita, zabwino kapena zoipa, zamwano kapenanso zaulemu.

Gule ndi anthu ake

Kudambweko kumakhala mafunso kapena maphunziro omwe amakhala ozunguza


kuti munthu apeze mayankho ake.

Akatha izi amayamba kumuuza miyambo ndi malango a nyawu nati, ‘Mum’phika
wa amayi ako osakapisamo manja; kubedi kwa makolo ako osamakapitako;
osakakhala pamodzi ndi amayi ako; ndiponso osakasewera ndi ana aang’ono.’

Mafunso ndi mayankho a ku gule wamkulu

• Nyama zimagona kuti? Kutanthauza kuti, ‘Kodi gule amakhala kuti?’


Yankho: kunkhokwe ndi kudzala
• Mawanga a nkhanga ndi angati?
Yankho: awiri; pamakhala mbuu ndipo bii
• Mawanga ankhanga adayambira kuti?
Yankho: adayambira kunsi mpaka kumtunda
• Zimwera kuti?
Yankho: pena pamakhala kunkhuti kapena kunkhokwe
• Madzi akadzala amalekeza muti?
Yankho: amalekeza m’mapazi
• Madzi akaphwa amalekeza muti?
Yankho: amalekeza m’khosi
• Namkungwi wa Chabwera, Chaona, Simoni, Chadzunda n’chiyani?
Yankho: msompho
• Namkungwi wa Kachipapa, Kwakwase, Kapoli ndi Kasinja n’chiyani?
Yankho: zingano
• Mafuta a Kwakwase ndi Kachipapa n’chiyani?

18
Yankho: phulusa (chipala)
• Magazi anyawu n’chiyani?
Yankho: thukuta lamunthu
• Mtima wa nyawu n’chiyani?
Yankho: munthu
• Kautsa gule n’chiyani?
Yankho: chabzero
• Nthiti yagule n’chiyani?
Yankho: chabzero
• ‘Ithani gule’
Yankho: namkungwi, chilale, thonje, makhwatha
• Pansipo!
Tanthauzo: wovinitsa nyawuyo wanyamulitsa ndipo atsitse pansi mmene
mwalowa nyawuyo
• Chalunda chosaguba
Tanthauzo: chaola munthu sameta chosamvera
• Tidzaonana podya mphonda
Tanthauzo: tsiku limene kudzakhale gule tidzakukhaulitsa kapena
udzamenyedwa

Munthu yemwe sadalowe ku gule wamkulu akakumana ndi anthu anyawu


amamufunsa mafunso monga omwe ali pamwambapa. Ndipo ngati iye sayankha
amamenyedwa kwambiri, mwina amaphedwa. Maliro otere sadziwika ndi anthu
ambiri, koma okhawo amene adaona pophedwa paja. Ndiponso saulula konse
ndithu. Eni mwanayo amangofuna koma wosampeza.

Mnyamata wolowa nyawu akamwalira amauziratu mfumu malirowo


asanatsukidwe. Pambuyo pake akatsuka mtembowo amabuma. Atatero amapita
kumanda. Pamalirowo amatenga zake zonse za mnyamatayo monga uta ndi mivi
yake, mpeni, ndodo ndi mkhate wosambira m’maso. Zonsezi amaziika pamodzi
m’manda kuti mzimu wake ungadzabwere kudzafuna zinthuzo, zimene adasiya.

Asanatuluke pamtanda, makolo a mnyamatayo amauza wakunjira nati, ‘Tifuna kuti


tilire malirowa mwakuvinapo nyawu.’ Wakunjira amauza nkhaniyi kwa mfumu,
ndipo mfumuyo imauzanso nduna zake. Atatero amakapanga nyawu nafika
kumudzi madzulo navinitsa nyawuzo masiku awiri. Makolo a mnyamata
amasonkhanitsa mphotho zofupa guleyo. Akatsiriza amameta tsitsi, anthu
namwazikana.

19
Mnyamata wokalowerera kudambwe

Pamudzi pamakhala anyamata ena amene amachedwa kukalowa kudambwe pa


zifukwa zina. Mwina kusowa nkhuku zokalowera mwina makolo ake ndi
Akhirisitu. Anyamata otere amalakalaka atalowa. Zitatero mnyamatayo amakonza
zoti akalowerere yekha kudambweko. Mozemba amapita kudambweko motsenjera
ndipo mwadzidzidzi amamutulukira kudambweko. Atamuona amamugwira
mwankhondo n’kuyamba kumumenya mwachisawawa koma molapitsa.

Kulowerera kudambwe si mwambo wake chifukwa kuchita ngati kupezerera


munthu akusamba. Panthawiyi yolowetsa mnyamata pamafunika kukonzekera
zonse bwinobwino.

Kulowera kumeneku mfumu imayenera kuuzidwa. Ndiyetu umakhala mlandu.


Dipo lake limakhala tonde wa mbuzi. Tondeyo amadyedwa kudambwe komweko
zosakhudza mafumu. Wolowererayo amaphunzitsidwa zonse molingana ndi
mmene amalowetsera wina aliyense. Nthawi yovinitsa zilombo namwali
amakhazikitsidwa mkwinya mwa wabwalo (m’mphepete mwa bwalo). Ndipo
nthawi yoti chilombo chikuvina pafupi ndi iyeyo iye ayenera kumachithira malovu
chilombocho. Umenewo ndi mwambo poopera kuti angayaluke
kumadzidzimukadzidzimuka. Komanso amamudyetsa khundabwi.

Ng’oma zitatha namwali amakhala kusimba ndi phungu wake, ndipo chakudya
amamutengera ndi phungu uja tsiku ndi tsiku mpaka tsiku loombetsa m’manja
litakwana.

Mayi wolowa kudambwe

Akazi ena poyendayenda, mwina pokatola nkhuni mosayembekezera


amakatulukira kudambwe ndiye amaona zilombo zili ndandanda ndipo amayamba
kumathawa. Akunjira akawaona amawapirikitsa mpaka kuwagwira. Zikatero
amakadziwitsa mfumu.

Ndiye nthawi yomweyo, mayi wogwidwayo, amamuonetsa gule aliyense


kudambwe ndipo amaphunzitsidwa kuyankha mafunso onse okhudzana ndi gule
wamkulu. Komatu kwa mayi kumasiyana ndi malowedwe a anyamata. Mwamuna
wake wamkaziyo akamva amakhumudwa kwambiri, koma sangachitire mwina
koma kugwirizana nazo. Nthawi zonse pakakhala gule pamudzipo mayiyo
amakhala nawo kubwaloko, ndipo nthawi yoti chilombo chikuvina mayiyo
amavinira m’mbalimu. Mwina chilombo chikamayimba nyimbo mayiyo

20
amapolokeza. Ntchito ya mayiyo (udindo) n’kupezera zosoweka kudambweko,
monga phala, ufa, nkhuku ndi mowa zochokera kumudzi. Ngati pali zoyenera
kuphika kudambweko umakhalanso udindo wake.

Patsiku loshambula mowa ndi patsiku lotsiriza pamene zilombo zonse zimavina
masana, mayiyo amavina nawo m’bwalomo ndipo amasupidwa ngati chilombo
chomwe.

Nyau kapena gule wamkulu


Kupembedza ndi kuyankhula, kapena ubale womwe ulipo pakati pa munthu ndi
Mulungu. Kutanthauza kuti munthu angathe kupembedza Mulungu kapena fano.
Koma gule wamkulu si chipembedzo ayi, ndi mwambo umene Achewa amachita
panthawi zosiyanasiyana, monga pa maliro ndi chinamwali. Iwowo amakhulupirira
Chauta amene amam’pembedza ndi kum’sirira nsembe. Ndiye mwambo wagulewu
ungafanane ndi mwambo wa maliro a Chikhirisitu, koma si kupembedza
kumeneku, ayi.

Tsono mpingo ndi gulu la anthu amene ali ndi chikhulupiriro ndi chiphunzitso
chimodzi ndiponso amachita mwambo wosonyeza kulowa kapena kulandilidwa
mugulumo, monga ubatizo kwa Mkhirisitu. Angakhale anyawu angafanane ndi
mpingo pazimene tanenapa, sasonyeza chipembedzo. Angofanana ndi gulu limodzi
m’mpingo wa Chikhirisitu.

Pajathu mpingo kapena gulu limakhala ngati banja kapena ana anyumba imodzi pa
khalidwe ndi zochitika zawo. Tsono wochita zosiyana mwina zosutsana ndi anzake
kapena amene sali ndi mbali mu upowo ndi wakunja. Ichi chikutanthauza kuti
ampingo umodzi atha kunena wa mpingo wina kuti ndi wakunja, kapena a gule
wamkulu atha kutchula Mkhiristu kuti ndi wakunja, Akhirisitunso chimodzimodzi.

Mayina a gulewamkulu

Njovu
Gule ameneyu ndi wamkulu kupambana magule ena onse. Ndiye satuluka wamba
kaya kuti chisawawa koma pokhapokha pa maliro a mfumu, nduna ndi a
namkungwi, komanso amatuluka pamkangali. Dambwe la Njovu ndi la mafumu
okhaokha. Mnyamata saloledwa kukhalira nawo popanda kupereka nkhuku.

21
M’nsupo wake ndi ng’ombe, mbuzi ndi kufundika mphasa pa msana. Nyimbo yake
amati:
Pang’onopang’ono abambo ogo ee!
Pang’onopang’ono abambo ogo dede!
Wochita mang’ombe amati: Hee, hee!

Njovu

Patsiku lotuluka Njovuyi imakafikira kuchitsime mpaka mfumu itapereka mkota


wa mbuzi. Tsopano imakavina, nayisupanso, ulendo wake umakhala omwewo wa
kuliunde kokagona.

Patsiku lotsiriza gule, Njovu imavinanso m’mamawa dzuwa lisanatuluke.


Itasupidwa imabwereranso kuliunde kon’kuja kukagonanso. Patsiku lotuluka
kudambwe, kumapita mowa wachimwetso, kutanthauza kuti ntchito yonse yatha.
Isanabwerere kudambwe kumadzulo imavinanso, ndiye amayiperekeza mpaka
kudziwe kumene adayivuula. Nyambo yake yowedzera ndi dzira la nkhuku.

Mdondo

Guleyu amakhala wamtali mwina mikono khumi ndipo amatuluka pa maliro a


anthu wamba monga mandoda, anyamata ndi amayi (ntchembere). Amatuluka
patsiku loshambula mowa. Anthu akamwa mowa wachimwetso, amachita
mang’ombe n’kumayimba nyimbo amvekere kuti, ‘Kachita ngati ubwerera nyata
iwede.’ Othirira n’kumati, ‘Hee, hee, hee.”

22
Mdondo

Kasiyamaliro

Iyi ndi nyawu yokongola kwambiri komanso amayipanga bwino zedi mwaluso.
Patsiku lotulutsa Njovu, Kasiyamaliroyo amatsogolera Njovuyo. Kubwalo
imayamba kuvina ndi Njovuyo. Nyimbo yake imvekere:
Chimcheka dede! Kasiya eede.
Othirira mang’ombe n’kumati:
Kasiyamaliro ee hehe!

Kasiyamaliro

23
Kasiyamaliro

Kalulu mkuluwabwalo

Poyambirira kapena kuti potsegula bwalo, zilombo zisadavine, amayamba ndi


Kalulu. Umenewu umakhala ulemu wapadera wopatsidwa kugule ameneyu.
Povina amapatsidwa ulemu wovinira pamphasa. Guleyu ndi wa chikoka ndiponso
wosangalatsa kwambiri. Nthawi zambiri amatuluka ngakhale masana, dzuwa
likuswa mtengo maka pa maliro amunthu wamkulu monga mfumu, nduna ndi
namkungwi.

Kalulu amatsogolera chitanda mpaka ku manda. Nyimbo yake amati: Kaluluwe!


Kaluluwe! Inde Kalulu we!
Othirira mang’ombe amati, “He-he-he-he-he-he-he!”
Mwina amati: Kaluluwe ndendeyo! He! Inde, Kaluluwe ndendewe! He-he-he-he-
he!”
Othirira n’kumati, “Kalulu mkulu wa bwalo!”

Chadzunda

Chilombochi maonekedwe ake ndi chakuda kumanso. Mayendedwe ake amakhala


ngati nkhalamba. Chimavina ngati gwetsa, mozungulirazungulira. Chimaoneka
maka pa tsiku lam’meto, kayanso pa mpalo, kapenanso pa mkangali.

Nyimbo yake amati, “Kumalambo dedede he- he- he-he! Kumalambo dede!
Tinkanena dede! Tinkanena dede hehehe!”

24
Chadzunda

Kadyankhadze, Chabwera Chaona, Chabwera Kumanda

Mayina atatuwa ndi a chilombo chimodzi. Chimaoneka chowopsa kwambiri;


chofiira ku maso kwake, ndipo chimavina modumphadumpha, ng’oma ili m’kati.
Chimakhala ndi mkwapulo m’manja mwake ndipo chimayenda mothamanga.

Kadyankhadze

Chimaoneka m’maliro masana, dzuwa likuswa mtengo. Nyimbo yake ina imati:
“Odede, dedza hoo! Odede, dedza ayo! Inde inde tate adagwa m’chipala!”
Kadyankhadze amavala kabudula ndi Malaya agwanda.

Simoni

25
Maonekedwe aguleyu amafanana ndi a Kadyankhadze, kusiyana kwake n’kuti
amaneyu amavala buluku. Komanso kuvina kwake satumphatumpha ngati
Kadyankhadze uja koma amavina cham’mbali. Kumaso kwake kumakhala kofiira
mochititsa mantha ndipo amayenda ndi nkhwangwa ya katemo, kosiyanapo ndi ija
timadulira mitengo.

Amavala Malaya aatali mmanja ndipo panthawi yovina amayika pansi


nkhwangwa. Atatha kuvina amatola nkhwangwayo. Mavinidwe ake amakhala
osangalatsadi. Nyimbo yake amati, “Koye koye dede! He, Omwale de! Mudatani
Omwale pochoka, koye koye!”

Simoni

Chilombochi chimaoneka pa maliro a mfumu, nduna ndi namkungwi ndipo


chimavina masana. Chovala chija chabuluku chimakhala chasaka ndipo
chimapangidwa ngati chimpinimomwe.

Chimtabwa (Mapulanga)

Nyawuyi imakhala ndi milomo yaitali kwambiri ndi mano aataliatali mbali zonse
ziwiri. Mkamwa mwake mumaoneka ngati moto poyenda ndipo povina
chimatenga misikiri iwiri, n’kumaiombetsa n’kumamveka kuti ngwi, ngwi.
Chimavina mbali zonse ziwiri chakutsogolo ndi kumbuyo.

Kawirikawiri chimavala ngati Simoni, thalauza ndi Malaya aatali manja.


Sichisupidwa kumanja poti m’manja mumakhala misikiri.

26
Namyikwi

Chilombochi ndi choopsa chifukwa cholinga chake n’kudzapha ziweto monga


nkhuku ndi mbuzi. Komatu ziweto zake ndi zapasiwapo. Kupha ziweto zakhomo
lina ndi mlandu. Mlandu wake umakhudza eni chilombocho, makamaka wakunjira.
Chilombo chonse chowedzedwa chisanapite kumudzi chimapatsidwa malamulo,
chikaphonyetsa malamulowo chimalangidwa. Zilombo amawedza ndi mbedza
imene amawedzera zilombo ndipo nyambo yake ndi dzira. Kuwedza zilombo
kumatchedwanso kuvuula.

Palambwe

Chilombo chachikulu mutu, wongoti thasaa. Ndiye pali nyimbo imati, “Bwerekeni
nkhwangwa n’katemere pamutu Palambwe ee! Chitandale ee! Chitandale!” Ena
amati, “Nkhwangwayo, eyaye! Kaliyaliya siyako njobwereka! Pamutu palambwe
aleke wana asewere!”

Kasinja

Pali akasinja amitundu iwiri: Kasinja wausiku ndi wamasana. Kasinja amavala
thupi lonse ndi zigodera zina zam’khosi ndi za m’chiuno, ndipo mavinidwe ake
ndiolingana. Nyimbo zakenso n’zofanana. Mwa nyimbo zake ina amati, “Olekeni
ochoke! Koto koto! Asiyireni mwana yekhayo, olekeni ochoke!”

Kapoli

Maonkedwe ake sasiyana kwambiri ndi a Kasinja. Kapoli ali ndi mawu aang’ono
koma ogalamula kwambiri ndipo mavinidwe ake ndi yokondweretsa. Nthawi
imene chikuvina amachiyimbira salamba, m’mbalimu anyamata
akuchitchetcherera mochizungulira, atavala maseche munthanthula. Amayi
nthungululu zili pakamwa, wosupa akusupa chilombocho komanso uja wa tseche
wotchetcherera.

27
Kapoli

Vinsabwe

Chimavala Malaya amasaka, ndipo mchiuno chimavala zigodera zonyedzanyedza.


Chimavina chakutsogolo ndi chambali. Chingathe kuvina usana angakhale usiku.
Nyimbo ina amati, “Ena azikhala ndi amawo dziko lomwe lino kumanda azinka
ndondo Chautayo wada ine.”

Vinsabwe

Kudambwe

Uku ndi kumalo kumene kumachokera nyawu zonse. Kumeneku ndiko kuchipala
kwa gule wamkulu. Amasankhula ku mtsinje, kukhwawa kapena kumanda. Pa
tsiku loyamba gule mwini maliro amafunsidwa kupereka chakudya cha tsikulo;

28
ndiwo ndi ufa. Dzina lake amati ‘chipondadambwe’, ndipo chakudyachi
chimaphikidwa komweko. Chakudyacho chimakhala cha eni mudzi.

Chimbano

Chimbano

Malamulo a kudambwe

1 Usabe Wakuba ndi mdani wa dziko ndipo chilango


Chimakhala kudulidwa chiwalo.

2 Usaphe Munthu wakupha mnzake nayenso


amaphedwanso.

3 Kulemekeza makolo Munthu wosalemekeza amalangidwa


mwapadera.

4 Usamalire Malangizo amakolo amati chimasomaso chimapha


maso – mapenyapenya amapha maso.

5 Ochita chigololo Magwiragwira amapha manja. Wochita


chigololo onse awiri amaphedwa ndi cholinga chakuti
aononga mudzi. Ndiye kuti zilombo zizingolowa
m’mudzimo.

6 Kunamizira wina Wabodza amamasula mudzi. Wabodza akamuyika


Pabwalo la anyakwawa namuyimika padzuwa payekha
amamusetetsa pa bodza lake.

7 Ndewu Akulu amati ndewu siimanga mudzi.

29
Izi zonse ndizoletsedwa, ndipo sizisiyana konse ndi malamulo khumi aja a
Mulungu.

Masiku ano zinthu zasintha. Wachigololo ndi wakuba sakuphedwa konse. Koma
kale m’malo mwa malamulo amenewa m’mudzi munali bata ndi mtendere, ndi
umodzi. Kusinthaku kwadza chifukwa cha kumvera kwa anyamata.

Mtsikana akapeza bwenzi

Mbeta yamakedzana sankakumana mtsikana ndi mnyamata pamaso ndi pamaso.


Zinkangothera kubwalo kumene amasonkhanako amuna okhaokha.

Akamvana kubwaloko mtsikana amauzidwa kuti amufunira mwamuna. Kenaka,


amamvana zachiongo, komanso chamlomo. Mtsikana uja akakwatiwa, pofuna kuti
asatenge mimba msanga amamuveka mkuzi podikira mkangali. Mosazengereza,
mfumu imasonkhanitsa nduna zake, madoda, ndiponso wakunjira kuti akonze tsiku
lodzameta namwaliyo. Atagwirizana, amaitana namkungwi namuuza za
mkangaliwo. Amaviika chimera kenaka kusalika nkhuni. Pambuyo pake,
amakonoletsa tsokwe. Kuyambira tsiku losalika nkhuni m’paka kutsogolo
chilombo chotchedwa Mjere chimaoneka n’kumazungulira mudziwo mmawa ndi
madzulo.

Akakonola amalengedza tsiku lotsuka kapena lovuula mphale. Tsiku lotsatira,


amalawirira kusinja, tsonotu piringupiringu wazilombo osasimba. Tsiku linzake,
amati lovuula kapena loteleka. Tsiku limeneli amaletsa zilombo kutuluka, poopera
kuti pangaoneke ngozi yogwetserana pamoto.

Patsiku lobwereza (lophikitsa) usiku wake kumadza zilombo monga Nkhandwe


ndiponso Mikango. Zilombozi zimachokera m’madambwe onse ozungulira,
ndiyetu amuna ndi amayi amasonkhana kubwalo n’kumavina gule wakhunju.
Atamwazikana nthawi yomweyo namwali amagwidwa momenyedwa khofi (pama)
kuti alire. Tsono zikatero zilombo zija, Nkhandwe, zimakhamukira kufupi ndi
nyumba kumene namwaliyo wagwiridwa. Zimatero mpaka mbandakucha
(mchilala kucha).

Namwali uja amamuphunzitsa mavinidwe a chisamba ndi umonso azikagonera ndi


mwamuna m’banja, komanso osalephera kumuuza miyambo. Kutacha, amapita

30
naye kumtengo wa anamwali, ukonso kumasonkhana anamkungwi onse amidzi
yozungulira. Namkungwi wapamudzipo, ndiye amatumiza mauthenga.
Anamkungwi aja ntchito yawo ndi yophunzitsa namwali mavinidwe, maphikidwe,
magonedwe, osaiwalanso miyambo.

Mnyamatayonso amaikidwa m’nyumba nasankha phungu. Ukonso amamulangiza


miyambo yam’banja, komanso kusagona ndi mkazi akaoloka. Nthawi itakwana,
amaitanidwa ndi anamkungwi kuti akamuvinire. Amamugoneka chafufumimba,
ndiye anamkungwi aja amamunyamula nayamba kuwakhirana (kuponyerana ngati
mpira).

Pamakhalanso nthawi ina yomuvulira namaimba nyimbo yoti, ‘Taona, taona,


chimkanda aye, aye.’ Chinamwali chisanayambike, mfumu imanenapo zake ndizo
namatula (mtulangala), ngati izi siziperekedwa pakutha kwa chinamwali mkaziyo
amakhala ngati mbeta, ndipo wina atakhala ndi zonse zofunikira amaloledwa
kutenga namwaliyo. Uku amati kuwombola. Woyambayo amapirikitsidwa
pamudzipo nati chinamwali chakanika.

Masiku a mkangali amakhala atatu. Tsiku loyamba amati chiuluulu ndipo mtsikana
amavekedwa kulekeza mchiuno, mawere pamtunda ndipo m’mutu amamuveka luzi
kapena mlaza.

Anamwali

Chingondo chimavekedwa kumutu kwa namwali ngati chipewa chija amavala


mafumu akumangalande. Namwali amakwezedwa pamapewa atamveka
mtemwende (thewera).

Chitengwa

Pamudzi pakafika mnyamata kudzafunsa mbeta ndi kuloledwa, mwambo wonse


umachitika mwadongosolo. Koma mkamwiniyo akakhala nthawi zina amapukwa

31
zopita kwawo. Asadafunse ankhoswe za chitengwa poyambirira amagundana
zifuwa ndi mkaziyo. Akagwirizana amakauza ankhoswe akuchimuna
kudzapempha chitengwa. Asadayankhe, amakhala naye pansi wawo uja.
Atavomereza motsimikiza mtima akuchimuna amaitanidwa nawauza kuti, ‘Nkhani
yanu idamveka chotsatira tipatseni nkhuku yachitengwa.’ Koma ngati mnyamata
amachita zabwino, mfumu pamudzipo imakana kuti mnyamatayo asachoke.

Patsiku lopita kuchitengwa, anzake amamuperekeza kumtengeza ziwiya monga


mtsuko wa madzi, m’phika, mkhate wosambira m’maso, mbale, mithiko ndi zina.

Mtengwa akadwala, nkhoswe zakuchimuna zimachita changu chokanena


kunkhoswe zakuchikazi. Kumudzi kumene kwachokera mkazi kukachitika maliro
kaya matenda, uthenga umatumizidwa kuja, ndipo mwamunayo amamuperekeza
mkaziyo.

Nthawi zina mtengwayo akaona zina zosamusangalatsa amati abwerera kwawo,


apo zikatero ndiye kuti chitengwa chakanika, ndipo nkhuku yachitengwa
imabwezedwa.

Chikumu

Nthawi zina mnyamata amangotenga kapena kukwatira mtsikana kopanda


ankhonswe kugwirizana. Mnyamata amatenga namwali mothawitsana, ndiye kuti
chikumu kapena chisomphole. Patapita masiku angapo mfumu imauza aja
adatenga mkazi uja kuti awadziwitse akuchikazi mofulumira, chifukwa Chauta ndi
mkhungu. Kalata imalembedwa motere:
• Amfumu a Chabwera, kwanuko musafune munthu wakuti; munthuyo
tidatenga ndife.
Ndine,
Mfumu Khombe

Kalata itafika kwa mfumu, akubanja la mtsikana amapatsidwa kalatayo.


Akuchikazi amakonza tsiku lokalondola. Akafika kumudzi kwa mnyamata abale
ake amtsikana uja amapatsidwa moni. Atalandira moniyo, apanjira amati,
‘Tidalandira kalata iyi imene mudalemba.’

Apamudzi amati, ‘Zoonadi, kalatayi tidalemba ndife, tidatenga mlongo wanu.’


Apanjira amati, ‘Tisadanene china chilichonse tiyambe tamuona munthuyo.’
Atamuona amati, ‘Ha, ndi zoonadi ndi wathu.’ Akakhalitsana pansi, apanjira amati,
‘Tipatseni chizulaminga. Mutipatse nkhuku ziwiri.’ Mosazengereza amapereka

32
nkhukuzo. Mawu achiwiri amati, ‘Tipatseni chizungulirakhonde. Mutipatse mbuzi
zitatu, koma cha mfumu mutipatsa nkhuku ziwiri ndiponso chiongo
mutikumbukire bwino lino. Tsonotu ndi msoti wa ng’ombe.’

Zonse zitaperekedwa, apanjira amatsanzika nati, ‘Tsopanotu ife titsata msana


wanjira.’
‘Ayi! Pepani, dikirani chakudya akuphika.’ Atadya amalawirana namapita kwawo.

Akafika kumudzi amakafikira kwa mfumu nalongosola zonse, n’kupereka


chizungulira mfumu. Zina zija monga chizula minga ndi chizungulira khonde
amagawana pachiweniweni, chifukwa pamatenda ndi pamavuto am’banja
amadziwitsana.

Chinamwali (Mkangali)

Ikakwana nthawi ya chinamwali mudzi wonse umakonzekera za mkanagli, poviika


chimera ndi pofuna nkhuni. Zonse zitatha atate ndi anyamata amauzidwa kumanga
mpanda wozungulira bwalo. Mudzi uliwonse umakhala ndi mbali yake yoti
amange. Izi zikatha pamakhala tsiku lofuna tsokwe ndipo m’mawa mwake
amakonola. Atapita masiku angapo, amavuula mphale ija ndi kusinja kapena
kupita nayo kuchigayo. Pamene amagwira ntchito yonseyi n’kuti zilombo monga
Akwakwase ndi Namalocha zikuvina, kusangalatsa anthu.

Atasinja tsiku linalo amayamba mowa, kapena kuti kufulula mowa. M’mawa
mwake amaphika mowa uja. Kutada kumamveka kulira kwa nkhandwe
ponseponse kuti, ‘Bwe! Bwe!’ Ndi kubangula kwa mikango ponseponse. Ichi ndi
chisonyezo choti mawa chinamwali chiyamba. Mithenga imapita kumidzi
yozungulira, ndipo madambwe onse amatumiza nkhandwe ndi mikango
kuchinamwaliko.

Pakati pa usiku, atate ndi amayi, kuphatikizapo asungwana ndi anyamata


amasonkhana kubwalo
lovinira gule. Atasonkhanitsa ng’oma monga mbalule, ndewere, mtiwiso,
mbandambanda, mpanje ndi gunda, ndi kuziwamba ndi moto wazinyatsi, gule
amayamba. Amayamba ndi gule wakhunju. Guleyu zimavina ndi
ntchemberembaya. Atavinavina amaleka ndi kukalowa m’nyumba ndi kugwira
anamwali osankhidwa. Amawapanda makofi ndipo anamwaliwo amalira. Apo
zilombo zimafika kufupi ndi kunyumba ndi kupokosera kwa kulira kwa mikango
ndi nkhandwe.

33
Ena amayimba nthungululu. Izi zimachitika mpaka m’matandakucha. Kutacha,
m’mawa midzi yonse yozungulira mudzi womwe kuli mkangali amakhalira gule
kumadambwe osiyanasiyana. Tsikuli amayi amavina chiuluulu ndipo yemwe
amayamba ndi phungu kapena namkungwi, mafumu ali pa mphasa, ali kuonera ndi
kusupa. Anamwali amavina bwino lake, atayamba amaonera chitsanzo cha
aphungu ndi anamkungwi. Kutada usiku, gule amavina ndi zilombo, monga
Kapoli, Kasinja, Makanja ndi Pedegu.

Panthawi yovina, Kasinja amafika ndi chinsungwi chachitali, ndipo namwali


amauzidwa kugwira mbali ina ya nsungwi. Ndiyetu kumakhala nkhondo yokokana
ndipo pofuna kuletsa nkhondoyi, phungu amapereka choombolera namwali uja.
Zitatha izi namwali amagona m’bwalo. Apo zilombo ziwiri zimavina molumpha
namwaliyo. Amamuwaza chitedze kapena madzi akhonje, omwe amanyerenyesa
kwambiri. Nyimbo yake amati, ‘Namwali akakhala wamwano, timuundireundire.’
Pamakhala zoopsa chifukwa namwaliyo amamupanda kwambiri. Kuti zonse zithe,
phungu uja amadzaombola moperekanso nsupo. Aphungu ena amapereka kapena
kusupa m’malo mwa anamwali kapena makolo.

Gule atatha, zilombo zina pamodzi ndi namwali uja amatsogolera kupita ku madzi.
Atafika uko namwali amauzidwa kusamba. Kusamba kwake kumakhala posamba
m’chiuno, miyendo, nganga kuphatikiza mabere, manja ndi mutu, pomwe kwina
ndi kusamba thupi lonse. Amayi amalangiza namwali masambidwe aziwalo zonse
za thupi lonse lachikazi, uku ndi kuphunzitsa ukhondo. Patsiku lachiwiri
pamakhalanso kuvina mjedza, ndi potsirizira amayi amafikanso ndi namwali kuti
adzavine.

Pathawiyi Chimukoko ndi gule amene amalowa m’bwalo. Chilombochi chitalowa


m’bwalomo, mwinanso bwalo limachepa, amayimba nyimbo namati, ‘Ikadza onani
kuno, tadzaonani ulombo bwalo olanda.’ Namatero mobwerezabwereza. Nsupo
yake ndi mkota wambuzi kapena tonde wa ndevu. Patsiku lotandala chilombo
sichipitanso kudambwe koma chakufupi ndi mudzi, kukhwawa.

Patsiku lachiliza guleyu amabweranso.

Mwambo wa fisi

Anthu amasankha mnyamata mwachinsinsi kuti akhale fisi, ngati namwaliyo ndi
wosakwatiwa, kuti akhale ngati mwamuna wake. Mnyamatayo amatchedwa ‘fisi’
popeza amafika nthawi yausiku yokha. Fisiyo amachoka kumbandakucha, kotero
anthu ena sadziwa za iyeyo. Fisi ntchito yake ndi kuyesa mtsikana za chinamwali

34
chake. Atafika fisi uja amalandiridwa ndipo amagwira ntchito imene wadzera
mpaka masiku angapo, ndipo atatha amapatsidwa malipiro omwe adalonjezana
ndipo zonse zimathera pomwepo. Fisi samaloledwa kubweranso.

Nthawi zina ngati malipiro asowa amati, ‘Fisi akagwira mbuzi sataya,’
amangotengeratu namwaliyo. Komanso angakhale malipiro ataperekedwa,
mnyamatayo amamvana ndi mtsikana kuti lingokhala banja. Nkhoswe zambali
zonse ziwiri zimakumana n’kupatsana zofunikira monga chiwongo kapena
chaliombo. Ena amati ‘kumuonga’ (kuthokoza). Izi zimakondweretsa makolo kuti
kupatukana mbanjamo kwatha ndipo ali omasuka kugonera limodzi pakati pa
mwamuna ndi mkazi wake monga kale. Dzina lina lakupatukanaku amati,
‘dongosolo’.

Koma ngati mtsikanayo sapeza bwenzi mwamsanga izi sizikondweretsa makolo


konse. Tsonotu zimenezi zimasowetsa mtendere m’banjalo. Fisi yemwe amabwera
ngati mtsikanayo sanapeze bwenzi amakhala mnyamata wapabanja kuti adzathe
chinamwalicho. Ndipo mtengo amagwirizaniratu pachiyambi, mwina mkota
kapena tonde wambuzi. Mtsikana amauzidwa kuti usikuwo kubwera mnyamata
kuti adzathe milanduyi.

Mkangali
Chinamwali cha mkangali ndi chinamwali choyamba ndiponso chovomerezeka.
Mkangali ndi chinamwali cha atsikana ndipo chiyambi chake chimakhala chakuti
mtsikana akathyola bano, kapena kutha msinkhu, mfumu imauzidwa kudzera kwa
namkungwi. Ntchembere zimakumana kunyumba kwa mtsikanayo kumuuza ndi
kumulangiza miyambo mpaka tsiku lomaliza msambo. Malangizo ake amatere;
‘Tsopano wakula ndiye osamasewera ndi anyamata kuti ungatenge mimba.
Komanso uzisambira pawekha, ndipo zipangizo zamsambo uzibisa pamalo
pobisika. Nthawiyi imaoneka pa mwezi kamodzi. Ndiye osathira mchere
mum’phika ngati waphika ndiwo pamene amayi ako achokapo, uzituma mmodzi
mwa anyamata kuti adzakuthirire mcherewo mum’phikamo.’

Zikatero namkungwi amakatenga mankhwala kwa mfumu otchedwa ‘khundabwi’


namumwetsa mtsikanayo. Msambo usanathe, saloledwa kutuluka, komanso
amalangizidwa kuti akakumana ndi mfumu azipaza kutali. Zikatere, makolo a
mtsikanayo amapatukana malo: bambo amagona pathala lalikulu ndipo mayi thala
laling’ono.

35
Nyumba zakale zidali zandendera tsopano pakati panyumbayo amaika mnzati
wochirikiza nyumbayo, komanso amakumba kadzenje kuti azisonkhapo moto
wophikira. Kadzenjeka dzina lake ‘dziko’, ndiye mbali zinazo kudzanja lamanja
limatchedwa ‘thala lalikulu’ ndipo lakumanzere ‘thala laling’ono.’ Mbali imene
mayi amakhalako pophika nthawi itakwana yogona onse awiri, mwamuna ndi
mkazi wake, amagona thala lalikulu.

Kuombetsa namwali m’manja

Patapita masiku angapo limakhalapo tsiku lokawonetsa namwali kwa makolo ake
(kuombetsa m’manja). Atayandikira kunyumba, phungu pamodzi ndi namwali uja
ndi ena operekeza amaomba m’manja mumvekere, puuu!Puuu! Puuu! Atafika,
amalandiridwa ndi makolo anamwali uja. Ndiye imeneyo ndiyo nthawi yoti
makolo apereke malangizo awo monga motere:
‘Tiyankhulenji, ndalama yanga ndi iyi. Lero mwakula musadzachitenso utchisi
(uve, kapena kukana kutumidwa), musamapisanso mum’phika ayi. Muzindidikira
mpaka n’tabwera, chifukwa mudzachita masaya ndipo pakamwa padzakhala ngati
pakamwa pa nsupa. Tikakuyitanani, muzigwadanso.’

Mjere

Nyawu imeneyi imatuluka pa mkangali kuyambira tsiku losalika nkhuni, lotola,


lofuna tsokwe, kukonola, kuvuula mpaka tsiku losinja. Mwachidule, tinganene kuti
amatuluka patsiku loyamba mpaka tsiku lakutha kwa gule. Nyimbo yake amati:
“Nyama, nyama, nyama.”
Othirira amati:
“Nyama yakwera mtunda, yasiya alenje mayendedwe ake ndi liwiro
lokhalokha.”

36
Mjere

Ntchito yeniyeni imakhalapo panthawi yosambula mowa wa mpalo kapena mmeto.


Patsikuli Mjereyu amalawirira m’mamawa nazungulira mudzi wonse
mobwerezabwereza. Masana potuluka Njovu, iye amatsogolera Njovuyo mogwira
chitamba, mzongo wanyama atakoloweka paphewa mpaka kumudzi. Njovu itatha
kuvina m’bwalo nipita kukagona, Mjere uja amabwerera kubwalo komwe kuja
ndipo amamuimbira nyimbo navina mpaka kusupidwa kokwanira. Amabwerera
kuja kogona Njovu. M’mamawa makamaka m’matandakucha kuli mbuu Njovu
imavinanso, Mjere ali m’khundumu madzulo. Dzuwa lili kutsetsereka, Njovu ija
imavinanso motsiriza n’kumatsata msana wanjira, kubwerera kudambwe komwe
idachoka. Pa nthawiyi, Mjere amakhala patsogolo atagwirira chitamba.

Chimkoko

Nyawuyi maonekedwe ake ndi olingana ndi makala. Chimenechi amasaka ndi eni
mudzi, ndichonso chimayambirira kuvina. Tsono ng’oma zili m’bwalo amayi
atadzanso moyandikira bwalolo mwadzidzidzi amangoona kumbuyo kwawo
chilombo chawazingira ndipo amasowa kothawira.

Chinamwali chopinda

Nthawi zina namwali amakhala asanakule. Tsono popeza namwali amafunika


kumeta akathyola bano ndiye mfumu ndi makolo amagwirizana kuti mtsikanayo
amete. Mtsikanayo amameta ndipo palibe chimaphonyedwa potsatira mwambo wa
chinamwali monga kuvina gule wamkulu ndi chisamba. Komatu kupindaku
mtsikanayo sakhala ndi mwamuna ndipo mtulangala superekedwa pokhapokha
atadzakwatiwa, ndiye wodzamukwatirayo amauzidwa kupereka mtulangala.

37
Chisamba
Chamba chimenechi ndi cha amayi okha okha. Tsiku limene pamudzipo wina
wamwalira ndipo ngati pakhale gule wamkulu namkungwi amapita kumidzi
yozungulira kukamema anamkungwi anzake, kuwadziwitsa za chisamba
chodzachitika usiku wa tsikulo. Chidziwitso chake amapereka thonje ngati kalata
yachidziwitso. Madzulo amayi onse amasonkhana ndipo onse amalowa msiwamo,
n’kuyamba kuvina mozungulira mtembo uja. Dzina lake amati kulonjera maliro
ndipo ololedwa ndi okhaokhawo amene adameta, osameta amatulutsidwa.
Amavina kanthawi kenaka n’kuleka napumulira. Akatha kudya chakudya
amayambiranso kuvina usiku wonse. Pamene chisamba chilli m’kati, gule
wamkulu amakhala m’mbalimo nachezera. Gule wake ndi monga Kasinja ndi
Kapoli.

Ngati pali anamwali, amawavinitsa ali pamapewa pa aphungu awo. Wosenza


namwali amatchedwa phungu. Iyeyu amakhala limodzi ndi namwaliyu nthawi
yonse kuyambira usiku uja mpaka kuchotsa maliro. Ndiye phungu amalandira
nsupo zonse zimene namwaliyo akumusupa kukhala ngati malipiro ake. Komanso
amaphunzitsa namwaliyo kamzunguze(kuyankhula mochita lipoti). Zimene
amaphunzira ndi ometa okhaokha, chitsimikizo choti wakula ndithu.

Namwali wakugwa m’chinamwali

Pamakhala atsikana ena amene adangolowa m’banja asanamete. Iwo amakhumbira


anzawo aja akuvina m’bwalomo. Iwo amalowerera m’gulu la amayi ndiye
amamugwira, namukhazikitsa pansi, mosazengereza namkungwi amakadziwitsa
mfumu. Zitatero zonse zokhudza chinamwali amauzidwa n’kuyamba kuvina nawo
chisamba. Mtulangala umaperekedwa.

Amuna akugwa m’chisamba


Pamene gule wachisamba ali m’kati, malinga ndi mavinidwe, amuna ena
amatengeka mtima. Mwadzidzidzi amalowa m’kati mwa amayi aja ndipo
amamugwira, namukhazikitsa pansi. Kenaka mfumu imadziwitsidwa ndipo
ikavomera amam’patsa mwambo wachisamba, n’kumupatsa nsalu yovinira
chisamba. Zikatero iyeyu amalowa ndithu ndiye nthawi zonse pakakhala mwambo

38
iye amaitanidwa n’kumavinira limodzi ndi amayiwo ndiponso n’kuchezera limodzi
ndi amayiwo.

Tsonotu zikatero mavuto amakhala pa phungu uja. Ndiye phungu uja amayenera
kumvetsa zonsezi ndipo kutacha amamuitanira pambali naonjezanso malangizo
aja. Kenaka amamuchenjeza kuti ayenera kukwaniritsa malangizo onse aja. Koma
akakhala mwana womvera, waulemu, wotumika, ndi wosapisa mum’phika, makolo
aja amangoti, “Tilibe mawu ambiri, pitirizani makhalidwe omwe aja. Chifukwa
kalitengera adaoletsa mazira ampheta.” Zikatere phungu zimamukondweretsa
kwambiri.

Koma ali m’tsimba akamangoonetsa chisawawa zitchetche mutu wonse, pamenepa


anthu amadziwiratu kuti ameneyu ndi nkhutukumve (puludzu). Akunjira
kuphatikizapo phungu uja amaonetsetsa kuti namwali uja akutsatiradi zonse
adauzidwa (adalangizidwa). Ngati akukana kutumikira makolo, kapena ena
achikulire amamuuza kuti, ‘Iwe usamale tidzaonana podya mphonda.’ Mawu
amenewa atanthauza kuti, ‘Tidzaonana panthawi imene kudzakhale gule wamkulu
kudambwe.’ Chifukwa kumatalikira ndi kumudzi ndiye atamenyedwa, ngakhale
alire, sangathe kumveka.’

Kutacha pamakhala nthawi yotulutsa chisamba ndipo amavina mozungulira


pakhomo pasiwapo. Mfumu ndi onse apamudzipo amasupa nsupo mothira
m’nsengwa kapena m’mbale. Zosupidwazo zimatengedwa ndi namkungwi
wapamudzipo nakhala nazo poduka mphepo n’kugawana mofanana. Kenaka onse
amayamba kumwazikana kupita m’makomo mwawo kukaphikira abambo
akwawo. Zitatero amasamba koma osadzola mafuta popeza ali pachisoni,
amabwereranso kusiwa kuja n’kuyambanso kuvina. Wogona kunyumba
sakondwera naye amati ameneyo wagona pofunda pamene iwo agona pamphepo.
Ogona kunyumba zawo amaloledwa koma sapatsidwako nsupo zonse zosupidwa.
Panthawi yoti maliro achotsedwa, uthenga umatumizidwa kwa mfumu kuti mudzi
watha. Mfumu imaitana amene amakhala ndi amayi kophikira ziphiko namufunsa
ngati ziphikozo zaphikidwa, kapena ngati chakudya chakonzedwa. Pamakonzedwa
dongosolo lakuti mwina chakudya achidye maliro asanaikidwe.

Maliro asadaikidwe gule wachisamba amatulutsidwa ndiye mafumu onse amapita


m’bwalomo kukasupa. Atatuluka apo gule wamkulu amavina, akatha mtembo
umanyamulidwa kulunjika kumanda. A gule wa chisamba amatsatira mtembowo
akuvina. Kumandako amayi aja amapitiriza kuvina mpaka ntchito yakumanda
itatha. Akabwerera kumudzi mafumu ozungulira amalawira kwa mfumu inzawo
nati, ‘Ha! Pepani bakhumatani tizionana.’ Si bwino mafumu kuchoka osalawira.

39
Alipo ena apuludzu amene sapita nawo ku maliro oterewa amangopenya
mosaganiza kuti tsiku lina iyenso adzafa. Tsono chakudza sichiimba ng’oma,
mosayembekezeka mwina maliro amamuonekera iyeyo. Uthenga utafika kwa
mfumu onse amauzidwa nasonkhana pasiwapo. Akakhudza, mfumu imalamula
kuti anyamata apite kuthengo(kumanda), tsono opita kuthengo amati, “Ife njira
yakumanda sitikuiona atilozere ndi iyeyu.” Izi zitanthauza kuti iyeyo sapita
m’maliro, umenewu umakhala mlandu. Mwina amatchera pokaika maliro ndipo
amati adzafotsere yekha.

Dambule
Chaka chilichonse pamakhala mwambo wolambula manda. Wakunjira amauzidwa
ndi mfumu kuti tsiku lakutilakuti tidzalambure manda. Amayi onse amakonzekera
ziphiko zodzadya patsikulo. Litakwana tsikulo onse amasonkhana kudambuleko,
komatu tsikulo lisanafike wakunjira amasamutsa zilombo zonse nakaziika kwina.
Amalambula kwakuti moto usadzalowemo. Ana osameta ndiponso atsikana
osakwatiwa ndi kumetedwa saloledwa kulambula nawo.

Ntchito yonse itatha ziphiko zimasonkhetsedwa pabwalopo. Ziphikozo amazigawa


magulu atatu. Gulu la ndoda zokhazokha zimene zili ndi zidzukulu, achinyamata
ndi amayi. Chakudyacho chimagawidwa mwadongosolo. Nthawi zina
pamaphikidwa mowa woti udzamwedwe patsikulo, womwe umagawidwa kwa
anthu amidzi yozungulira. Gule wamkulu saloledwa kuvinapo. Mwina manda ena
amadirizika ndipo pa pnthawiyo amawakonzanso powafotesera (kukwirira).

Kumanda kuli zigawozigawo. Gawo loyamba limakhala labanja lachifumu. Manda


amafumu amaikidwa m’nyumba kapena pabwalo la gule wamkulu. Chigawo china
ndicho cha anthu wamba aamuna ndi aakazi omwe. Ndipo chigawo china ndi
alendo monga cha akamwini ndi atengwa. Palinso manda ena amene ndi a ana
aang’ono maka ofera m’chikuta. Kumanda amenewa amuna saloledwa koma
ntchembere zokhazokha. Maliro ake amanyamulidwa ndi ntchembere popita
kumandako. Dzina la manda amenewa amati manda ansenye. Amuna sapitako
chifukwa pali chikhulupiriro chakuti mwamuna woponda pamanda amatupa
miyendo kotero amayi amadzikumbira okha n’kuikanso okha. Ziphiko zimakhala
zakudya ntchembere zokhazokha. Zonse zikatha amamwazikana ndipo sagona
pakhonde. Wolira amakhala mayi wa mwanayo ndipo ena onse salira ngakhale
bambo wamwanayo saliranso.

40
Pali chikhulupiriro chakuti munthu akafa amauka chinthu china monga fisi,
kambuku, insa, mkango, mvuwu ndi zina. Makolo adakhulupirira kuti Chauta,
Mphambe, Chisumphi, Leza sapha munthu koma mfiti ndiyo imachita izi.
Chifukwa cha chimenechi pamatenda ndi pamaliro amagwirana ufiti. Palinso
chikhulupiriro chakuti mzimu wamunthu wakufa umabwereranso kumudzi
n’kumacheza ndi anthu amoyo powalotetsa maloto.

Namwali akatha msinkhu


Pamene namwali wam’banja lina ali pafupi kutha msinkhu, makolo ake
amapatukana malo. Amachita izi podziwa kuti ngati satero apha mwanayo.

Tsiku lakutha msinkhu namwali, amayi amasonkhana nakhala naye masiku atatu.
Panthawiyi iye saloledwa kutuluka, koma nthawi yausiku yokha. Ngati namwaliyo
anali wosakwatiwa, makolo ake amafuna munthu womakakhala ngati mwamuna
wake masiku ena. Munthu wotere amatchedwa ‘fisi’ popeza amafika nthawi
yausiku yokha ndipo anthu ambiri samadziwa. Iye amachoka usiku kapena
kum’bandakucha. Makolo a namwaliyo amapita kwa mfumu ndi nkhuku nati,
“Mwana uja wakula.” Amatero kuti mfumuyo ipatukane ndi mkazi wake kuopa
kuti angadule namwaliyo, ndiponso kuti mfumu ifune mankhwala oti namwaliyo
azadye. Chinanso ndi chakuti ngati mfumu ili ndi mzinda izikhala itadziwa kuti,
chaka chino ndimeta namwali pabwalo langali. Itafika nthawi yometa, namwaliyo,
ankhoswe akuchikazi amapita kwa ankhoswe akuchimuna nawauza za chinamwali.
Mwamsanga akuchimuna amasonkhetsa chuma, mbuzi, nkhuku, mphasa ndi zina
zoyenera pa chinamwali. Izi zonse zimaperekedwa kwa mfumu. Dzina lake la
chumachi amati, ‘mtulangala’, ndipo mfumuyo imagawana chumacho ndi
amalume ndi makolo ake a namwaliyo.

Patsiku logwira namwali amayamba kufulula mowa, ndipo patsiku lophika,


madzulo, amayi ndi amuna amakhala otanganidwa kukonzekeratu za
chinamwalicho.

Madzulo kumamveka kulira mawu onga a nkhandwe ndi mkango. Mkangowo


umapangidwa ndi chingwe ndi thabwa, akalizunguza apo pamamveka ngati kulira
kwa mkango. Nkhandwezo zimapangidwa ndi ting’oma tazipanda (madende)
ndipo polira kumamveka kuti, rwe!Rwe! Rwe! Mwina bwe! Bwe! Bwe!
Panthawiyi amayi amaitana namwali kuti alowe m’nyumba m’mene muli amayi
ena. Atalowa amam’menya pama, ndipo atalira, nkhandwe ndi mikango zimafika
pafupi ndi nyumbayo. Zimatero mpaka m’mawa ndipo amayi amaimba
nthungululu usiku wonse. Kukacha, amuna amapita patsinde lamtengo, natcha

41
mtengowo ‘Mtengo wa namwali’ namavina chisamba ndi namwaliyo. Kumtengo
wa namwali kumakhala malango ndi mavinidwe ake. Panthawi yamadzulo amafika
amuna kudzavina mnjedza ndipo amayi amafikanso kubwaloko ndi namwali
atangomveka thewera ngati mbusa (mnyamata wolisha ng’ombe), mawere ndi
matako akuonekera.

Tsiku limene namwali amavina kapena kavinidwa amati, ‘Chingondo’. Namwali


amaoneka mosiyana ndi kale, amavala ntchekwera ngati mwamuna, komanso
mkanda kupingisitsa pa mtima ndi kumbuyo ndiponso kumutu amaikako chinthu
choyera ndi cholukidwa mwaluso, mwina mofiira, mwakuda ndi moyera
kuzungulira mutu wonse. Nthawi zina amavina yekha pansi, koma nthawi zonse
amavina ndi namkungwi yemwe amayamba kuvina momutsogolera. Namwaliyo
amakwezedwa pamapewa atamuika nsengwa kukamwa.

Tsiku lotsiriza amamuyendetsa namwaliyo pakhomo panyumba za anansi pamodzi


ndi kwa mfumu. Koma mwamuna wa mkaziyo amangokhala wosatuluka konse
kubwalo.

Panthawiyi amayi amafika ndi namwali pakhomo lake naimba nyimbo nati,
“Tayalani maye. Tayalani maye, tayalani maye, tayalani mphasazo, namwali
agonepo.” Mwamsanga namwali wamwamunayo amayala mphasa ndipo namwali
wamkaziyo amagonapo. Amayi amaimba ng’oma ndi nyimbo zawo pamphepo,
ndipo namwali wamwamunayo amawafupa. Patsiku loshambula mowa kapena titi
kuviirira zimafika nyawu zovina masana. Mayina awo ndi awa: Chabwerachaona,
Kachipapa, Kavinsabwe, Njovu ndi Jere.

Kavinidwe
M’njovu amalowamo ndi ankhoswe akuchikazi awiri ndi akuchimuna awirinso
atasenza chimtengo.
Potsiriza mfumu imapereka mbuzi ndi mphasa kwa Njovuyo ndiponso chikatiko
(mbiya) chamowa. Atatha izi amameta, ndipo pamakhala tsiku lokavinira namwali
wamwamuna. Atatero anamwaliwo amaloledwa kugona pamodzi.

Malango kwa namwali

• Mkazi amamva nkhwali. Ndiko kutanthauza kuti pamene nkhwali imalira


m’mawa iye azidzuka naphika kapena kusinja.
• Mwamuna uzimpenya kumimba popeza nkhope siisinthika. Kutanthauza
kuti azidziwa njala ya mwamuna wake nthawi zonse.

42
• Mwamuna akakhala kubwalo kwa anzake, ndipo ngati iwe waphika
chakudya uzituluka pabwalo ndi kutsokomola kuti mwamunayo adziwe.
Koma ngati mwamuna sadziwa ichi, ali ndi mlandu.
• Mphotho zonse za pachinamwali zimene zimapatsidwa kwa mkaziyo ndi za
phungu wake wa namwaliyo.
• Mkazi kapena mwamuna akachita chigololo amadula mnzake.
• Tsiku lovinira mwamuna amavina chomuzungulira namamuimbitsa; ngati
alakwa ndiye kuti chakanika chinamwalicho.
• Ntchembere ziwiri zimati mwamuna akachoka mkazi osamameta tsitsi,
ndipo ngati ameta amatsimikiza kuti amachita chigololo. Ndi
chimodzimodzinso mwamuna akameta tsitsi mkazi akachokapo.
• Nthawi zonse pogona namwali amaimba nyimbo yolaula, ndipo ngati
mwamunayo imulaka, apo chinamwali chamulakanso.
• Tsiku loyamba kulowa panyumba amapha nkhuku yophikira kumodzi ndi
mankhwala. Poika mankhwalawo mum’phika mwamuna ndi mkazi
amagwirizana akuimba nyimbo.
• Ana saloledwa kudya nawo nkhukuyo koma eni okhawo.
• Ngati mkaziyo akudwala matenda achikazi sayenera kuphika madzi osamba
mwamuna.

Namwali wamkazi amauzidwa kuti akakumana ndi mwamuna wosayamba


kuyankhulana naye mpaka atamupatsa mkanda. Akakumana ndi mfumu azigona
pansi mpaka mfumuyo itapyola.

Mfumu imachita dongosolo kuti anamwaliwo ingawadule. Chimodzimodzi makolo


a anamwali amachitanso choncho.

Pasanathe masiku ambiri mwina kumamveka kuti mmodzi mwa anamwaliwo


akudwala, kaya akusanza magazi. Namkungwi amapita kwa mfumu nati,
“Mwasunga bwanji anamwali?” Ngakhale mfumu samanena kuti sadawasunge
bwino anamwaliwo, komabe izi sizimakhulupirika ndipo onse amangoti mfumu
yadula namwali. Pa nthawiyi mfumu imakhala ndi nkhawa podziwa kuti ili
pamlandu woopsa. Chikhalireni mwina amadziwa kuti namwaliyo sadam’dule
konse.

Mwadzidzidzi mwina kumamveka kuti namwaliyo wamwalira ndipo anthu onse


maso amakhala pa mfumu kuti yadula namwali. Amapitanso namkungwi kwa
mfumu nati, “Namwali uja watsirizika monga ndidabweranso tsiku lija kudzanena

43
kuti namwali akudwala.” Mfumuyo mwachisoni imangokhala chete podziwa kuti
anthu aziganiza kuti ndiye wapha namwali koma chikhalirecho si choncho.

Akatsuka maliro ndi kudzoza mafuta, anthu onse amalira. Amuna amasonkhanitsa
makasu napita kukayamba kukumba manda. Akazi amasinja mphale kuti aphike
nsima ya amuna ogwira ntchito kumanda. Mandawo amakumba kwambiri.
Atamaliza zonse amapita kumudzi kukanyamula mtembo. Amaikanso pamodzi
miphika, nsengwa, mithiko, zipande, ndi zina zonse, monga mwa katundu
wachikazi, zomwe ankagwiritsa ntchito.

Atamaliza kukwirira amapita kumadzi kukasamba ziwanda, akazi kwa okha


ndiponso amuna kwa okhanso. Atafika kumudzi amawaula makasu kuti ziwanda
zipse ndi moto.

Pometa amavinanso nyawu masiku awiri, ndipo amatuluka pamtandapo. Koma


mwina eni namwaliyo amachoka pamudzipo, kuti mfumu yapha mwana wawo.

Mkazi wachitengwa

Za machitidwe a chitengwa zakambidwa kale pamaliro a mwana wamtengwa.


Mkaziyu akadwala nthawi zonse, ankhoswe akuchimuna ayenera kukadziwitsa
ankhoswe anzawo akuchikazi. Koma popeza izi zalembedwa kale mpofunika
kunena pang’ono za chitengwa chobana, chomwe ndi chosadziwika ndi anthu.

Mwina kumakhala kuti makolo a mkazi kaya a mfumu amalongolola, namati


mnyamatayo sagwira ntchito yachipongozi. Pa chifukwa ichi, mnyamatayo
amakadziwitsa ankhoswe ake nati, “Ine kumene ndikukhala, apongozi
amalongolola kwambiri masiku onse, choncho mukandipemphere chitengwa.”
Ankhoswe akuchimuna amakumana ndi ankhoswe anzawo. Atafika amapatsidwa
moni, nati, “N’kwambwino?” Iwo amati, “Inde n’kwabwino.” Nanga
mwangodzatichezera?” Akunjira amati, “Inde tadzakuchezerani.” Ndipo mwini
mudzi amati, “Uwo ndi ufulu wokhawokha.”

Wakunjirayo amaonjezera mawu ena nati, “Chobwerera kuno n’choti mutilole


kutenga chitengwa.” Nkhoswe yakuchikaziyo imati, “Imani ndikafunse makolo a
mkaziyu.” Atapita uko nasimba nkhaniyo, makolowo amati, “Ife sitifuna kuti iye
n’kutengedwa chitengwa popeza mwanayu ndiye mzime (womalizira kubadwa).
Nanga iye akapita uko ife adzatisinjira ndani popeza kuti ife nkhalamba?” Mawu
onsewa amauzidwa kwa nkhoswe yakuchimunayo. Atapita kwawo amauza

44
mnyamatayo kuti chitengwa chakanika. Panthawiyi mnyamata samakhala
wosangalala pokumbukira mavuto amene iye amawaona.

Mwakuyesayesa amafunsa mkazi wake nati, “Ine pano sindifunapo; ndidayesa


kupempha chitengwa koma alongo ndi makolo ako adakana. Nanga iwe utani?”
Mkaziyo amayankha nati, “Pepani musaope chikwanje chifukwa amachita kusula.”
Mawuwa amatanthauza kuti, ‘Musade nkhawa, ine nditha kupita kwanu
mosavuta.’

Mayankhidwe amakondweretsa mnyamatayo, ndipo mwachinsinsi iwo awiri


amatengana napita kwawo kwa mwamuna. Ankhoswe akuchimuna amakhala ndi
nkhawa podziwa kuti mnyamata waputa milandu. Ankhoswe akuchikazi salondola
mkaziyo popeza amadziwa kuti chakudza sichiiimba ng’oma. “Iye akuti wachoka
pano koma chidzafika chinthu china choti chidzafuna ife nkhoswe zakuchikazi;
monga maliro, matenda, ndewu ya pabanja ndi zovuta zina zotere, koma ife
sitidzalola konse.” Kotero, m’banjamo mukaoneka matenda, mwamuna amachita
mantha kunena kwa eni mkazi.

Mwatsoka mkaziyo amamwalira. Zitatero mudzi wonse umachita mantha podziwa


kuti sadziwa chomwe eni mkaziyo adzanena. Ndipo amasonkhana napangana
chomwe angachite pokanena. Akapangana, amatha kutuma mnyamata wokanena
zamalirowo.

Pokanena, mwina amaima panjira naitana dzina la mlongo wake wa mkaziyo nati,
“Mlongo wanu wamwalira pamudzi wakuti!” Amatero poopa kumenyedwa ndi
anthu apamudzipo. Akumvawo amapangana nati, “Tisakhale tiyeni, ukakhala
mlandu tikakamba komweko.”

Pofika kufupi ndi mudzi amaima kunjira namalira. Eni mudziwo amapita ndi
mbuzi yoti anthuwo alowe m’mudzimo. Akalandira amalowa m’mudzi
mwankhondo, koti atha kumenya munthu.

Akamaliza amakhala pansi. Akapatsidwa moni, akunjirawo amati, “Kodi wathu


tinkafuna uja muda’mtenga ndinu kuti mudzamuphe kuno?” Apamudzi amayesa
kupepesa nati, “Pepani ichi sichidachitike ndi munthu, koma Mphambe.”

Ndipo akunjirawo amati, “Chabwino tipatseni mbuzi yotidziwitsa kuti wathu ali
pano.” Ndipo amapatsidwa. Akatero amati, “Chabwino, tsopano tipatseni mbuzi
ina yakuti maliro atuluke.” Mwamsanga amafuna mbuziyo nawapatsa, nadulanso
mkanda wovomerera mlandu. Maliro otere mwina amanyamulidwa ndi eni napita

45
nawo kwawo. Akaika maliro amabweranso patsiku lometa kumudzi kumene
mkaziyo adamwalilira.

Akafika amati, “Tafika kudzatsiriza nkhani yathu ija.” Eni mudziwo amati, “Izo
nzoona popeza uwu ndi mwambo wakale.” Aja amasonkhanitsa chuma
nachipereka kwa eni maliro. Koma ngati chasowa amayesa kudandaula kuti,
“Pepani mutikhululukire kwinaku popeza tayesetsa uku ndi uku, koma sitidapeze
chuma chokwanira.

Ndipo eni maliro amati, “Kodi mumachiyesa chapafupi kutenga mwana wa eni
n’kubwera naye pamudzi wanu; sikuba kumeneku, kodi? Ngati mutipatsa chuma
chosakwanira ife sitilandira.” Apamudzipo amayesanso kubwereka chuma kwa eni
omwe ali nacho, napereka chikapezeka chokwanira.

Amapitanso kumadzi nakasamba, nabwera, ndipo amayi amaphika chakudya


chotulukira pakhonde. Amatenganso malumo nametana mipala. Pochoka
amapempha chimwerana mowa, ndipo akawapatsa amapita mwachimwemwe.

Mkazi akakhala ndi pakati


• Mkaziyo saloledwa kuthira mchere mum’phika kuti angadule omwe adye
ndiwozo.
• Mwamuna sayenera kuyenda moipa ndi akazi ena kuopera angadule
mkaziyo.
• Mwamuna azidziwa kuti, panthawiyi mkazi amayankhula zopanda pake,
mwina zopsetsa mtima, ndipo mwamunayo sayenera kum’menya popeza
amatero chifukwa cha katundu amene ali naye.
• Mwamuna sayenera kumayenda kutali panthawiyi.
• Chifukwa chakudwala kumene, mwamuna azigwiranso ntchito zachikazi
angakhale sikoyenera kwa iye.
• Mkazi wapakati saloledwa kuonera nyawu chifukwa makolo amaganiza kuti
iye atha kudzabereka mwana wonga chinyawu.
• Mwamuna saloledwa kuona mmene mkaziyo akuchirira, koma ayenera
kubwera anamwino akachoka. Ndiponso mwamuna amapatsa anamwinowo
chuma popeza kuti iwo adagwira ntchito.
• Asanachire mkaziyo, amafika anamkungwi ndi ntchembere zina ndi
kumuvinira pomulanga zina.

Maliro a mkazi wosiya mwana pobereka

46
Pamaukwati nthawi zonse pamakhala ankhoswe oyang’anira zovuta za mabanja.
Amayi ndiwo amadziwa kwambiri maonekedwe ndi mayendedwe a anamwali.
Ndiko kunena kuti pamene namwali ameta, monga tanena kale, amayiwo
amaonetsetsa banja latsopanolo. Iwo akaona kuti mkaziyo ndi wotopa,
mwamsanga ankhoswe akuchikazi amauza namwaliyo kuti afulule mowa
woonerana ndi ankhoswe akuchimuna. Ataphika mowawo amaitana ankhoswe
akuchimuna, nati, “Bwerani kuno kuli mowa wachinkhoswe.” Atafika aja
amawadziwitsa kuti wanuyu adalasa, kutanthauza kuti mkazi wake ali ndi pakati.
Mosavutika ndi kuyankha akuchimuna amavomera.

Pakapita miyezi, pamene mkaziyo nthawi yobala yafika, mwamunayo amatuluka


m’nyumabamo, ndipo azamba amafika kudzathandiza wodwalayo. Pobala mwina
mkaziyo amamwalira asanabereke konse.

Ngati mkaziyo amwalira nthawi yobereka isanakwane malirowa amatchedwa


‘nthumbi’. Atamaliza kutsuka malirowo amalira. Atatero amatumiza mithenga
yokanena malirowo kumidzi yozungulira ndi kwa ankhoswe akuchimuna. Atamva
ankhoswe amadziwa kuti kuli milandu yoopsa ndithu.

Atafika uko amalira nakakhala kumene amuna a pamudzipo ali. Uko amawapatsa
moni, nawafunsa kuti, “Mwamva zoipa?” Ajawo amati, “Eya!” Eni mudzi amati,
“Monga tidakuuzani kuti wanu adalasa, koma lero nyama yolasidwayo yafadi.”
Akunjira amati, “Inde, izo zamveka koma wangolakwa ndi Chauta.” Eni mudzi
amati, “Tipatseni mkanda wovomera mlanduwu.” Ndipo akunjirawo amapereka
mkandawo. Ankhoswe akuchikazi amauza anyamata a pamudzipo kusonkhanitsa
makasu ndi kupita kumanda. Akukumba mandawo ankhoswe aja amakamba
nkhaniyo. Ndipo amapereka chotulutsira maliro, chomwe chikhala mbuzi imodzi.

Poika maliro amanyamulira pachithatha, nasenza anthu anayi, akazi akuimba


ng’oma zachisamba. Amuna otenga maliro amazungulira nyumbayo katatu
mwaliwiro. Atatsiriza amatenga maliro nawanyamula pamapewa.

Amapita kumanda mwaliwiro. Maliro otere madoda ndi amayi apakati amalira
mowafulatira monga mwa miyambo ya Achewa.

Atafika uko amangoika m’dzenje osakwirira namwazikana. Mmodzi mwa


amunawo amauzidwa kutumbula malirowo. Amachita izi poopa kuti ngati
satumbulidwa mtundu wonse wa mkazi womwalirawo udzafa ndi nthenda
yanthumbidwayo. Munthuyo amalowa m’dzenje napyoza maliro ndi mpeni
wanthungo. Akamaliza amachoka msanga napita kutali; uku akumaliza mluzu

47
(khweru) ndipo amuna omwazikawo amadziwa kuti wakufayo watumbulidwa
ndithu. Tsono anthu amafika nayamba kukwirira malirowo. Atatha amapita
kumadzi kukasamba ziwanda; pobwera kumudziko amawaulanso makasu.
Amagona pakhonde masiku ena natuluka patsiku lometa.

Patsiku lometalo ankhoswe akuchimuna amapereka mbuzi makumi awiri kapena


kupitirirapo monga mwakufuna kwa eni mkazi womwalirayo. (Onani m’buku la
‘Mbiri ya Achewa’ za Mazengera ndi Mdzinga.) Munthu uja wotumbula maliro
amapatsidwa mbuzi. Pometa, makolo a wakufayo amati, “Wanuyu tengani,
timam’konda kukhala, pakadakhala wina mkazi tikadampatsanso.” Atatero
amapereka muvi naperekanso chimwerana mowa.

Munthu wakhate
Nthenda yakhate idadziwikanso kalekale pakati pa Achewa ndi kuopsa kwake.
Koma makhwala ndi malewedwe ake sadadziwike. Nthendayi imafala
mumphweya timapuma. Imafalikira anthu amene alipafupi ndi odwalayo monga
ana, mwina n’chifukwa amanenera kuti ndi nthenda ya pamtundu. Ndipo nthendayi
imakhala nthawi yaitali isanayambe kuonetsa zizindikiro.

Itakwanira nthawi nthendayo imayamba kutulutsa zizindikiro m’mphuno,


pamiyendo ndiponso m’malo ena. Panthawiyo anansi ake ndi ena onse
samuyandikira, popeza amachita nyansi ndi zilonda zake.

Koma ngati wodwala nthendayo ali ndi banja lake, banjalo limakhala naye
pamodzi ngakhalenso ana ake omwe.

Anthu odwala nthendayi amakhala nthawi osafa msanga, koma ziwalo zina
zimaduka monga zala, mapazi, ndi zina. Zikatero munthuyo amakhala wozunzika
ndiponso wosalimva kukoma dziko lino lapansi. Ichi chimaipira anansi ake nati,
“Akadayenera kufa msanga ndithu.” Ndipo chifukwa chosafa msanga apo amatcha
nthendayi dzina lakuti, ‘Nthenda yalizunzo’.

Nthendayi sadaikhulupirire kuti njopatsirana. Makolo athu amati nthendayi ili


kumtundu. Koma mwinadi zimachitika choncho, chifukwa choti munthu wakhate
amayandikanadi ndi anansi ake, ndipo nthendayo imafikiradi kwa ana ndi anansi
ake msanga. Makolo athu sadakhulupirire kuti anthu ena apadera angathe
kugwidwa nayo. Koma popeza kuti nthendayi njopatsirana monga timawerengera
m’mabuku amene adalembedwa ndi akatswiri, nthendayi imakulirakulirabe ndipo
mwadzidzidzi munthuyo amamwalira nayo. Pamaliropo samalira ayi, amangokhala

48
ndi chisoni chokha komanso chimwemwe podziwa kuti munthu azunzika nthawi
yaitali. Pokumba manda amangokumba pang’ono, ndipo atamaliza amachoka onse.
Anansi a wakufayo amamutenga namukulunga mumtolo waudzu. Maikidwe ake
m’mandamo amangoponya ngati galu koma osakwirira konse.

Manda ake Sali pamodzi ndi ena koma kwina kutali. Manda otere alipo lero lino
m’midzi yambiri, ndipo anthu amachita kupitapo. Pamaliro otere padalibe kumeta,
koma amangowamba ziwanda nawaulanso makasu awo, kupha mizimu.

Munthu wodwala nthomba

Nthendayi idadziwika kale lomwe pakati pa Achewa, ndipo idali yoopsa monga
nthenda yakhate ija. Matengedwe ndi machiritsidwe ake sankadziwikanso.
Nthendayi ikayamba m’banja, mayi kapena mmodzi mwa ana a m’banjamo
kapenanso banja lonselo limatulutsidwa m’mudzimo kukakhala kunja kwa mudzi
kutali ndithu monga mtunda umodzi kapena iwiri.

Nthendayi ikagwira mwana wa mbanja ndipo pomusamalira bambo ndi mayi ndi
ana ena amagona naye pamodzi. Nthawiyi kuti ntchentche zili ngw’a, ngw’a,
ngw’a, iwo amangozisiya osazisamala konse, ngakhale zili kukhala m’maso
kapena pathupi koma osazipitikitsa.

Anansi a banjalo samabwera kudzazonda matenda, koma amabwera ndi chakudya


nachiika panjira, naitana kuti mayiyo akatenge panjirapo. Iwo athawa mayiyo
asanafike, chifukwa chogonera pamodzi ndi wodwalayo. Ndipo amasowa
wotumikira mnzake namangosauka.

Njira yopita kumeneko imatsekedwa kuti anthu ena opita paulendo angadzere njira
yomweyo. Amasamalitsa koposa, ndipo kutero kudali kwabwino popeza ngakhale
lero zikuchitikabe monga m’maiko olongosoka. Amatero poopa kufalitsa
nthendayo. Patsiku lomwalira wodwala mmodzi wa m’banjamo amachoka
nakanena kumudzi kuti wakuti wamwalira. Ambiri samafika kumaliroko koma
achinansi owerengeka okha. Enawo amangolirira kumudzi osapita konse
kumaliloko.

Kumanda sikumapita anthu ena apadera koma achinansi okha. Amakumba


mandawo pomwe wakufayo adagona panthawi yodwalayo. Atamaliza kukumba
dzenjelo okumbawo amachoka, ndipo ena amatenga mtembowo naukankhira
m’manda.

49
Pamaliro otere satumiza anyamata okanena kumidzi ina, chifukwa a midzi
yozungulira samabwera kumaliroko. Mwambo wa Achewa pamanda
amakhazikapo nkhadze womwe ndi mutu wamitengo yopanda masamba womwe
umakhala ndi tinthambi tambirimbiri ndipo masamba ake ndi tinthambi tomweto.

Maliro a munthu womwalira ndi nthenda ya nthomba samaikapo nkhadze. Ndipo


anamfedwa samameta tsitsi msanga, koma amadikira mpaka nthendayo itatha
konsekonse.

Ikatha nthendayo, amayenderana ndi anzawo namwerana mowa chipanda


chimodzi.

Nzokondweretsa kwambiri m’zaka zamakono kuti nthendayi ikudziwika


matengedwe ake, ndi kachiritsidwe kake. Koma alipo anthu ena amene amaopa
katemera wa nthomba (smallpox).

Uzimba
Uzimba ndi chinthu chodziwika m’dziko muno ngakhalenso pakati pa mitundu ina
ya dziko lapansi. Nyama zomwe zimapezeka m’tchire ndi mvuwu, ng’oma,
ntchefu, insa, mphoyo, mkango, nguluwe, kaphulika, mbidzi, nswala, mphalapala,
m’mbulu, kambuku, fisi, chuzu, nkhwere, kalulu, chiuli, kanungu, nungu, nengo,
chiuzimbi ndi kamundi.

Ndipo angakhale machitidwe ake ndi zipangizo zake zimasiyana, koma cholinga
chake ndi chofuna nyama kutsuka m’kamwa m’mene nkhuli idaonongamo.

Pakati pa Achewa mwini uzimba amalengeza za uzimbawo m’midzi yozungulira.


Akafika pamudzi ndipo apeza amuna palibe, iye amatenga masamba ndi chimanga
chofiira chonenera uzimbawo nachipatsa akazi nati, “Nachi chimanga mudzapatse
amuna anu akafika.” Akaziwa amapempha wolengeza uzimbayo kuti awavinire.
Wauzimba amati, “Taombani m’manjamo,” Akaziwo amayamba kuyimba nyimbo
nati, “Wanya waliwamba, wanya waliwamba.” Iye amaseketsa akaziwo kwambiri
namati, “Pe! Pe! Pe!” Namaganyula miyendo namavina.

Amachita izi m’midzi yonse imene iye watumidwa kukanena zauzimba. Pochoka
apo amati, ‘Ndithu nyama nayi,’ nayesera kudya chimangacho ku magazi a nyama.

50
Kumemeza liwamba kumakumbutsa kuti m’mabanja onse kumene liwamba
lamemezedwa alongosole liwamba pakupatukana m’nyumba. Izi zikusonyeza kuti
usiku woti mawa kuli liwamba mwamuna ndi mkazi m’banja lililonse samagonera
pamodzi, kuopera kudula liwambalo kuti angaononge mpingu (tsoka).

Mwini uzimba amasamala kwambiri osagona pamphasa koma paudzu. M’mawa


amadzuka nadzutsa mkazi wake nati, “Nachitidzi, taukani uikepo kankhali kuti
ndidyeretu.” Mwana wa mkazi kapena mkazi wa mwini uzimba amadikira
m’nyumbamo n’kugona pamasamba mpaka kutha kwa liwamba kuti nyama
zizipezeka zitagona pambuto.

Popita kuuzimbako mwini uzimbayo amatenga udzu umene iye anangonapo usiku
uja. M’njiramo iye amafuula nati, “Liwambalo! Liwambalo! Wihi! Liwambalo!
Liwambalo! Wihi!”

Mwini liwambalo amalawirira pamalo pamene pakayambire liwambalo. Akafika


amakuwa kuti, ‘Uzimbawo, perekezeni mwana akana kholowa.’

Ali pamalopo amagona paudzu uja ndipo atafika onse amampeza ali mtulo.
Kugonako kusonyeza kuti nyama zigonenso. Atadzuka amalonjera onse nati,
“Mwabwera nonse?” Iwo amavomera nati, “Eya.” Ndipo amayamba kunena
malamulo auzimba nati, “Muuzimba mukaona insa (gwape), kalulu, nkhanga,
mbawala, ngoma, ndi ntchefu, izo zonse muphe; koma mukaona nyalugwe, njoka,
fisi, mkango ndi nkhandwe; muzithawe popeza si ndizo ndifuna kuti muphe ayi.”

Pamasankhidwa anthu atatu okhulupirika, wina kumsongwe wakudzanja lamanja


wina wakumanzere. Munthu wachitatu ntchito yake ndi yokadzulitsa miyendo ya
nyama zophedwa patsikulo. Akatero uzimbawo umayambika. Akuchita uzimbawo
kumamveka kuti, “Ndamulasa! Ndamulasa!” Ndipo ena amathandiza nati,
“Wolasayo! Wolasayo! Wolasayo!” Atapha, mwini liwambayo amapatsidwa
mwendo wathako panyama iliyonse imene yaphedwa pauzimbawo. Iye
amakhalanso ndi ena omuthandiza ndipo pamene iye kulibe amalandira miyendo
ya nyamazo, nati, “Akatigawira kumudzi tikakafika bwino.”

Pauzimbawo, mwini uzimba amapatsidwa mwendo wathako. Pakutha liwamba


onse amabwerera kwawo atapachikira akalulu mwina ntchenzi m’chiuno. Pa tsikuli
amayi saphika ndiwo zamasamba podikira nyama.

51
Akafika kumudzi amuna onse amakumana pabwalo. Ndiye miyendo yonse imene
idakadzulidwa amaiunjika pabwalopo n’kumagawana molingana. Pogawanapo
sipamakhala wodandaula konse.

Mwangozi munthu wina amalasidwa ndi mnzake, ndipo onse amasonkhana


pomwepo nafunsitsa zangoziyo. Munthuyo amamupereka kwa mwina uzimba kuti
akasamalidwe komweko. Koma ngati wamwalira, apo pamakhala mlandu waukulu
ndipo amalipa dipo lalikulu ndithu.

Ndiponso ngati munthuyo walumidwa ndi chilombo, amam’nyamula nakamuika


ku nyumba kwake kwa mwini uzimba. Patsiku la mlandu amati, “Iwe muja
udabwera kwathu numati mawa liwamba, kodi umatiitanira chilombo?” Mwiniyo
amayesa kudandaula, koma zosamveka kwa eni munthu wolumidwayo. Munthu
ngati waferatu umakhalanso mlandu wochititsa mantha.

Uzimba uli pawiri, wina amatentha tchire la munthu wina wake ndipo ngati
munthu wina alumidwa kapena kulasidwa, pamenepo mlandu wake amalipa
tchirelo. Uzimba wina ndiwo wongopita m’matchire ambiri a anthu ena amene iwo
adatentha kale. Mlandu wa anthu olumidwa m’matchire a uzimbawo amalipidwa
chuma chambiri, makamaka mbuzi zambiri popeza Achewa adali ndi mbuzi
zokhazokha ng’ombe zisanafike.

Atapatsana chikokerana fodya, mlanduwo umatha, ndipo amameta tsitsi


bwinobwino. Mwanjira yolipa tchire magawo ambiri a dziko adalandidwa kwa eni
napatsidwa kwa eni munthu wolasidwayo. Ichi ndi chifukwa chake mafumu athu
akukumbana nalimbirana dziko.

Malamulo a uzimba
• Tsiku lomemezedwa liwamba sikuloledwa mwamuna ndi mkazi wake
kugona malo amodzi kuti kungakaoneke ngozi ku uzimbako.
• Pomemeza liwamba amatenga chimanga chofiira kufanizira magazi a
nyama.
• Mwini liwamba amagona paudzu kapena pamasamba. Amachita izi
chifukwa masiku onse amasendera nyama paudzu kapenanso pamasamba.
• Mwini uzimba amagona pamalo ponyamukira liwamba kuti nyamanso
zigone.
• Amene ali ndi mkazi wapakati saloledwa kupita nawo kuuzimba kuti
kungakaoneke mpingu.

52
• Anthu akalasana kuuzimba, mwini wa uzimba amapereka nkhuku popeza
ndi iye adamema uzimbawo.
• Akazi saloledwa kupita nawo kuuzimba.
• Nyama zophedwa kuuzimba mwini uzimba amapatsidwa mwendo wathako
wa nyama iliyonse yophedwa.
• Mkazi mwina mwana wamkazi wa mwini uzimba saloledwa kutuluka
m’nyumba mpaka auzimba atabwera; amatero kuti nyama zingathawe
kuuzimbako.
• Mwini uzimba atalandira miyendo, imagawidwa kwa mfumu ya mudzi
popeza nayenso imalongosola nawo liwamba.

Uzimba

Kapolo

Dzinali limatanthauza munthu wogonjetsedwa ndipo wopanda mphamvu. Dzinali


kapena mchitidwewu ndi wakalekale, ngakhale mu Baibulo (Buku lo Patulika)
muli nkhani zokhudzana ndi dzinali. Yosefe, abale ake adamugulitsa muukapolo.
A Israeli adatengedwa muukapolo ku Babuloni, ndi zina zopotsera.

Mawu oti kapolo amatanthauza munthu wopanda ufulu uliwonse wonena


zakumtima, wogwidwa pankhondo, woperekedwa monga dipo pamlandu kapena
wotoledwa panjira kapenanso woperekedwa chikole. Ntchito ya kapolo idali
yosalipidwa ndipo samaloledwa kudandaula, samayenera kuwiringula ngakhale
kukana. Amatha masiku angapo osadya koma ntchito akugwirabe. Akalakwira
pang’ono amalangidwa kolapitsa, komanso samayenera kuthawa akamalangidwa.

Kapolo amagwira ntchito yakalavulagaga tsiku lonse lathunthu, osalandila malipiro


kapena kanthu kalikonse. Akangolakwitsa amamenyedwa kwambiri mwankhanza

53
yoopsa. Amapatsidwa chakudya chosakwanira ndipo nthawi zina amadwaladwala.
Kapolo akakhalitsa amatchedwa ‘mwana’ ndipo dzina la ukapolo silimamvekanso.

Ukapolo udali wamitundumitundu, wina udali wotengedwa pankhondo


atagonjetsedwa. Nkhondo idali kumenyedwa m’njira zosiyanasiyana. Nkhondo ina
imabuka polimbirana dziko. Opambana aja amatenga dzikolo n’kukhala lawo ndi
kumalamulira, ngakhalenso eni dziko aja.

Ukapolo wina udali wogulitsidwa. Pali mitundu ine imene imapeza chuma chawo
pogula ndi kugulitsa akapolo. Ndiye wogulitsidwa amakhala mwana wosamvera
(puludzu). Makolo ake akatopa naye amangoti, “Tengani uyu. Bola mutipatse
thumba lamchere kapena malipande awiri ansalu ya biriwita (nsalu yakuda).”

Ukapolo wina udali woti ukakumana naye munthu amene utam’dziwiratu kuti
sangalimbelimbe, otereyo umam’bweza kumene walunjika (kumsemphetsa
chikuwa). Zitatero umamusandutsa kapolo namakugwirira ntchito. Ngati ndi mkazi
kutsogolo amasanduka mkazi wako n’kumanga naye banja, zikatero ukapolo
umathera pomwepo.

Kapolo wotero poyenda amamuthira ufa m’khutu kapena m’kamwa kuti asathe
kumva, kufuula ngakhalenso kulira. Ukapolo wina umabwera chifukwa chakuti
mwina mlandu ukakula ndipo dipo lake lasowa, ndiye amangopereka munthu
kusandutsa dipo la mlanduwo. Zikatero samatchedwa kapolo, amakhala ngati
chiweto ndipo amakhala movutika.

Kapolo wogwidwa panjira

Nthawi zina munthu amadziyendera, ndiye akakumana ndi anthu omenya nkhondo
amamgwira n’kutsogoza kum’pititsa kowirira namukhazikitsa pansi. Kumeneko
amamuthira ufa wa lipoko m’kamwa n’cholinga chakuti asathe kuyankhula
kapenanso kukuwira ena. Kutada amayenda naye mozungulira. Mwina
kukam’fikitsa kutali kwambiri, n’kubwerera nayenso kupita naye uku ndi uko
ndipo kukamacha amapita naye kunyumba kwawo atatopa kwambiri.

Amamubindikiza m’nyumba masiku angapo. Komatu mwina kwawo kuli pafupi


zedi, mwina mitunda inayi yokha. Ngati munthuyu ndi wamwamuna amagwira
ntchito zachimuna monga zolima kwa dzuwa kalowe, kusamala ziweto, ndi zina
zotere. Koma ngati ndi wamkazi iyayi amafa ndi tsokwe ndi kutola nkhuni.

54
Ukapolo wamkazi sumachedwa kutha maka ngati ndi wokongola, chifukwa mfulu
zimamukwatira ndiye ukapolowo umathera pomwepo. Mwamwayi mwina
amakwatiwa ndi mfumu kumene.

Pali nthano yochitsa chidwi imene ikuti azungu a mishoni oyamba monga Rev AC
Murray ndi Rev Robert Volk mu 1888 adapempha mfumu ya Agoni, mfumu
Chiwere, kuti awapasire ana oti awaphunzintse, koma mfumuyo idapereka ana a
akapolo kwa a mishoni. A kapolo aja adaphunzitsidwadi, ena nasanduka
aphunzitsi, ena akapitawo mpaka kusanduka abusa a Mawu a Mulungu.

Uku kudali kukankhira pumbwa ku chipwete, paja akulu adati, ‘Patsogolo


m’pambuyo pomwe.’ Mfumu Chiwere ankaganiza kuti azungu ndi mfiti amadya
anthu, ndiye chosatira chake am’banja la chifumulo adatsalira pamaphunziro.

Ukapolo wogwidwa pankhondo

Nkhondo ikabuka pakati pa mitundu ya anthu, ogonja amatengedwa ukapolo.


Amatengedwa ambiri ndipo amachita kugawana ngati mbewa. Akapolo achikazi
amatchedwa kuti adzakazi. Achimuna amawatcha kuti akapolo. Masungidwe a
akapolo adali okakamiza ndiye sitingazengereze kunena kuti ukapolo umenewu
udali woopsa ndi womvetsa chisoni. Nkhondo ikatha pamakhala kubwezerana
akapolo.

Nkhondo zilipo zosiyanasiyana monga yogalukirana/youkirana eni okha,


yolimbirana malire a dziko ndi yolimbirana dziko. Nkhondo yogalukirana
imakhala yolimbirana utsogoleri ndi kayendetsedwe ka ulamuliro kapena dziko.
Nkhondo zotere zawanda makamaka muno mu Africa, Kubaluya, Kubaluya
(Middle East) ndi kwa Amwenye (Far East).

Nkhondo zoterezi zikabuka pamapezeka mitundu ina kulowerera ndipo zikatero


kumachita ngati kukwerezera moto. Zotsatira zake zimakhala kubwezera chitukuko
m’mbuyo chifukwa anthu sakhala ndi nthawi yopita kuminda kukalima, popeza
amakhala ndi mantha ndi kusowa mtendere. Zotsatira zina ndi kusakazika kwa
chuma chopezekapezeka.

Kopolo wogulidwa

Masungidwe a kapolo sadali abwino popeza akapolowa amamenyedwa pa


chifukwa chochepa. Amagwira ntchito koposa mphamvu zawo. Amalandira
chakudya chosakwanira konse. Pamatenda samasamalidwa bwino. Ndipo

55
mnyamatayo amakhala wosasangalala nthawi zonse pokumbukira makolo ake
ndiponso ntchito ndi masungidwe ake kwa mbuye wake.

Maliro akapolo sadali monga momwe adali mwana wa mfulu. Anthu amapita
kumanda nakumba pang’ono, natenga malirowo ali okulungidwa m’tchika
labango. Kukakhala kuti mbuye wake wa kapoloyo adali wabwino, amachita zonse
monga momwe anagachitire ndi mwana wake.

Lero dziko lonse la Africa ndi mayiko ena omwe, ukapolo udaletsedwa ndi Boma.
Pamene Dr. David Livingstone adayendera dziko lathu lino adamva chisoni
kwambiri ndi anthu amene amvutiak kamba kamalondawa. Ndipo chifukwa cha
ntchito yake yotamandika malondawa adaletsedwa ndi maboma ambiri.

Ukapolo

Padali ana omwe adali apuluzu ndi osamvera ndiponso omva zawokha. Oterewa
kukadza amalonda, maka aluya amawagulitsa ndi mchere mwina litaka la nsalu.
Ogulitsidwa uja samadziwa kuti wagulitsidwa. Amalonda aja akamanyamuka,
wogulitsidwa uja amauzidwa kuti awaperekeze alendowo kuti awatule kunjira.
Ndiye akamafuna kubwerera amamuumiriza kupitiriza ulendo. Ngati avutitsa
amamumenya kolapitsa ndipo ulendo umakhala womwewo wopitiratu.

Za ufiti, mankhwala ndi matsenga


Mfiti
Mfiti ndi dzina la munthu wakudya ndi kupha munthu. Pali chikhulupiriro choti
pali anthu odya anzawo. Gulu limeneli pamakhala amuna ndi akazi. Akuti maliro
atayikidwa, iwo amasonkhana kumanda mozungulira muunda (mtumbira) pamene
wakufayo waikidwa. Atazungulira muundawo, amatenga muzu wamankhwala

56
n’kumenya pamwamba pa muundawo n’kuitana dzina la malemuyo. Nthawi
yomweyo malemuyo amatuluka yekha m’mandamo. Zikatero amamuphanso
nasenda thupi lonse n’kuyamba kugawana ziwalo molingana. Zikatero
amamwazikana. Pophika amaika malo obisika omwe ena amati pansi. Itapsa
amadya mobisa kwambiri. Mwamuna ndi mkazi onse akakhala mfiti ati kudya
kwake sikuvuta konse.

Masiku ano maliro akafukulidwa wakufayo amapezeka ndiye pamagwa funso


lakuti, “Kodi mfiti zimadya chiyani?” Kunena kwina amati wakufayo saikidwa
m’manda nthawi ija yonyamula chithatha, wakufayo amatsala m’nyumba
momwemo ndipo chija chimaikidwa m’manda chimakhala chifanizo chabe.

Ufiti ulipo ungapo, wodya anthu ndi wampheradumbo. Mfiti zina zimapha munthu
chifukwa cha zimene alinazo monga ziweto, galimoto ndi zina. Izi mfiti sizidya
nyama ya munthu. Mfiti zotere tikhoza kuzitcha mfiti za m’pheradumbo
(m’pheranjiru). Zimangopha ndi mankhwala aululu, mwina ndi mizu kapenanso
zolengedwa zina monga ulembe (sumo). Komanso pali mankhwala ena ongolemba
malire kuti utalumpha mzerewo ungafe ndithu. Mankhwala ena otemberera
potemba amati, “Dzuwa uliona potuluka pokha, polowa sulipenya.”

Pali zitsamba zina zaululu zimene munthu atadya amafa. Pakauka mkangano
pakati pa munthu ndi munthu mnzake, mmodzi mwaiwo amafunafuna mankhwala
ophera mnzakeyo pomudyetsa. Maphedwe ake amathirira kuchakudya monga
nsima, mowa kapena kuphala lachimera, mwinanso ku tiyi.

Atamwa kapena kudya, m’mimba mumawawa kwambiri. Zitatero amasanza


zobiriwira ndiponso kutsegula kapena patapita kanthawi munthuyo amafa. Anthu
amadziwa ndithu kuti mankhwalawa achokera kwa mdani uja malinga ndi
kusagwirizana kuja, ndiye wolira amalira mopenyetsetsa mdaniyo. Zikatero eni
maliro amapita kwa sing’anga kukaombeza kuti akawauze amene wachita
zimenezi, ndipo sing’anga uja amatchuladi yemweyo. Sing’anga kenaka amafunsa
olira uja kuti, “Nanga amaneyu timutani?” Yankho lake limakhala loti iyeyu
afenso. Maphedwe ake mwina amamuikira mankhwala panjira kuti akalumpha afe
ndithu, mwina kuti achite misala.

Mfiti ikadziwika anthu amaiopa ndi kusayifunira zabwino, angakhale achibale ake
omwe.

Kusamalira mtembo

57
Akuthatha ndi imfa, ena amagwira miyendo yonse iwiri n’kuiphatikiza, ena
amagwira manja n’kuwakanikiza mbali imodzi yamutu mokhumatitsa, ena
amatseka maso kuti asang’omboke, ndipo thupi lawakufayo litazizira amatenga
mkuzi n’kunjata manja ndi miyendo; amanjatanso kuchigama mpaka pakati pa
mutu.

Amakauza mfumu ndipo mfumu ija ikabwera imalamula kuti atsuke, ndipo
amamusambitsa thupi lonse n’kumuveka ziwalo zonse osaiwalanso kumudzoza
mafuta. Zonse zitatha mfumu imauzidwa kuti, “Tatsuka.” Ngati ndi mayi,
womutsuka amakhala ntchembere zokhazokha, koma ngati ndi mwamuna otsuka
amakhala ndoda zokhazokha.

Pambuyo pa zonse mfumu imalamulira ndi mawu niti, ‘Tiyeni tikhuze ngoziyi.’
Ndiye woyambirira kukhuza amakhala mfumu, kenaka onse amatsatira pambuyo
pa mfumuyo n’kubuma. Poika chitanda amasanja ndi kuikapo udzu, ndipo
pamwamba pake amaikapo mphasa. Mferekazi (dzinali ndi lamkazi amene
mwamuna wake amwalira) amakhala ndi kansalu m’manja n’kumaingitsa
ntchetche mpaka nthawi yochotsa maliro. Popita kumanda, mferekazi
amamufunditsa nsalu thupi lonse kuyambira kumutu mpaka m’munsi. Pamakhala
amayi omugwirizira, makamaka alamu ake. Atafika padzenje mferekaziyo amatapa
dothi lodzala chikhato n’kuthira m’mandamo. Kumeneko amati n’kulawirana
ndiponso kuuza mzimu wa wakufayo kuti usakamukumbukirenso.

Asing’anga

Pali asing’anga ochiza anthu odwala. Tsono ena zizimba zake amazipeza potenga
ziwalo za munthu. Asing’anga ena amatha kuthandiza munthu wosabereka,
mwamuna kapena mkazi omwe amatchedwa chumba. Sing’anga akhoza kukhala
mwamuna kapena mkazi. Ziwiya zosungiramo mankhwala ndi mphondo za
ng’ombe, nkhosa, nyanga za nyama zakuthengo monga insa (gwape), chipembere,
ngoma ndi zina.

Mankhwala ena amatemera n’kupaka m’mabalamo, ena kumwetsa, ena kuveka


m’chiuno kapena m’khosi.

Palinso asing’anga ena ongoombeza, n’kuvumbulutsa zinsinsi. Munthu akadwala


pamudzi asing’anga oombeza amaitanidwa. Atafika amafunsa chiyambi cha
matendawo. Atamva amatenga nsupa n’kuyang’anamo, ndipo amaona kuti
wodwalayo adamulodza ndi uje, “Bwerani mudzionere nokha.” Zitatero amafunsa

58
achinansi a wodwalayo nati, “Kodi amaneyu timuchitenji?” Yankho limati,
“Iphani, mwina mulumazeni kapena mudooleni maso.” Mfumu ikafunsidwa
funsolo kuyankha kwake kumakhala kwakuti, “Ingophani, pano kuti anthu akhale,
chifukwa mudzi kapena dziko ndi anthu, ndipo thengo m’mabala.”

Mtsiriko

Kutsirika kwake kudali kwakuti ukaba ugona pomwe wabapo mpaka kukuchera
pomwepo. Ngati waba nkhuku, nkhukuyo imalira m’phikamo mwina m’mimba.

Mtsiriko wina udali woumitsa mimba, wina pakamwa kupotoka. Munthu wofuna
kuba ziweto amangopeza khola lili pakati pa nyanja. Nyumba ikakhala yotsirika
mwina mfiti siingathe kuiona. Akakhala makhola aziweto mwina amazingidwa ndi
zilombo monga mikango. Munthu atayandikira zilombozo zimamupitikitsa.

Mankhwala
Pofunsira mbeta pamafunika mankhwala. Pofuna ntchito pamafunika mankhwala
opezera ntchito. Pofuna kukwezedwa patchito pamafunikanso mankhwala. Amayi
apamitala amafuna mankhwala otchedwa ‘konda ine’. Mankhwalawa amathiridwa
ku ndiwo mwina mumkhate wosambiramo. Mwamuna wosakhazikika pakhomo
kapena woyendayenda amamudyetsa mchira wabuluzi chifukwa buluzi
sachokachoka, mwake ndi m’khonde.

Matsenga (masenga)

Matsenga n’kuchita zinthu zododometsa. Anthu amatsenga amatha kusanduliza


munthu wamkazi kuti akhale wamwamuna. Chingwe kusanduka njoka, mphinjiri
kusanduka chilombo monga mkango, fisi kapena kambuku. Koma pali ena
otchedwa mfiti kapena athakati, amenewa amadzipangira ndege pogwiritsa ntchito
chipapa cha lichero n’kumauluka mlengalenga mpaka kukafika ku Joni
n’kubwerako kusanache. Ena amalenga khoswe wotenga ndalama zamwini
m’thumba kapena kukatenga chimanga cham’munda mwa mwini n’kuchipititsa
m’munda mwawo. Aliponso ena amene usiku amatalika mamita angapo
utakumana nawo ndipo amauka natsika mpaka pansi. Uwu ndi ufiti kapena
matsenga.

Zikhulupiriro zina za ufiti ndi matsenga

• Munthu wolemera amakhala ndi mantha podziwa kuti atha kulodzedwa ndi
mfiti mwinaso kufa msanga.

59
• Mkazi wankhope yokongola sayenera kukana amuna podziwa kuti ngati
atero atembereredwa ndi amasenga.
• Amuna a nyawu, amauza ana kuti, “Ngati muulula nyawu potsiriza pake
mudzachita misala.”
• Amakhulupirira kuti munthu atangolemba panjira nati, “Ngati uje aponde
pano adzachita misala, kupunduka kapena kumwalira wosadwala konse.”
Ambiri amayenda moopa posadziwa chimene mdani waika panjira.
• Pamakhalanso wina amene amadziwa mankhwala ochiza matsengawo,
ndipo amati, “Ngati munthu amene adalodza iwe sadya nsima kapena sagona
monga anthu onse, matenda amenewa satha konse. Koma ngati ndi munthu,
matendawa atha.”
• Anyawu amaopsa anthu nati, “Ngati ubisala pathengo kuti uone nyawu
zathu, maso ako achita khungu.”
Lero tili okondwa kuti anthu ena ayamba kuzindikira kuti ufiti ndi matsenga ndi
zachabe.

Masasa

Pamudzi chomwe chimachitisa kusamuka ndi mavuto monga ufiti, ngakhalenso


imfa zochitika mowirikiza, udani ndi kusowa malo okwanira olimapo kapena
kudyetsapo ziweto. Nyumba zisanamangidwe mtsogoleri wa anthu osamukawo
amafuna mtsiriko wodzatsirikira masasawo. Mtsirikowo amazungulira malo
onsewo. Ntchito yamtsiriko n’kuteteza mudzi kumfiti ndiponso kuzilombo monga
mikango, fisi, nyalungwe ndi kangombwa. Tsiku lokalowa, anthu a mudzi
amaunjika mphondo zodzala ndi mankhwala, ndiponso mbiya zazing’onozing’ono
komanso mafuwa pamphambano.

Patsiku lokalowa samapala moto kubwinjako. Mtsogoleri wa anthu osamukawo


amapeka motowo pogwiritsa mtengo wofewa ndi mpheko. Koma ntchito yopeka
moto ndi yovuta moti pamafunika anthu angapo chifukwa zimawawitsa m’manja.

Moto ukayaka amausonkha ndi nkhuni zouma kotero mudzi wonse umapala moto
pamenepo. Malamulo amati munthu asaunike kapena kulowa ndi moto
m’mudzimo, popeza kutero kudali kuunika mudzi. Zikatero umakhala mlandu.

Akakhala pa masasapo kwa kanthawi, pamafululidwa mowa woti amidzi ina


yozungulira adzaone masasawo.

60
Nthawi zina pamasasapo mavuto osiyanasiyana monga mikangano ndi ndewu.
Akuluakulu amayesetsa kuweruza milanduyi mwachilungamo. Mwachitsanzo
nkhuku ya munthu wina ikasowa, munthuyo mwina angokayikira mnzake amapita
kukamwa mowa dala. Akabwerako amakuwa nati, “Mverani! Nkhuku yanga
mwadya, ndikupitirani kwa sing’anga kotero zimene muone pano ndi zimenezo.”
Kutacha nduna za mfumu zimalawirira kukhomo kwa wotukwana uja ndi
kumufunsa kuti, “Kodi kutukwana kuja mudayambana ndi yani?” Woyankha
amati, “Inetu ndimalira nkhuku yanga imene munthu adandibera dzulo masana.”
Funso limati, “Kodi munthu amene wakuberaniyo mwamugwira?” Yankho: “Ayi,
sindinamugwire.” Ndiye chiweruzo chimati, “Popeza wakubayo simunamgwire
ndiye mwatukwana mudzi, kotero mulipira mkota wa mbuzi.”

Munthu wogwidwa ndi nkhani zachiwerewere dipo lake lidali kuphedwa onse
awiri. Izi amachitira popewa kuti zilombo zisamalowe pa msasapo
n’kumadzagwira ziweto.

Munthu wofa ndi mankhwala


Ena amati alipo mankhwala amene munthu angathe kuikira mnzake panjira,
nalemba nati, “Ngati uje sindiye wobadwa mwa mkazi alumphe lemboli, koma
ngati iye wabadwanso monga ine, tionana.” Ndipo ati munthuyo akadumpha
amamwalira kapena kupunduka kapenanso kufa mozunzika.

Mankhwala ena adali temberero. Anthu awiri akamenyana, koma winayo poona
kuti iye wamenyedwa kwambiri ndiye amayamba kunena zambiri mosalingalira,
nati, “Iwe, ine sundidziwa kuti ndine swiswiri sapita m’chimera, ndipo lamawa
suliona potuluka.” Winanso amati, “Inenso ndine mwana wa Pite, bololo sakonda
madzi, ndipo lamawa uliona potuluka pokha koma kumene lizilowera suliona.”
Anthu oonera ndewuyo amamvetsetsa zonsezi nazisunga. Mwatsoka winayo
amadwala ndipo abale ake amapita kwa mnzake wotemberera uja nati, “Monga
mwa mawu anu aja mnzanuyo akudwala.” Koma iye amati, “Koma ine dzulo lija
ndidangonena mosaganiza bwino.” Koma enawo amati, “Ayi mudanenetsa bambo,
kapena mayi. Nanga wathuyu adwala bwanji?”

Patsiku lomwalira munthuyo, achibale ake amati, “Mnzanu uja wamwalira monga
mwa mawu anu aja.” Munthuyo nkhawa ndi mantha, amayesa kukana, koma
sizimveka konse. Iye amalipitsidwa chogonekera maliro, ndiponso dipo lenileni.
Kuyambira tsiku limeneli, munthuyo amadziwika kuti ndi mfiti ndipo anthu
amachita naye mantha nthawi zonse.

61
Maliro a munthu womwa mwavi
Mwavi ndi dzina la mtengo waululu wakupha munthu. Koma anthu ambiri
ankakhulupirira kuti ndi makhwala olondola ndipo amangopha mfiti zokha, kapena
wakhalidwe loipa monga chiwerewere.

Mfumu m’mudzi ikaona kuti anthu akutha kufa amaganiza kuti pamudzipo pali
mfiti imene ikutha anthu. Pakati pa Achewa ndi mitundu ina amalingalira kuti,
munthu aliyense yemwe wamwalira idamuloza mfiti basi. Salingaliranso kuti
matenda ena munthu amadzitengera yekha nafa nawo. Atasinkhasinkha mfumuyo
imati, “Kudakakhala bwino ngati ndikatenge mwavi kuti onse adzamwe.”

Akafika kwa mwini wa mwaviyo, iye amati, “Tikuoneni wawa.” Mfumuyo


nivomera ninena kuti, “Nanga mwadzangoyenda?” Mfumu imayamba kufotokoza
tsatanetsatane wa mmene zidachitikira kwawoko. Wamwaviyo amatenga
kamtondo kakang’ono komwe iye amasinjiramo mwavi ndi kamusi kake.
Posinjapo amanenerera zambiri.

Mfumuyo imaneneratu kuti, “Pokhala pathu ndi iwe, tikakhale mopenyana ndipo
ndikakaimirira chala changa chakumwendo ameneyo ukam’mwetse mwavi
wopanda mphamvu koma ndikakagwetsa chalacho kwa woteroyo ukam’mwetse
wamphamvu.”

Atafika kumudziko amaitana nduna yake ndi madoda a m’mudzimo nawauza kuti,
“Ndakatenga thumba (mwavi) kuti tonse tiyere, popeza anthu afa ambiri. Onsewo
amavomera mwachimwemwe podziwa kuti mwavi umalondola mfiti, koma wina
amene sali mfiti sumulondola ayi.

Mwaviwo amakamwera kuthengo, ndipo mfumu ndi mwini mwaviwo amakhaladi


mopenyana ndi kuyamba kumwetsa anthu. Mwiniyo amati, “Ngati iwe uli mfiti
wodya anthu, ndiponso wakuba, ndi wachigololo, suliona polowa lero dzuwa.’
Wakumwayo amati, “Ngati ine ndimadya nyama ya anthu, udziwe mwavi, koma
ngati ine ndine mwana ndigona madzulodzulo, komanso ngati ine ndimanyenga
mkazi wamwini iwe ndiwe ungadziwe.” Koma tisaiwale kuti wamwaviyo
amayang’aninitsitsa chala cha mfumu. Chikaimirira chalacho woteroyo
amamwetsedwa mwavi wabwino, koma kwa iye yemwe chamugwera chalacho ndi
watsoka ndithu. Ena amasanza koma movutika. Koma kwa amene wapatsidwa
mwavi wamphamvu amasauka kuti asanze koma osatheka. Wamwaviyo amati,

62
“Ifani chafufumimba mungandiphere thumba.” Ndipo munthuyo amamwalira.
Onsewo amasekerera kuti munthuyo adalidi mfiti.

Maliro a munthu wotere anansi ake samawasamalira, amangowataya m’dzenje


ngati phulusa, ndipo amachita izi podziwa kuti sangasauke ndi maliro a mfiti
yodya anthu. Zakumeta ndi zina zonse zochitika pa maliro a munthuyo
samazisamala.

Anthu omwetsa mwavi mwina amasintha mayina awo monga Chinguwapangu,


Kamgundumula ndi ena.

Maliro a munthu wachuma

Anthu osauka ndi olemera amapezeka pakati pa anthu am’maiko onse. Nthawi
zonse wosauka amagwira ntchito kwa munthu wolemera. Wachuma sasowa
abwenzi ocheza nawo popeza munthu amadziwa kuti ndikakafika pakhomopo
ndikadya zabwino ndiponso ndikagona pabwino.

Komanso pali mawu akuti, ‘Wosauka ndiye amakhala nthawi wosafa msanga
koma wolemera amafa msanga.’

Pakati pa Achewa wina akapeza mbewu kubzala bwino kumunda, ndipo walonga
nkhokwe zitatu, kapena zinayi amayesa tsoka nati, “Ine ndalaulidwa,” Mwinanso
amakhala ndi ziweto zambiri, koma munthuyu sagona bwino masiku onse popeza
amakhala ndi nkhawa yakuti iye munthu wina adzamulodza ndi kumwalira
asanadyerere chuma chake.

Ataganizaganiza choti achite ndipo akachipeza, ndiye kuti amafuna mankhwala


kuti iye asalodzedwe ndi mfiti.

M’mawa kutacha amapita kwa munthu amene amadziwa mankhwala osunga thupi.
Ndipo mwiniyo amati, “Inde mankhwala ndimadziwa koma mtengo wake ndi
mbuzi khumi.” Mwamsanga wolemera amavomera kuti apeze chipulumutso.
Ndipo iye amakhulupiriradi mankhwalawo.

Atagona tsiku lina, amalota atulo munthu ali chilili pakhomo kufulama namalodza.
Kutacha m’mawa amafotokozera mkazi wake ndipo mkaziyo amati, “Pepani
amuna anga, ine mkazi wanu wapamtima ndikuuzani kuti pitaninso kwa
sing’angayo kuti akakupatseni mtsiriko wa nyumbayi kuti mfiti zizidzaona ngati
pali nyanja.” Nthawi zonse mawu a akazi samakanidwa, ndipo mofulumira

63
amapita kwa sing’angayo natenga mankhwala otsirika nyumba kuti mfiti
zisafikenso.

Nthawi zambiri wolemera akamwalira banja lonselo limakhala ndi chisoni


chachikulu. Patsikulo pamafika anthu ambiri amaononga chumacho momwaza,
kuswa, kudya ndiponso kuchiika pamodzi ndi mwiniyo. Patsiku lotuluka pamtanda
achibale a munthu wolemerayo amatenga chuma chotsala monga ziweto, zakudya
ndi zina. Mkazi ndi ana amangouzidwa kupita kwawo osamupatsako chumacho.
Ichi n’chomvetsa chisoni kwambiri ndithu.

Munthu wophedwa mwangozi


Ngozi ndi chinthu chimene chimachitika mwadzidzidzi. Koma maonekedwe ndi
machitidwe a ngozi amasiyanasiyana.

Ana posewera ndipo mosayembekezeka mmodzi amaponya mwala nutema


mmodzi mwa iwo. Pomwepo ana ena amachita mantha, ndipo amathawa nasiya
mnzawo wina atavulala. Koma mwana amene walasa mnzakeyo amakhala
pomwepo namadikira wolasidwayo. Maganizo ake panthawiyi amati,
“Ndikadangokhala bwenzi zonsezi sizikadachitika.”Amachitanso mantha nati
sindiziwa chomwe achite makolo anga, ndiponso makolo a wolasidwayo ngati iye
amwalira. Akulu amafika kudzaona ngoziyo ndipo amanyamula wovulalayo napita
naye kumudzi. Akulu amachitanso ngozi.

Machitidwe angozi yotere akakhala anthu abwino amangoti ndi ngozi. Koma ngati
makolo amwanayo ndi anthu ovuta amanena kuti mwanayo akasungidwe kwa
makolo a mwana womulasayo mpaka atachira. Koma ngati wovulalayo amwalira,
apo pamakhala milandu yopanda dipo lina koma kulipanso munthu wamoyo.

Dipo lotere ndi lija anthu amati, “Dziko kulipa dziko ndipo khungu kulipa
khungu.” Ndipo mwana wolasa mnzakeyo ndiye amaperekedwa dipo, ndipo a
banja linalo amamulandira ngati mwana wawo weniweni.

Ngozi ina ndi yomwe imachitika anthu awiri akamenyana ndipo winayo nagwa
naferatu. Womenyayo amakhala pa mlandu waukulu kwambiri. Atalipilitsidwa
amaika malirowo, nameta nasekererananso.

Maliro a munthu wofa mwadzidzidzi

64
Imfa yadzidzidzi ndiyo imathetsa anthu nzeru, ndipo anthu onse sazindikira
chimene chaagwera kuti n’chiyani. Izi zikutanthauza kuti munthuyo amamwalira
wosadwala konse.

Machitidwe a imfayi mwina amalingana ndi imfa yangozi. Akazi popita kukatola
nkhuni amapita ambiri. Ndipo mmodzi mwa iwo poti akwere mumtengo athyole
chikunicho, mosayembekezera amagwa naferatu. Imfayi imadodometsa anthu
polingalira kuti mnzawoyo wangofa wosadwala.

Koma mwina mkazi amadzuka m’mawa napita kunkhuni, kumadzi ndi kwina
nabwerako ndipo kenaka nasinja mphale. Atamaliza izi zonse madzulo amaphika
nsima kuti banja lake lidye. Ndipo mayiyo amangozindikira akuti, “Ndagona
pano,” nsima wayisiya ili pamoto. Bamboyo poyesa kumfunsa kuti, “Kodi make
Ntchowa mwachita bwanji?” mwina bamboyo sayankhidwa konse.

Ndipo bamboyo amaitana anthu. Atafika anthuwo amaona chochitikacho.


Anthuwo amafunsa kuti, “Kodi iyeyu amadwala?” Bamboyo amati, “Ayi.”
“Nanga … kapena munamenyana?” Iye amati, “Ayi ndithu.” “Nanga iye
sanakuuzeni tsiku limodzi lonse kuti ine ndimadwala nthenda yakutiyakuti?” Iye
amati, “Ayi, ngakhale n’pang’ono ponse.”

Atafunsidwa mafunsowa anthuwo amati, “Fotokozani bwino mafedwe ake a


munthuyu.” Bamboyo amati, “Mmawa iyeyu wadzuka bwinobwino ndipo masana
anapita kunkhuni ndi anzake koma pobwera uko anapitanso kumadzi. Atatha
zonsezi anayamba kusinja mphale, ndipo nthawi yamadzuloyi anayamba kuphika
chakudyachi. Pambuyo pake tangoona mnzathu akuti ‘ndagona pano’. Ndiyo imfa
ya mnzangayu.”

Malirowa saliridwa msanga popeza amaganiza kuti kapena munthuyo


wangokomoka chabe ndipo kapena aukanso. Atadikiradikira naona kuti wakufayo
sakudzuka, apo amauza amayi atsuke malirowo. Atatsuka amauza amuna kuti
mfumu ija tamaliza kutsuka (munthu akamwalira amatchedwa mfumu). Kenaka
anthuwo amabuma maliro.

Amuna ena amapita kuthengo nakaveka mnzawo masamba m’khosi, m’chiuno ndi
pachifuwa, namveka nsalu kumaso, naboola pawiri kuti azionerapo. Ichi ndi
chinyawu chimene chimatchedwa Kang’wing’wi. Ndipo Kang’wing’wi amafika
kumudzi namavina akazi akuimbira nyimbo. Kang’wing’wi amakhala ndi zibonga
ndipo amatha kupha nkhuku iliyonse ndiponso kumenya munthu ndi zibonga.
Dzina la zibongazo amati, ‘zigelo’.

65
Kang’wing’wi

Panthawiyi amuna amakhala ali kumanda. Ataika malirowo amachita zonse monga
mwa miyambo ya Achewa.

Maliro a munthu wakhunyu

Nthenda yakhunyu ndi nthenda yoopsa. Dzina la nthendayi amati, linjirinjiri


kapena nthenda yakumwezi.

Nthendayi imatchedwa yakumwezi popeza imafikira wodwalayo panthawi yokhala


mwezi ndi nthawi yakufa mwezi. Pathawiyi munthuyo amayankhula mosaganiza
ndipo amachita ngati wamisala. Amakhalanso wosatsutsika nachita makani. Anthu
ambiri amachita naye mantha, namaleza pamene ayamba kulongolola ndi
kumachita zina ndi zina.

Tsiku loyamba nthendayi siimadziwika, ndipo mwina imam’fikira ali pafupi ndi
moto mwinanso pamadzi. Ndipo makolo ake a munthuyo samulola kuyenda yekha
panthawi ya kukhala ndi kufa kwa mwezi.

Mankhwala Achichewa amakhalapo, ndipo makolo amafunsafunsa asing’anga


amene amadziwa mankhwalawo. Nthendayi mwina imatha nimachita
kamodzimodzi pamwezi kaya patapita miyezi wiri. Sing’angayo amapatsidwa
chipondam’thengo, chofunira mankhwalawo.

66
Imfa ya munthu wodwala nthendayi amachita m’njira zosiyanasiyana. Matendawo
akamubwerera pafupi ndi moto iye amagwera pamotopo. Ndipo ngati palibe anthu
pafupi amangopserera. Pofika anthu amapeza kuti munthuyo watha kale kupsa.
Amaitanizana kudzaona zachisonizo natenga zopsererazo naziunjika pamphasa
nayamba kulira maliro.

Mafedwe a anthu ena odwala nthendayi amachitika pamene apita kukasamba. Ali
pamadzipo nthendayi imamufikira ndipo amakomoka ali m’madzimo. Anzakewo
mwina sazindikira msanga kuti mnzawoyo wakomoka. Atakhalakhala amaona kuti
mnzawoyo satuluka m’madzimo. Ndipo anawo amathamanga napita kumudzi
kukauza makolo ake. Anthu onse amafika nayamba kumira kufuna wakufayo.
Akapezeka amamunyamulira kumtunda namuika pamphasa. Kuchokera uko
amapita naye kumudzi.

Maikidwe ake sasiyana ndi maikidwe a maliro ena onse, ndipo amameta nachita
zonse monga mwa miyambo ya Achewa. Pomalizira penipeni amatulukanso
pamtanda.

Maliro a munthu wopsa ndi moto

Moto ndi chipangizo chabwino cha mabanja onse a dziko lapansi. Komanso zoipa
zake za moto ndi zosasimbika. Achewa amakonda kutentha tchire kuti aphemo
nyama mosavuta. Tchire limakhala ndi mwini amene amamemeza kuti tchirelo
litenthedwe patsiku lakutilakuti. Patsiku lonenedwalo anthu amasamala
kulongosola mwambo wopatukana m’banja pogona monga momwe amachitira
uzimba, monga tawerenga ponena za munthu wolasidwa kuuzimba.

Amauziratu anthu tsikulo lisanafike kuti amene ali ndi kanthu kake m’chiremo,
monga mirimo yosiidwa, akachotse tsikulo lisanafike. Patsiku lonenedwalo
amafika onse kudzatentha tchire. Amakhala mbali ndi mbali namayembekezera
kumene nyamazo zingatulukire kuti aziphe. Mwiniyo amauza mwana wake
woyamba ndi mkazi kuti asatuluke m’nyumbamo mpaka tchirelo litatha kupsa.
Amatero kuti nyamazo zisatulukirenso. Akutentha, nyama zimatuluka m’tchiremo
uku ndi uko kuthawa moto. Anthu okhalirawo amaziletsa nazipha kunja kwa
tchire.

Koma mwina nyama ina imalasidwa ndipo ili pafupi kufa imalowanso m’tchiremo.
Koma wolasayo amalephera kupirira poganiza kuti nyamayo itsirizidwa ndi wina.

67
Ndipo Poona kuti mtima ukumuwawa amalowa patchirepo kuti akatsirize nyama
yolasidwayo. Koma nyamayo mwina imathawirabe kutali.

Nyamayo akaitsiriza, koma kuti abwerere komwe anachoka amaona kuti moto
wagundika kwambiri. Amayesayesa kuthawira uku ndi uko ndi kufuula kwambiri
koma motowo umabwerabe. Pofuna chipulumutso amachipeza mumtengo
nakwera, koma popeza moto umalirima kwambiri, malawi ake amakwera
m’mwamba kwambiri. Munthuyo amapsera momwemo, ndipo amafika anthu
nadzatenga mtembo wake kuti akaike m’manda. Apa pamakhalanso mlandu ndi
mwini tchire nati, “Inu mudatiitanira nkhondo kuti ife tidzapsere m’tchire lanu.”
Choncho mwini tchire amapereka dipo kwa eni munthu wakupsayo. Dipo lake
nthawi zambiri imakhala tchirelo.

Munthu wodzipha yekha


Anthu odzipha amapezeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi. Chifukwa
chodziphera ena ndi mavuto a m’banja, kukwiya kwa nthawi zonse kapena
manyazi pochita choipa china chimene chimachititsa manyazi. Makamaka anthu
odzipha okha ndiwo amakhalidwe osachedwa kukwiya m’mitima mwawo.
Angakhale m’Buku Lopatulika timapeza kuti Yudasi Isikalioti amene adapereka
Ambuye Yesu Khristu adadzipha yekha poganiza kuti adachimwa pakupereka
mwana wa Mulungu.

Ndipo pofuna kutsata bwino imfa yodziphayi tiyeni tiyese kulondola zitsanzo zina
zimene zimachitika kuti munthuyo adziphe. M’banja mwina mkazi amakhala
wolongolola kwambiri. Mnyamata poyamba kukhala m’banja sadziwa mavuto a
banja ndipo pamene mkazi alongolola iye amakhala ngati kapolo wopanda ufulu
weniweni. Pofunafuna chochita chimasowa nayamba kufuna njira yoti angathe
kuzipulumutsa kumavutowo.

Mosachedwa amapita kwa bambo, kapena amalume ake nati, “Ine ndapeza mavuto
pabanja langa mkazi ndiwolongolola, tsono ndimafuna kuti ndimuleke.” Koma
nthawi zina iwowa amamukakamiza, ngakhale iyeyo mumtima mwake sapeza
bwino. Nthawi zonse amakhala wosasangalala nafunafuna njira yothawira
mavutowo. Atalingaliralingalira mwanjira yausatana iye amapeza kuti kuli bwino
angofa. Mobisa, msanga amakwera mumtengo nadzikoleka m’chingwe pakhosi
nafa.

Nthawi zina anthu a m’mudzi amalondola masiku ambiri koma osamupeza.


Mwamwayi munthu wina amachita ngati akungoyenda ndipo mwadzidzidzi

68
amaona mtembowo uli lende m’mwamba. Mofulumira amafuula nati, “Tengani
mphasazo, munthu uja anadzikweza ali pano!” Anthuwo amatenga mphasa napita
nakanyamula mtembo. Anansi ake a munthu wakufayo amati, “Tiyeni tilondole
chifukwa chake chodziphera.” Motero amaitana mkaziyo namufunsa nati, “Kodi
m’banjamu munali ndewu patsiku lija wasowa mwamunayu?” ndipo mkazi
amanena chidachitika m’banja panthawiyo, koma mwina amayesa kubisa kuti
mlandu ungamuvute. Atabisa motero anansi a munthuyo amaulula kuti,
“Munthuyo patsiku lakutilakuti iye adadza kwathu natiuza zakutizakuti.” Ndipo
zikatero pamakhala mlandu.

Maliro a chitsiru

Uchitsiru uli wamitundu ingapo, wina ndiwo wakuti amayankhula zosamveka


bwino ndipo iye mwini sakumva zonena anzake, ndipo wina ndiwo uchitsiru
womangoseka nthawi zonse. Munthu wotere kumupatsa chovala salandira konse.
Anthu otere si kuti amapezeka pakati pa Achewa okha, komanso pakati pa mitundu
yina ya dziko lapansi. Nthendayi mayambidwe ake sitidziwa, kapena munthu
amangobadwa nawo uchitsiruwo, koma za ichi sitidziwitsitsa.

Uchitsiru wina ndiwo woti chitsirucho chimagwira ntchito bwinobwino ndi kuvala
bwinobwino, koma chimangoseka popanda choseketsa chenicheni. Ngati makolo
amuuza mwambo ndi zina, iye sazimvera konse. Koma ngati ndi mkazi, amuna
safuna kumukwatira podziwa kuti chitsiru sichimva ndi kugwira ntchito
molongosoka. Namwaliyo amakula koma uchitsiru sumamuthera.

Chitsiru chotere chikamwalira anthu amaika bwino monga mwamaikidwe a


Achewa naliranso, koma savinirapo nyawu monga amachitira pamaliro ena onse.

Uchitsiru wina ndiwo uja wakuti ‘umunthu’ umasowa, samavala ndiponso ntchito
sagwira konse. Makolo akalandira mwana wotere m’banja, amamulera monga
mwamaleredwe a Achewa. Koma uchitsiruwo umadziwika pamene mwanayo
wakula.

Mwana atakula uchitsiruwo umayamba kudziwika. Ngakhale makolo amayesetsa


kumuveka chovalacho, koma iye amavulanso. Munthu wa uchitsiru wotere
amachita zosalongosoka ponse ngati wamisala. Maonekedwe ake amadziwika ndi
kutuwa ngati kaphulika, chifukwa sasamalira pokhala. Chitsirucho chikakhala
chachimuna sichifuna kukwatira konse. Poyenda amayenda osasamala za kuvala
konse. Amayenda ulendo wautali napyola midzi yambiri koma sachita manyazi ndi

69
umaliseche wake. Anthu amene amakumana naye amangoseka koma iye
osalabadira konse.

Chitsiru chotere chikamwalira, anthu amadziwitsana kuti chitsiru chija


chamwalira, ndipo sabuma konse ndi kumva chisoni kwambiri pa maliro otere,
koma mwina makolo ake okha amalira.

Mdulo

Mdulo ndiyo nthenda ija yamapapo, ndipo wodwala amasanza magazi kapena
kutsokomola magazi. Koma makolo athu amati nthendayi ndi mdulo ndipo
matengedwe ake ndi aja ndalongosola m’mitu yoyambayi. Gwero lake amati ngati
makolo salinda mwana pamene iye wapita ku ulendo, mwanayo amatenga
nthendayi. Izi ndizo zimene makolo athu ankakhulupirira.

Mayambidwe ake a nthendayi chimayamba ndi chifuwa ndipo munthu


amatsokomola namalavula magazi. Pakapita nthawi mimba yake imauma. Koma
ngati wodwalayo ndi mwana wa banja lina, makolowo amadana kwambiri, kotero
mawu amatuluka kuti, “Bambo mwandidulira mwana.” Makolowo amayesayesa
kufuna sing’anga wodziwa mankhwala ophika. Atampeza amamphikira mwanayo
kuti akhalenso bwino. Mankwalawo amaphikira pamodzi ndi nkhuku. Pamene zili
kuvuta motere anthu ena amaseka nati, “Banja la uje lidadziphera mwana wawo.”
Wodwalayo amakhala wovuta ndipo amafuna zinthu zambiri kotero angakhale
wodwazika matendawo sangamukwaniritse pazofuna zake.

Sing’anga wamakhwalayo amayetsetsa kuchiritsa wodwalayo, nthawi zina


amathadi kumuchiritsa. Pamenepa anthu ambiri amatama sing’angayu kwambiri
ngati iye ndiye Mulungu wokhoza kuchiritsadi munthu. Munthu wamankhwalayo
amafuna malipiro ake pamatenda wachiritsawo. Choyamba amati, “Mundipatse
chipondam’thengo, chifukwa ndasauka pofuna mankhwalawo m’thengo,
polasidwa ndi minga ndiponso kusauka ndi kukumba.”Akapatsidwa amatinso,
“Ndifuna kuti mundisudzule kuti ndimete wodwalayu.” Ndipo makolo akapeza
chumacho, sing’angayo amalandira mokondwera, kenaka amatenga lumo nameta
wochizidwayo napita kwawo.

Koma popeza kuti nthendayi ndi yochokera kumapapo, mwina mankhwala


amalephera. Ndipo sing’anga pofuna kukhulupiritsa anthu amati, “Koma mdulo
unapeza malo ambiri m’chifuwamo.” Mwachimenechi wodwalayo amamwalira.
Anansi amalira napenya makolo a mwanayo kuti sadalongosole bwino miyambo.

70
Maliro a mkamwini

Mkamwini ndiye munthu kapena mnyamata wodzakwatira pamudzi wina umene


suuli wake. Dzinali limatanthauza kuti munthuyo si wa m’mudzimo, koma ndi wa
eni ake a mudzi wina.

Mkamwini kale adali wa zaka zambiri zopitirira 18, koma lero alipo akamwini
azaka 14, ndiponso mkazi wa zaka zocheperapo. Banjalo limachitidwa
mwachibwana ngati zamasewera basi. Kudzakhala bwino ngati ichi chidzakonzeka
m’tsogolo muno.

Mabweredwe a mkamwini ndi osiyanasiyana. Pamudzi pakapezeka mbeta,


amabwera ofunsira mbetayo nati, “Ine ndili ndi chipsolopsolo chatambala ndipo
ndifuna msoti,” Ndiko kunena kuti, “Ndili ndi mnyamata wofuna mbeta.” Mwiniyo
amafunsa kuti, “Kodi msotiwo mwaupeza kuno kaya kwina?” Wofunayo amati,
“Msotiwo uli ndi inu.” Atavomerezana amaperekeza mbetayo monga
ndafotokozera kale pa maliro a namwali.

Patsiku loperekeza mwamuna, akuchimuna amakonzeratu kutenga chiongo


chonenedwa ndi akuchikazi chomwe chikhoza kukhala mbuzi imodzi kaya
zingapo. Ndiponso chamlomo chimakhala thadzi lankhuku. Chamlomo
akuchimuna amapereka kwa nkhoswe yakuchikazi pa ntchito yokambirana ndi
akuchimunawo, pozindikira kuti ndi ntchito yaikulu ndi dipo lomwe. Atapereka
zonsezi amathokoza nati, “Zikomo, wanuyu tamulandira koma mum’dziwitse kuti
sitifuna bodza, ulesi ndi zina.” Nauzidwanso kuti, “Amake auje ndi apongozi anu;
auje ndi akazi anu aakulu.” Namaliza zonsezo.

Kukacha m’mawa, mnyamatayo amafunsa komwe kuli munda wa banjalo.


Atauzidwa, tsiku lina m’mawa kwambiri amapita kumundako, nayamba kulima.
Iye amalima mpaka masana, pamenepa apongozi amauza mlamu wake kuti
akamuuze kuti tsopano abwerere kumudzi. Mnyamatayo amachita manyazi kupita
kumudzi msanga, ndipo amangolimabe mpaka apongoziwo atamupatsa nkhuku
yomuchotsera pamundapo. Nthawi zonse mkamwini amagwira ntchito
yachikamwini koposa momwe amagwirira kwawo.

Nthawi yoyamba mkamwiniyo sadya kwambiri. Tsiku loyamba nthongo zitatu


nati, “Ndakhuta.” Pa nthawiyi mkamwiniyo ayenera kuleka chakudyacho ngakhale
ndiwo zake zikhale nyama. M’mawa mwake nthongo zisanu, tsiku lina amadya
nthongo khumi, ndipo akakhalitsa amatha chakudya chonse chimene chapatsidwa

71
kwa iye. Ichi chidali ngati chikhalidwe chawo cha Achewa kuti iye asayambe
kuonetsa kudya kwambiri.

Patsiku loti iye wadwala, amithenga amapita kwawo msanga kukawadziwitsa


anthu kuti mnyamatayo akudwala. Koma atamwalira amafika achinansi, ndipo
malirowo amanyamulidwa. Zochitika zonse zimakachitikira kwawo.

Mkaziyo amametedwa nauzidwa kukwatiwa ndi wina ngati angafune


kukwatiwanso.

Maliro a nankungwi

Namkungwi ndiye mulangizi wachikazi, koma machitidwe ake asiyana m’zambiri


ndi mlangizi wa Chikhirisitu.

Mfumu ikagula mzinda kuti izimeta anamwali, iyo imafuna namkungwi wake woti
azidzalangiza anamwali a pamudzipo. Mfumu imasankha mwana wa mlongo
wake, wamkazi, kuti akhale mfumukazi wake.

Ntchito yake imachitika makamaka panthawi yachinamwali, ndiyo kulangiza


anamwali mmene amayenera kudzakhalira m’banja mwawo. Koma dziwani kuti
nthawi zina amayamba kulowana m’maukwati awo mpaka zaka, kapena chaka
chimodzi. Nthawiyi amadikira kuti mtsikanayo athe msinkhu. Ndipo atatha
msinkhuwo ndipamene amachita chinamwali.

Nthawi yoshambula mowa wachinamwali amuna amafika ndi Njovu. Panthawi


yausiku iye ndi anamwali amapita kumene Njovuyo yagona, ndipo amatengako
chitamba ndi phulusa la pa dambwe napatsa mfumu. Mfumu imakasakaniza izi
pamodzi ndi mankhwala ena. Atakonzeka mankhwalawo amatchedwa
‘khundabwi’ amene amapatsidwa kwa anamwali kuti amwe. Mtulangala
(chabwalo) mfumu imapatsanso namkungwi, wakunjira ndi nduna yake kuti amwe.
Mkazi aliyense saloledwa kulangiza namwali koma iye yekha.

72
Kasiya maliro

Panthawi yomwalira iyeyo, mfumu ndi anthu ake onse amamva chisoni ndipo
amatsuka nabuma. Akukumba manda amuna ena amachita nyawu ina yotchedwa
“Kasiyamaliro”. Nyawuyi imapita kumudzi nikavina. Akazi amakondwera ngati
tsiku laukwati chifukwa cha nyawuyo. Koma ena amamva chisoni kwambiri
podziwa kuti mlangizi wawo wapita. Ataika maliro, madzulo nyawu yotchedwa
Kachipapa, imafika naimba nati, “Wapita namkungwi e-e! Talire bwanji maliro.
Wapita namkungwi e-e. Talire bwanji maliro.” Akaziwo amatsira mavume ake,
ndipo amaimba mwina usiku wonse mpaka kucha. Atatero amapita kwawo.
Patsiku lometa mpalo pamafika Njovu ndi Jere, ndipo mfumu imawaza Njovuyo
mankhwala aja a ‘khundabwi’. Powaza mankhwalawo mkazi wa mfumu
amakhalanso pomwepo.

Itakapuma Njovu, mfumu imatenga mbiya yamowa ndi kupatsa Njovuyo kuti
ikamwe. Patsiku lopita kwawo Njovu, mfumu imayenera kupereka mbuzi. Patsiku
lampalo pamafika zinyawu izi: Simoni, Kachipapa, Chabwera ndi Pedegu ndi
kuvina nthawi yamasana.

Wakunjira

Kunyawu kumakhala atsogoleri ambiri, wina ndi Wakunjira. Uyu ndiye wamkulu
wolamulira gule yense ndi zovuta zina. Pamakhalanso ena, ndiwo atsabwalo; awa
ntchito yawo ndi kubwereka ng’oma zoimbira nyawuzo, kusesa ndi kulambula
pabwalo la nyawu ndipo kuyang’anira zonse zochitika pabwalopo kuti zonse
ziyende molongosoka bwino.

73
Pedegu

Udindowu, wa wakunjira, mfumu imapatsa mphwake, mwana wamwamuna wa


mlongo wake, amene amayembekezeka kudzakhala mfumu pamene mfumuyo
imwalira. Ndipo ntchito yake imafanana ndi ija ya namkungwi.

M’mudzimo mukakhala maliro pamene mwini malirowo afuna kuti pavinidwe


nyawu, amapita kwa wakunjira nati, “Zikomo,” ndipo iye amavomera nafunsa kuti,
“Kodi wachita kubwera kachimawamawa n’kwabwino?” Ndipo mwini malirowo
amati, “Inde kuli bwino, koma chobwerera ndi chakuti ine sindindagone bwino
usiku walero, azimu andichezetsa. Azimuwo akuti bwanji inu makolo
mudangonditaya ngati galu osandivinira nyawu pamaliro anga? Koma ngati
simuvina nyawu pamaliropo, mmodzi mwa inu amwalira ndithu.”

Mawuwa amayerekeza kuti wakufayo adafika usikuwo ndi kuyankhula m’kulota.


Amanena kuti mizimu ya anthu omwe adafa kale imafika usiku kudzayankhula ndi
anthu osiidwawo, ndipo imatha kudziwitsa tsoka limene likudza kwa iwo
kapenanso mwayi. Pakati pa Achewa mwambo wakuti munthu akalota tsoka
kapena mwayi amafotokoza malotowo kwa ena ndipo amayesa kumasulira
malotowo mosiyanasiyana; mwina amati ali ndi mwayi mwinanso amati tsoka;
mwina milandu idzakufika mosachedwa. Atamva izi wolotayo amakhala
wosasangalala ngati malotowo amulozera kumilandu, imfa, tsoka ndi zina
zomumvetsa chisoni.

Atamva wakunjirayo amapita nazo izi kwa mfumu nati, “Auje afuna kuti tivine
nyawu pamaliro awo aja.” Ndipo mfumu imati, “Chabwino ngati ali ndi mphoto

74
zofuna nyawuzo mutha kuuza ana kuti akamemeze gule pamidzi yozungulira.
Wakunjira amaitana anyamata onse kuwauza kuti, ‘Pamudzi pano padzakhala gule
mawa, ndipo inu anayi pitani mulengeze gule pamidzi yozungulira.” Nauzanso ena
a iwo kuti akayendere gule, ndiko kuti akasende luzi ndi kutema chabzero ndi
udzu, ndiponso kukaona m’midzi mmene muli makoko, m’nkhuti ndi m’madzala.
Atayendera, amapita kukaba gule ndi makoko, amapita pakati pausiku anthu
atagona. M’mamawa wakunjira ndi anyamata amalawirira ku dambwe. Ndipo iye
amaona kuti zonse zilipo; koma ngati alipo yemwe anakana kukaba guleyo, uyu
amapirikitsidwa ku dambweko, ndipo amafikanso ndi nkhuku ngati afunanso.
Nthawi yam’mawayo kumamveka, “Ho! Tate waye! Aliko gule.” Uyu ndiye
Kapoli, nyawu ina. Atamva ichi akazi onse amakondwera kwambiri podziwa kuti
lero tidzaimba nyimbo zathu zoimbira nyawu, usiku.

Kapoli

Kapoliyo amangofuula tsiku lonse kuti anthu opita m’njira yapafupi adziwe kuti
kumeneko kuli nyawu. Kumanga nyawu yonse ndi ntchito yakalavulagaga ndipo
mwina imatha nthawi yaitali, koma chifukwa cha kuchuluka anthu, mwina imatha
masana. Si mudzi umodzi umene umachita nyawu, komanso midzi yozungulira.

Wakunjira amalandiranso anyamata obwera tsopano ku dambweko, nawauza


mmene zonse zimachitira ndi mayankho a mafunso. Koma ngati kuli milandu
komweko iye ndiye amatha zonsezi. Iye amakhala ngati khutu ndi pakamwa pa
mfumu, amauza anyamata zofuna za mfumu. Pometa maliro pamafika mowa ndipo
iye amaugawa kwa onse. Popita ndi nyawu kumudzi amatsogolera ndi iyeyu
namatukwana akazi kuti aziopa nyawuzo nathawire m’nyumba.

75
Maliro ake a wakunjira amaikidwa mwaulemu monga a namkungwi.

Maliro a nduna ya mfumu

Pamaliro anduna, mfumu imauza madoda am’mudzi kutsuka malirowo, ndipo


akatsuka mfumu imayamba kulira kopambana, onse amaliranso podziwa kuti
mtetezi wawo wafa, tsopano asowa wowateteza.

Popita kumanda amuna amayesa muyeso wamtembo kuti akalinganize bwino malo
oyenera kukumbidwawo ndipo onse amapita kumanda. Akafika uko ndipo
asanayambe kukumba, amafika wina ali mchenje, mphondo yamankhwala
yopatsidwa ndi mfumu nati, “Mfumu ikuti tilembe pamene tifuna kukumba ndi
mankhwala kuti tisapeze zovuta zina pokumba, monga miyala ndi zina zotere.”
Akachita izi, amayamba kukumba mandawo.

Mdondo

Ali kumandako amachitanso nyawu, ‘Kasiyamaliro’ ndi ‘Kachipapa’,


namakasewera ndi akazi kumudzi. Ichi n’chifukwa chakuti mwana asapite
kumandako amene ali wosalowa nyawu kuti asaone nyawuzo. Poika maliro amaika
ng’oma zikuimbidwa, nyawuzo zikuvina, mpaka atatha kukwirira mtembo. Usiku
amavinanso nyawu mpaka tsiku lotuluka pamtanda. Akameta tsitsi loyamba
amatuluka.

Panthawi yampalo pamafika Mdondo, Jere ndi Kasiyamaliro ndipo akazi amaimba
nyimbo zawo nati, “Nyamayo de! Dede! Aye! Nyama mdondo!” Amaimba
motsirirana mavume. Nyimbo ina amati, “Ana amuna n’chilombo adakatenga
nyama kuthengo. O Dede! Aye! Odede aye!” Mdondo ndiyo nyawu yaitali
yokhala, imakhala ndi anthu asanu ndi anayi kapena khumi m’kati mwake monga
sitima.

Zitapita izi zimafika zina zija zovina masana zomwe ndi Kachipapa, Simoni,
Chabwerakumanda ndi zina. Zitafika zimayamba kupereka kasitomu; kugula

76
bwalo kwa wakunjira uja, ndipo iye ndi mfumu amagawana. M’mawa Mdondo
umavinanso nufupidwa mbuzi ndi mphasa.

Maliro a mfumu ya mzinda

Mfumu ndiye mkulu wa mudzi, amene amayang’anira zochitika m’mudzimo.


Mzinda ndicho chinthu mfumu imagula kuti izimeta anamwali m’mudzimo.

Mfumu ikamwalira, mudzi onse anthu amamva chisoni, komanso mudzi


umagwedezeka, mitu ya anthu imazungulira. Mfumu ikadwala mosazengereza,
nduna kapena kazembe amadziwitsidwa. Atafika munyumbamo amafunsa nati,
‘Ndili chikhalire kunyumbaku ndangoona akazi anuwa akundigundira chitseko.
N’tawalonjera ndidawafunsa kuti, “N’kwabwino?” Pondiyankha anati,
“N’kwabwino pang’ono, amfumu Ovungula sadagone bwino, usiku onse kubuula
ndi kuyankhulayankhula. Ndiye ndangoimirira kumathamagira kunoku. Kodi
chavuta n’chiyani?” “Sindidagone lero, pa mtimapa pakutentha, m’mimbamu
mukupota ndipo mtimawu uli kwanguchokamo.” Ndiye ndunayo imati, ‘Ha!
Pepani mavuto amenewo.’

Ndipo mfumuyo ikamwalira, wakunjira amasonkhanitsa anyamata onse


n’kuyamba kutumiza mauthenga kumidzi yozungulira. Anthu amauzidwa tsiku
loika maliro. Ponena maliro zimatere: ‘Odi!’ Amfumu amayankha motere monga:
‘Yee, monitu. Nanga n’kwabwino kapena ayi n’koipa?’ ‘Opingeni watisiya, ndiye
maliro ndiwoika mawa.’ ‘Chabwino tamva.’ Nthawi yomweyo mfumu imauza
nduna kuti idziwitse anthu onse za uthenga wa malirowo. Kutacha anthu onse
amasonkhana pabwalo kudikira mfumu kuti awatsogolere kupita ku maliro
kuja.Mfumu itafika pamalopo ulendo wopita kumaliroko umayambika; patsogolo
mfumu pa mbuyo pa mfumu nduna, pa mbuyo pa nduna madoda, pambuyo pa
madoda anyamata.

Atayandikira pasiwapo mfumu imayamba kulira n’kutsatana ndi nduna, madoda


ndiposo anyamata, ndiyetu buuu… Atatha amakhala pamalo pamene pasonkhana
eni mudzi paja. Mfumu, mwini mudzi amalonjera akunjira aja motere, ‘Hi!
Mwamva kodi?’ ‘Inde.’ ‘Yayi, Chauta watigwera. Komatu imfayi ndi yadzidzidzi,
sitidazonde konse matenda. Matenda ake adawayambira kumunda polima. Ndiye
tidagoona kuti Ophiri, Opingeni si moyo. Titafika kuti tizazonde tidapeza
akutsendera moyo, ndizimene taona kuno.’

Ufumu wa Achewa

77
Mfumu itafa, panthawi yometa malirowo anthu amapangana kulonga mfumu ina.
Patsikuli amasonkhana anyakwawa, madoda, amayi, atsikana ndi anyamata.
Anyakwawa amafunsa amayi nati, ‘Mukuganiza kuti pamudzi pano amene angathe
kusunga anthu bwino ndani?’ Ndipo amayi amanena munthu amene angathe
kusunga mudzi, natchula monga ‘Kalichero’.

Atamwa mowa amatsonkhana munyumba imodzi. Mwadzidzidzi


woyembekezerayo amagwiridwa, ndipo amafuula nati, ‘Kathewerawe!
Kathewerawe!’ nafuula kopambana. Panthawiyi amatchula dzina la mfumu
yomwalirayo, monga Kathewera indali mfumu yomwe idasunga mudziwo
poyamba. Mfumu yasopanoyo imayesa kukana ndi kulimbalimba, koma anthuwo
amamuumirizabe ndipo ena amamumenya mapama.

Kalicheroyo amayesa kukana mwina poopa abale ake kuti angamuphe chifukwa
cha ufumu. Dziwani kuti ufumu wa Achewa amalonga mphwake wa mfumu,
yemwe ali mwana wa mlongo wa mfumu, osati mwana kapena m’bale wake
monga imachitira mitundu ina. Akatero amayamba kuyimba nati, ‘Ponda, ye, ye,
ponda. Ponda, ye, ye, ponda.’

Atatha izi amayamba kulanga nati, ‘Lero mwakula, zachibwana lekani. Ngati
munali kuba, kuchita chigololo, kusewera ndi ana ndi zina zotere zonse muleke
lero.’ Mmenemo amayi akuombera m’manja, kuvomereza mawu onenedwawo kuti
ndioona ndiposo okhulupirika. Mfumuyi imauzidwa zonse zamasungidwe ena a
mudzi, monga kutsirika mudziwo kuti zilombo zisamafikemo. Ndipo anthu
amauzidwa kuti palibe mmodzi azati, ‘Kalichero,’ koma aliyense anene kuti,
‘Amfumu,’ kapena ‘Akathewera.’

Tsono mfumu yasopanoyi ngati ikufuna kuti pamudzipo pakhale muzinda poti
izimetera anamwali, imapita kwa mfumu yomwe imagulitsa mankhwala. Atagula
amafika kumudzi, natenga mankhwalawo pamodzi ndi mafuwa amene amayiwo
amayambira kuika pamowa wachinamwali.

Panali zinamwali zambiri pakati pa Achewa. China n’choti, namwali akadumwa,


mwadzidzidzi mfumu imauzidwa ndi namkungwi kuti namwali uja ali ndi pakati.
Mfumu imamva chisoni pozindikira kuti namwaliyo wamudula, ndipo azafa
msanga. Mlandu utakambidwa, mwini mkazi amapereke tonde wa mbuzi. Mbuzi
itaperekedwa, mfumu imauza namkungwi wake kuti avinire namwaliyo.

78
Tsiku lina amasonkhana anamkungwi ndi amayi a midzi yoyandikana kudzavina
chinamwali. Dzina lachinamwali chotere amachicha ‘Chimbwinda’; ndiko kuti ali
ndi pakati chinamwali asanachite.
Amayi amasonkhana kunyumba kwa namwaliyo, nayamba kumvula zovala zonse
ndi kumulola kuvala m’chiuno mokha. Panthawiyi mimba yonse ili poyera.
Amachita ichi kuti mfumu ndi ena onse aone mimbayo. Atatero namwaliyo
amatengedwa napita naye ku mtengo wa anamwali kuti akam’vinire.

Patsikuli amasonkhana anthu ambirimbiri. Mfumu imalamula kupha tonde uja,


ndikutenga magazi ake pamodzi ndi mankhwala aja nathira m’njira yonse imene
namwaliyo adzapitamo. Ndipo ana, amayi ndi namwaliyo amaponda pamwazipo,
koma mfumu yokha siimadya chakudya cha pachimbwinda.

Mfumuyo podwala, nduna zake pamodzi ndi amayi amapita kwa woombeza ula.
Atafika waulayo amati, ‘Moni nonse. Nanga mwasiya kwa bwino ku mudzi?’
Amayankha nati, ‘Ife tasiya matenda, ndipo tatsata inu kuti mutidziwitse chimene
mfumuyo yadwalira.’

Waula amapita pamene zipangizo zake zimakhala, nazitenga nayamba kuombeza.


Ndipo amati, ‘Mtengowo. Mtengowo. Kodi ndi nyanga? Tandiuza mtengo.’ Koma
akunjirawo ngati saomba m’manja, iye amaziwa kuti si nyanga. Nayambanso
kuyankhula kuti, ‘Mtengo tandiuza, kaya ndi mzimu wa mfumu ya kale, kaya ndi
chiyani?’ Samanenanso kanthu mpaka ataomba m’manja. Koma ngati ndi chidani
chimene mfumuyo ndi mnyamata wapamudzipo adatengana tsiku lina, akunjirawo
amavomereza poomba m’manja. Ndipo waulayo amaleka nati, ‘Tafootokozani
mmene chidanicho chidadzera.’ Atafotokoza akunjirawo, iye amati, ‘Mdaniyo
adawachitira mankhwala, ndipo mankhwalawo ali pakhomo lorowera.’

Zitamva izi, ndunazo, zimapita kumudzi nafotokoza zonse ndi kuti ula wagwira
uje. ‘Akuti adaika mankhwala pa khomo, ndipo ngati mankhwalawo sachotsedwa
mfumuyi ifa.’ Amafunafuna mankhwalawo koma osawapeza. Kwa iye amene ula
wam’gwera amakhala ndi nkhawa poziwa kuti ali ndi mlamndu ngati mfumu
yamwalira. Koma amachitanso mantha kutsutsa waulayo. Aula amanena zambiri
koma zosachitika; mwina amati mukapeza wodwalayo atamwalira, koma mwina
amamupeza wamoyo nachira.

Itakhalanso bwino mfumuyo, anthu onse amasangalala, koma mfumuyo imadana


kwambiri ndi munthu amene uja ula udam’gwera, naligalira kuti munthuyo ndi
mfiti.

79
Nthawi zonse mkazi akatha msinku, kuyambira pamenepo amathawana ndi mfumu
mpaka tsiku lachinamwali chake. Koma muja amati masiku sakoma onse,
mwadzidzidzi mfumuyo imatupa miyendo ndipo anthu amaganiza kuti mnyamata
amene adachita chimbwinda chija ndi amene adula mfumu. Nduna ya m’mudzi
imatuma anyamata okanena kwa mfumu imene idali nkhonswe ya mfumu polonga
mfumuyo ndiponso kwa mafumu ena onse.

Patsiku lakuti matendawo akula, akazi saloledwa kusinja m’mudzimo. Mobisika


kumamveka kuti mfumuyo yamwalira, anthu amachotsa katundu yense
m’mudzimo pamodzi ndi ana omwe, nakawaika kumizi yozungulira.
Mwamsanga nduna imasonkhanitsa nkhuku zokanenera maliro kwa mafumu ena,
ndipo anyamata amapita nakanena za malirowo. Atasonkhana mafumu onsewa,
amasonkhanitsa ng’oma zamtundu wa ndewere, mpanje, mtiwiso, gunda ndi
mbandambanda. Akaimbaimba, mafumu onse amavina mnjedza. Ena onse
saloledwa kuvina nawo koma mafumu okhaokha. Akatero onse amabuma
kwambiri mwachisoni.

Anthu ali kumanda, amafika mafumu a midzi ina ndi anyamata awo nachita
mputho, ndiko kuti atha kupha munthu aliyense am’peze, ndiponso zoweta
zilizonse popeza amapha chilichonse chimene akumana nacho, kotero anthu ambiri
amathawa. Ichi ndicho chifukwa chake katundu pamodzi ndi ana amachotsedwa,
kuopetsa mpunthowo. Ophedwawo amakhala mtsamiro wa mfumu. Zikuchitika
zimenezi nyawunso zimakhala zili lakalaka uku ndi uko. Ndipo akazi amakhala
otanganidwa kwambiri kuononga zinthu za mfumu yomwalirayo, monga
chimanga, chuma cham’nyumbamo, ndi zina zilizonse zopezeka m’nyumbamo.

Poika malirowo mwina amaika patapita masiku awiri, kuti amuna athe ku kumba
manda akuya kwambiri. Mtembo umanyamulidwa ndi nyawu izi:
Chabwerachaona, Ngangande, Njovu ndi Jere. Akazi samaonera maikidwe amaliro
amfumu. Katundu wina wam’nyumba amaikidwa pamodzi ndi ophedwa awiri
kapena anayi aja. Koma namwali okongora amaikidwa wa moyo kuti afukate
mfumu pa miyendo yake. Namwaliriyo amalira kufuna kutuluka koma kosatheka
kutero, amakwiridwa m’manda. Ndipo namwaliyo amamwalira polephera kupuma.

Nyau zimayamba tsiku lomwelo kuvina mpaka tsiku lotuluka pamtanda. Mfumuyo
ikamwalira akazi ake onse amatchedwa ‘aferekazi’, kutanthauza kuti anafedwa
aakazi. Akaziwo pamodzi ndi ana amathira dothi m’mandamo, chidzindikiro
chotsadzikana. Amatero kuopa mzimu wa wakufayo kuti ungadzafike ndikuvutitsa
abale, akazi ndi ana ake.

80
Atatuluka pamtanda, aferekazi amasambitsidwa nametedwa koyamba. Ndipo
zikatha izi aferekaziwo saloledwa kusamba thupi lonse, koma m’manja mokha
mpaka pa tsiku lometa kachiwiri; patapita zaka ziwiri. Chaka choyamba
mafumuwo amaphikitsa mowa kuti aone adzukulu ndi aferekaziwo. Panthawiyi
amasonkhana anthu ndi nyawu zochokera m’midzi yozungulira, navina masiku,
ndipo pa tsiku lotsiriza, aferekazi amaonana ndi adzukulu. Mowa umenewu
umatchedwa ‘sambiram’maso’. Ndiko kuti ayembekezanso mowa wina
wodzasambira thupi lonse ndi kumeta tsitsi lotsiriza.

Nthawi yapakatipo ena akalota maloto, m’mawa podzuka amasimbira ena


malotowo. Akaombeza, waula amati mizimu ifuna mowa ndi chisi; ndiko kuti
akaphike mowa ndiponso akaphe nyama nayiotcha kuti fungo lake limveke
m’mudzimo. Mwamsanga amachita izi podziwa kuti ngati satero mzimuwo utha
kuphapo munthu wina.

Akaphika mowawo amaitana mafumu, ndipo tsiku lomwa mowawo amalemekeza


mizimu. Akapha mbuzi natenga ziwindi ndi nyama ina pamodzi ndi mowa nautsira
pa mtengo kuti mizimu idye zimenezo. Podzuka m’mawa, amapeza nyerere ndi
zina zadya nyamayo, ndipo amakondwera kwambiri natenga yotsalayo nayipatsira
ana kuti adye zotsala, nayiotcha nadya.

Patsiku lometa maliro, patapita chaka, amafika mafumu ndi anthu ena. Ndipo
nyawu zimayamba kuvina tsiku lopola mowa kulekeza tsiku loshambula mowawo.
Patsiku loshambula pamafika nyawu zovina masana ndi usiku. Zilombo za masana
ndizo: Kadyankhanze, Simoni, Kachipapa, Chisambwe, Makanja, Pedegu, Njovu
ndi Jere. Zimenezi ndizo nyau zazikulu zomwe sizingafike pamaliro aliwonse,
koma pa chinamwali, maliro anamkungwi ndi maliro amfumu, basi.

Panthawiyi ngati pa mudzipo pali namwali amam’meta, angakhale ochokera


kumudzi wina. Koma ngati mfumuyo idali yopanda mzinda, maliro ake amasiyana
ndi a mfumu ya mzinda. Nyau zina zimafikapo, koma Njovu ndi zina zomwe
zimafika pa maliro a mfumu ya mzinda sizifikapo. Kusiyana pakati pa mfumu ya
mzinda ndi yopanda mzinda ndiko kuti, wopanda mzinda amatumiza anamwali
kwina.

Zitatha izi aferekazi amaloledwa kukasamba thupi lonse nametedwa. Asanachoke


amafunsidwa chipindatchika (chitsanzikano), ndipo aliyese amapereka mbuzi
imodzi. Koma ngati alipo wina wake, mphwake wa mfumu yomwalirayo, amane
afuna kulowa chokolo cha malume ake, wina amapita nati, ‘Auje afuna kulowa
chokolo kwa inu.’ Mayiyo mwina amakana nati, ‘Uje sindimufuna, koma uje.’

81
Ngati aferekazi ndi ambiri, amphwake a mfumu amalimbirana akaziwo. Ngati
mfumukazi yatengedwa ndi mphwake wa mfumu, uyu samapereka chipindatchika,
koma mphwake wamfumu, womutengayo.

Polonga mfumu yatsopano pamakhala kulimbirana amphwake a mfumu, wina nati,


‘Mfumu ndikhale ine,’ winanso natero. Ichi chimavuta opereka ufumu. Koma pali
ena amene amaopa ufiti, iwowa amakhala chete osalimbirana nawo.

Mfumu itagwidwa mkazi wake amayitanidwa nakhala pamodzi ndi mwamuna


wake. M’matanda kucha amalowa m’kuka muja nayiutsa mfumu n’kuyifunsa kuti
ifotokoze maloto. Amati, “Bambo, mwadzuka bwanji, nanga mwalota zotani?”
Mfumu imafotokoza maloto onse ndipo mafumu aja amatanthauzira malotowo.

Kukacha pakhomo polowera m’nyumba m’mene mfumuyo yagona amayikamo


nsengwa yoti aliyense wolowa kudzaona mfumu aziponyamo mkanda ndi
ndalama. Nsengwayo sayichotsa m’khomomo mpaka masana. Mowa
utashambulidwa m’nyumbamo amayikamo mtsuko wa mowa. Umayikidwa kuti
mafumu ena azimwa. Malo ena pamayikidwanso mowa wina wotchedwa
(chimzinda). Mowa ukakunthidwa mtsuko wina, kaya chikatiko chimaperekedwa
kwa adzukulu aja, ndi amene amadikira mowa uja.

Chikatiko china chimapumphulidwa n’kuchitumiza kudambwe. Kumene


kumatuluka Njovu ndi Mdondo ndi dambwe la mamfumu okhaokha. Anyamata
amakhalanso ndi dambwe lawo. Mnyamata atafuna kumakhala kudambwe la
mamfumu amachita kuperekanso nkhuku yopitirako. Nthawi itakwana kuti zinthu
ziyambe Kasiyamaliro amanyamuka ku dambwe lake kukatsogolera Njovu.

Mwadzidzidzi kumamveka chivomerezi ndi phokoso loopsa, Kasiyamaliro


patsogolo Njovu ndi Mnjere pakatikati pake. Nyimbo zili kuyimbidwa
m’mbuyomu ndi gulu la mfumu ndi bungwe la chiwoye. Oyimba n’kumati,
“Pang’onopang’ono, obambo de de pang’onopang’ono, obambo de de, obambo de
de, obambo de de.” Othirira n’kumati, “Yeee yeee-he”. Malo oyamba kukafikira
Njovu ndi onsewa ndi ku chitsime kuti akamwe madzi. Tsono kuoopa kuti madzi
angathe amapita ndi mbuzi ya tonde. Zikatero Njovu imanyamuka ulendo
wakubwalo. Itafika, ng’oma zimayimbidwa chiwoye chilli m’kati ndi nthungululu
zosanena. Ndiye Njovu imagona m’bwalomo. Ndipo itasupidwa imapita ku liunde.
Mosazengereza chikatiko cha mowa chimatumizidwa komweko kuti Njovu
ikamwe.

82
Patsogolo Kasiyamaliro ndi Mjere uja amabwerera kuti nawonso akavine
pawokha, ndiye nyimbo yake amadziyimbira namati, “Nyama?” Wothirira amati,
“Nyama yakwera mtunda, yasiya alenje.”

Zitatha izi wakunjira amagawira mowa ku madambwe onse mofanana. Atatha


kumwa tsopano zilombo zimayamba kusokoloka. Zilombo ndi monga Chadzunda,
Simoni, Kadyankhadze, Mbiyazodooka, Chinsabwe, Makanja, Pedegu, Kachipapa,
Mbaula, Kachibongwe, Maliya, Nyolonyo, Chimtabwa, Mapulanga, Chiudza,
Kadzombe, Nsanzazayenera Kamfiti, Kwakwase ndi Kang’wing’wi.

Makanja

Zilombozi zina zimadziyimbira zina amachita kuziyimbira. Povina zina zimavina


chimodzimodzi. Mafumu amawayazira mphasa m’bwalomo kuti akhalepo. Posupa
(kufupa) wosalowa saloledwa kuyandikira chilombo. Pamakhala munthu woliza
salamba, ndiye akaona kuti chavina mokwanira amachiyimbira salamba
yochotsera.

Chikamakanirira amati, “Kwawokwawo.” Koma chovina bwino amachiuza kuti,


“Bwalolo!” ndiye kuti, “Bwalo ndi lawo.” Masiku ano amati, “Ko! Ko! Ko!”

Mochedwa dzuwa likulowa, gule yense atavina amakhala mathero azonse, anthu
n’kumang’ondokana. Usiku wotsatira ndilo tsiku lamchezo. Usiku wonse
kumakhala kuchezera kuyimba mpaka kufikira mbembembe kucha.

M’matandakucha dzuwa lisanatuluke Njovu imavinanso ndipo imasupidwanso.


Poperekeza ku liunde mfumu yatsopano ija imaperekeza Njovu ija moitsogolera,
atayigwira chitamba. Kumadzulo mfumu yatsopano imatulutsidwa kuti ayilange.

83
Ng’ombe

Malo olangira mfumu yatsopano akakonzedwa anthu onse monga mafumu, ndoda,
ntchembere, asungwana ndiponso anyamata amadza kufupi ndi bwalo. Poyamba
wolowa kuka ndiye amautsa nati, “Timverane.” Onse n’kuvomera akuomba
m’manja kuti bo, bo, bo. “Ayi ndaimirachi n’kuti tsopano tilange mfumu yathu.
Ndiye pano tikhale omasuka kunenapo chomwe mudziwa pamakhalidwe a
mfumuyi, oipa kapena abwino.”

“Poyambirira, ayambe ndi mafumu ndipo ena titsirizira. Woyamba kutiyankhula


ndi mfumu uje. Akatha awa otiyankhulanso, komatu asanayankhule ayambe
kuyika ndalama m’mbale.” Ndiye zimayenda motere. ‘Ine amfumuwa ndidaona
kuti akamwa satheka konse ndiye lero muchepetse mkhalidwe umenewo. Mfumu
n’kudzala kotayira zinyalala, mukamva akukujedani, musamafunse m’malo mwake
muzitsokomola n’kumapitiriza ulendo wanu. Tsono ndisanachoke ndiyimbapo
nyimbo imene imati, “Mfumuwe, mfumuwe, mfumuwe, gwira mtimawu
mfumuwe, usagwire za ana mfumuwe”. Anthu amamasuka, ovinawo atachokamo
m’bwalomo mumalowa wina nati, “Ndiyimbapo yanga nyimbo.” Amayamba nati,
“M’manjamo m’manjamo. Mungakule, tingachepe, kanthu kali ndi mwini,”
n’kumayimba mobwerezabwereza. “Mawu anga ndi ongothokoza makhalidwe
amfumuyi, ayi pepani pitirizani khalidwe lomwe lija osamveramvera.”

Wina amaimiriranso moyimbapo nayimbapo nyimbo yake. Nyimboyo amati, “De


de nkhutukumve de de nkhutukumve, mawu oyipa umaleka.” Mawu anga ngakuti,
“Kuona maso ankhono n’kudekha. Khwangwala wamantha adafa ndi ukalamba.
Ichi chakoma, icho chakoma pusi adagwa n’chagada.”

Nyimbo inanso imati, “Mudzi ukamanga umakhala bwino ndi wana, ayee,
kuyankhula kuja udzaleke, ayee, mwakula lero mwakula.”

84
Mawu otsiriza

Abale sibwino kwenikweni kukhulupirira zaufiti kapena matsenga kuti zimenezi


zingathe kukudwalitsani kapena kukuphani.

Nthenda zambiri zimafika kwa munthu chifukwa chosowa ukhondo monga


kusasamba, kumwa madzi osaphitsa, kusavundikira zakudya zathu, kusakhala ndi
zimbudzi ndiponso ntchenche ndi zilombo zoluma ndi zina zosaoneka ndi maso.
Zimenezi ndizo adani athu. Masiku onse musachite nazo ubwenzi, ndizo mfiti
zimene zikufuna kutiranda moyo wathu nthawi zonse. Pitani ku chipatala pamene
mudwala, ndipo kumeneko mudzachira kosakayika, malinga ngati mufulumiza
kuuza dokotala zamatenda anu onse, bwinobwino.

Mdulo ndi miyambo ina yamakolo zilibe mphamvu ya kupha munthu.

M’dziko lino mudafika anthu amitundu yosiyanasiyana, ndiponso nthenda zina


zidafikanso ndi mitundu inayo. Mwaichi pitani ku chipatala kumene anzeru
adapeza magwero ndi machiritsidwe a nthenda zina. Mankhwala ena achikuda
alibe mphamvu yakupha tizilombo tating’onoting’ono tija.

Zikomo.

Mwini Mtunda
Dziko lidagawidwa motere;
1. Dziko(Area) ndi gawo loyang’aniridwa ndi Traditional Authority(Chief).
2. Mkati mwa dziko muli zigawo ndizo Mtunda. Mmenemu woyang’anira wake
amati Mwini Mtunda.
3. Palinso gawo lina ndilo Mudzi, ndipo woyang’anira wake amati Mfumu kapena
Nyakwawa (Village Headman). Ntchito yake ndikuyang’anira Nzika kapena
Mbadwa za m’mudzimo.Mfumuyi imapatsidwa malo ndi Mwini Mtunda.
Wopempha malo amatchedwa Mbiri, atawapeza a Mfumu amafunsindwa

85
cholinga chake, ndipo iye amati, ‘Palibe, ndilikufuna malo okhalapo.” Mwini
Mtunda amanyamuka nakam’lozera dela limene azakhalepo.

Nyumba zisanamangidwe pamachitika mwambo wake. Malowo amatsirikidwa ndi


mankhwala wochedwa Ntchiri, kuti mfiti ndi zilombo zisadzadutsepo.

Patafunika bwalo la nyawu Mwini Mtunda amafunsindwa. Potsiriza tsiku


lolambula bwalo Mwini Mtunda nakalozera malo woti alambule. Amatsirikanso
malowo, kuletsa ndewu ndi maphokoso. Mwini Mtunda amalandira cha Mtunda.
Atafuna mtengo wanamwali ampereka zonse zofunikira pa Mkangali. Mfumu
imadyetsedwa Khundambwi ndi Mchenje. Amadyera limodzi ndi namkungwi.

Pakaoneka maliro Mwini Mtunda amadziwitsidwa pompatsa nkhuku yonenera


malirowo. Panyengo ya masika Mbiri amayenera kupeleka cha Mtunda, mwina
madengu khumi a chimanga. Dzina la zoperekazi amati Mitulo. Ngati munthu
wamwalira pamafunikanso kupereka chidoola nthaka

86

You might also like